< 2 Chronicles 33 >

1 Manasseh was twelue yeere olde, when he beganne to reigne, and he reigned fiue and fiftie yeere in Ierusalem:
Manase anali wa zaka khumi ndi ziwiri pamene anakhala mfumu, ndipo analamulira mu Yerusalemu kwa zaka 55.
2 And he did euill in the sight of the Lord, like the abominations of the heathen, who the Lord had cast out before the children of Israel.
Iye anachita zoyipa pamaso pa Yehova, potsatira machitidwe a mitundu imene Yehova anayithamangitsa pamaso pa Aisraeli.
3 For he went backe and built the hie places, which Hezekiah his father had broken downe: and he set vp altars for Baalim, and made groues, and worshipped all the hoste of the heauen, and serued them.
Iyeyo anamanganso malo opembedzerapo mafano amene Hezekiya abambo ake anawaphwasula; anamanganso maguwa ansembe a Baala ndi kupanga mafano a Asera. Iye amagwadira zolengedwa zonse zamlengalenga ndi kumazipembedza.
4 Also he built altars in the house of the Lord, whereof the Lord had saide, In Ierusalem shall my Name be for euer.
Manase anamanga maguwa mʼNyumba ya Yehova, mʼmene Yehova ananena kuti, “Ine ndidzakhala mu Yerusalemu mpaka muyaya.”
5 And he built altars for all the hoste of the heauen in the two courtes of the house of the Lord.
Mʼmabwalo onse awiri a Nyumba ya Yehova anamangamo maguwa ansembe a zolengedwa zonse zamlengalenga.
6 And he caused his sonnes to passe through the fire in the valley of Ben-hinnom: he gaue him selfe to witchcraft and to charming and to sorcerie, and he vsed them that had familiar spirits, and soothsayers: hee did very much euill in the sight of the Lord to anger him.
Iye ankakapereka ana ake aamuna ngati nsembe yopsereza ku chigwa cha Hinomu, ankachita zamatsenga, kuwombeza ndi ufiti, ankakafunsira kwa woyankhula ndi mizimu ya anthu akufa. Iye anachita zoyipa zambiri pamaso pa Yehova, kumukwiyitsa Iyeyo.
7 He put also the carued image, which he had made, in the house of God: whereof God had said to Dauid and to Salomon his sonne, In this house and in Ierusalem, which I haue chosen before all the tribes of Israel, will I put my Name for euer,
Manase anatenga fano losema limene anapanga ndi kuliyika mʼNyumba ya Mulungu, zimene Mulungu ananena kwa Davide ndi kwa mwana wake Solomoni kuti, “Mʼnyumba ya Mulungu muno, mu Yerusalemu muno, malo amene ndawasankha pakati pa mafuko onse a Israeli, ndidzakhalamo mpaka muyaya.
8 Neither will I make the foote of Israel to remooue any more out of the lande which I haue appointed for your fathers, so that they take heede, and do all that I haue commanded them, according to the Lawe and statutes and iudgements by the hande of Moses.
Ine sindidzachotsanso phazi la Aisraeli kuchoka mʼdziko limene ndawapatsa makolo ako, ngatitu iwowa adzasamalira kuchita chilichonse chimene ndinawalamulira za malamulo onse, malangizo ndi miyambo imene inapatsidwa kudzera mwa Mose.”
9 So Manasseh made Iudah and the inhabitants of Ierusalem to erre, and to doe worse then the heathen, whome the Lord had destroyed before the children of Israel.
Koma Manase anasocheretsa anthu a ku Yuda ndi Yerusalemu, kotero anachita zoyipa zambiri kupambana mitundu imene Yehova anayiwononga pamaso pa Aisraeli.
10 And the Lord spake to Manasseh and to his people, but they would not regarde.
Yehova anayankhula kwa Manase ndi anthu ake, koma iwo sanasamaleko.
11 Wherefore the Lord brought vpon them the captaines of the hoste of the King of Asshur, which tooke Manasseh and put him in fetters, and bound him in chaines, and caryed him to Babel.
Kotero Yehova anawatumizira atsogoleri a ankhondo a ku Asiriya amene anagwira Manase ukapolo, anayika ngowe mʼmphuno mwake, namumanga ndi zingwe zamkuwa ndi kupita naye ku Babuloni.
12 And when he was in tribulation, he prayed to the Lord his God, and humbled him selfe greatly before the God of his fathers,
Ali pa mavuto akewo anafunafuna kuti Yehova Mulungu wake amukomere mtima ndipo anadzichepetsa kwakukulu pamaso pa Mulungu wa makolo ake.
13 And prayed vnto him: and God was entreated of him, and heard his prayer, and brought him againe to Ierusalem into his kingdome: then Manasseh knewe that the Lord was God.
Ndipo atapemphera, Yehova anakhudzidwa ndi kupempha kwakeko ndipo anamvera madandawulo ake. Kotero anamubweretsanso ku Yerusalemu ndi ku ufumu wake. Ndipo Manase anadziwa kuti Yehova ndi Mulungu.
14 Nowe after this he built a wall without the citie of Dauid, on the Westside of Gihon in the valley, euen at the entrie of the fish gate, and compassed about Ophel, and raised it very hie, and put captaines of warre in all the strong cities of Iudah.
Zitapita izi iye anamanga khoma la kunja kwa Mzinda wa Davide kumadzulo kwa kasupe wa Gihoni ku chigwa mpaka polowera ku Chipata cha Nsomba kuzungulira phiri la Ofeli. Iyeyo anakweza kwambiri khomalo. Anayikanso atsogoleri a nkhondo ku mizinda yonse yotetezedwa ya Yuda.
15 And he tooke away the strange gods and the image out of the house of the Lord, and all the altars that he had built in the mount of the house of the Lord, and in Ierusalem, and cast them out of the citie.
Iye anachotsa milungu yonse yachilendo ndi fano mʼNyumba ya Yehova komanso maguwa ansembe onse amene anamanga pa phiri la Nyumba ya Mulungu ndi mu Yerusalemu, nazitayira kunja kwa mzinda.
16 Also he prepared the altar of the Lord, and sacrificed thereon peace offerings, and of thankes, and commanded Iudah to serue the Lord God of Israel.
Kenaka anabwezeretsa guwa lansembe la Yehova ndi kupereka zopereka zachiyanjano ndiponso zopereka zamatamando ndipo anawuza Yuda kuti atumikire Yehova Mulungu wa Israeli.
17 Neuerthelesse the people did sacrifice stil in the hie places, but vnto the Lord their God.
Komabe anthu anapitiriza kupereka nsembe ku malo achipembedzo, koma kwa Yehova, Mulungu wawo yekha.
18 Concerning the rest of the actes of Manasseh, and his prayer vnto his God, and the words of the Seers, that spake to him in ye Name of the Lord God of Israel, beholde, they are written in the booke of the Kings of Israel.
Zina ndi zina zokhudza ulamuliro wa Manase, kuphatikiza mapemphero ake kwa Mulungu wake ndi mawu amene alosi anayankhula kwa iye mʼdzina la Yehova Mulungu wa Israeli, zalembedwa mʼmabuku a mafumu a Israeli.
19 And his prayer and how God was intreated of him, and all his sinne, and his trespasse, and the places wherein he built hie places, and set groues and images (before he was humbled) behold, they are written in the booke of the Seers.
Pemphero lake ndi momwe Mulungu anakhudzidwira ndi kupempha kwakeko, pamodzinso ndi machimo ake onse ndi kusakhulupirika kwake, ndiponso malo onse amene anamanga, malo azipembedzo ndi mafano a Asera ndi mafano asanadzichepetse, zonse zalembedwa mʼmbiri ya alosi.
20 So Manasseh slept with his fathers, and they buried him in his owne house: and Amon his sonne reigned in his stead.
Manase anamwalira ndipo anayikidwa mʼmanda mʼnyumba yake yaufumu. Ndipo Amoni mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.
21 Amon was two and twentie yeere olde, when he began to reigne, and reigned two yeere in Ierusalem.
Amoni anali wa zaka 22 pamene anakhala mfumu ndipo analamulira mu Yerusalemu kwa zaka ziwiri.
22 But he did euill in the sight of the Lord, as did Manasseh his father: for Amon sacrificed to all the images, which Manasseh his father had made, and serued them,
Iye anachita zoyipa pamaso pa Yehova, monga anachitira Manase abambo ake. Amoni analambira ndi kupereka nsembe kwa mafano onse amene anapanga Manase.
23 And he humbled not him selfe before the Lord, as Manasseh his father had humbled himselfe: but this Amon trespassed more and more.
Koma kusiyana ndi abambo ake Manase, iye sanadzichepetse pamaso pa Yehova. Amoni anawonjeza kulakwa kwake.
24 And his seruants conspired against him, and slewe him in his owne house.
Akuluakulu a Amoni anamuchita chiwembu ndipo anamupha mʼnyumba yake yaufumu.
25 But the people of the land slewe all them that had conspired against King Amon: and the people of the land made Iosiah his sonne King in his steade.
Koma anthu a mʼdzikomo anapha onse amene anakonzera chiwembu mfumu Amoni, ndipo anayika mwana wake Yosiya kukhala mfumu mʼmalo mwake.

< 2 Chronicles 33 >