< 2 Chronicles 32 >
1 After these things faithfully described, Saneherib King of Asshur came and entred into Iudah, and besieged the strong cities, and thought to winne them for him selfe.
Zitatha zonse zimene Hezekiya anachita mokhulupirika, Senakeribu mfumu ya ku Asiriya anabwera ndi kuthira nkhondo dziko la Yuda. Iye anazinga mizinda yotetezedwa ya Yuda, kuganiza kuti ayigonjetsa.
2 When Hezekiah sawe that Saneherib was come, and that his purpose was to fight against Ierusalem,
Pamene Hezekiya anaona kuti Senakeribu wabwera ndipo wakonzeka kuchita nkhondo ndi Yerusalemu,
3 Then he tooke counsell with his princes and his nobles, to stoppe the water of the fountaines without the citie: and they did helpe him.
iye anakambirana ndi akuluakulu ake pamodzi ndi atsogoleri a gulu lankhondo za kutseka akasupe ochoka ku kasupe amene anali kunja kwa mzinda, ndipo iwo anamuthandiza.
4 So many of the people assembled themselues, and stopt all the fountaines, and the riuer that ranne through the middes of the countrey, saying, Why should the Kings of Asshur come, and finde much water?
Gulu lalikulu la anthu linasonkhana, ndipo anatseka akasupe onse pamodzi ndi mtsinje umene umayenda mʼkati mwa nthakamo. Iwo ankanena kuti, “Nʼchifukwa chiyani mafumu a Asiriya akabwera kuno adzapeze madzi ambiri?”
5 And he tooke courage, and built all the broken wall, and made vp the towers, and another wall without, and repayred Millo in the citie of Dauid, and made many dartes and shields.
Kenaka iye anagwira ntchito molimbika kukonza madera ogumuka a khoma ndi kumangapo msanja. Anamanganso mpanda wina kunja kwa mpanda winawo ndipo anamanga zolimbitsa Milo ku mzinda wa Davide.
6 And he set captaines of warre ouer the people, and assembled them to him in the broade place of the gate of the citie, and spake comfortably vnto them, saying,
Iye anasankha atsogoleri a ankhondo olamulira anthu ndipo anawasonkhanitsa pamaso pake pa bwalo la chipata cha mzinda ndi kuwalimbikitsa ndi mawu awa:
7 Be strong and couragious: feare not, neither be afraide for the King of Asshur, neither for all the multitude that is with him: for there be more with vs, then is with him.
“Khalani amphamvu ndi olimba mtima. Musachite mantha kapena kutaya mtima chifukwa cha mfumu ya ku Asiriya ndi gulu lalikulu lankhondo limene ali nalo, pakuti ife tili ndi mphamvu yayikulu kuposa imene ili ndi iye.
8 With him is an arme of flesh, but with vs is the Lord our God for to helpe vs, and to fight our battels. Then the people were confirmed by the wordes of Hezekiah King of Iudah.
Iye ali ndi mphamvu ya anthu basi, koma ife tili ndi Yehova Mulungu wathu kutithandiza ndi kuchita nkhondo zathu.” Ndipo anthu anapeza chilimbikitso kuchokera pa zimene Hezekiya mfumu ya Yuda ananena.
9 After this, did Saneherib King of Asshur send his seruants to Ierusalem (while he was against Lachish, and all his dominion with him) vnto Hezekiah King of Iudah and vnto all Iudah that were at Ierusalem, saying,
Nthawi ina, pamene Senakeribu mfumu ya ku Asiriya ndi gulu lake lonse lankhondo anali atazinga Lakisi, iye anatumiza atsogoleri ake ankhondo ku Yerusalemu ndi uthenga uwu kwa Hezekiya mfumu ya Yuda ndi anthu onse a ku Yuda amene anali kumeneko:
10 Thus saith Saneherib the King of Asshur, Wherein doe ye trust, that ye will remaine in Ierusalem, during the siege?
“Senakeribu mfumu ya ku Asiriya akuti: Kodi inu mukukhulupirira chiyani, kuti mukukhalabe mu Yerusalemu mutazingidwa?
11 Doeth not Hezekiah entice you to giue ouer your selues vnto death by famine and by thirst, saying, The Lord our God shall deliuer vs out of the hande of the King of Asshur?
Pamene Hezekiya akunena kuti ‘Yehova Mulungu wathu adzatipulumutsa kuchoka mʼdzanja la mfumu ya ku Asiriya,’ iye akukusocheretsani, kuti mufe ndi njala ndi ludzu.
12 Hath not the same Hezekiah taken away his hie places and his altars, and commanded Iudah and Ierusalem, saying, Ye shall worshippe before one altar, and burne incense vpon it?
Kodi si Hezekiya amene anachotsa malo opembedzerapo Mulungu ameneyu ndi maguwa ansembe ndi kunena kwa anthu a ku Yuda ndi Yerusalemu kuti, ‘Muzipembedza pa guwa lansembe limodzi ndi kupserezapo nsembe?’
13 Knowe ye not what I and my fathers haue done vnto all the people of other countreyes? were the gods of the nations of other landes able to deliuer their land out of mine hande?
“Kodi inu simukudziwa zimene ine ndi makolo anga tachita kwa anthu a mitundu ina? Kodi milungu ya mitundu imeneyi inatha kupulumutsa dziko lawo kuchoka mʼdzanja langa?
14 Who is he of al the gods of those natios (that my fathers haue destroied) that could deliuer his people out of mine hande? that your God should be able to deliuer you out of mine hand?
Kodi ndi milungu iti mwa milungu ya mitundu ina ya anthuwo, imene makolo anga anayiwononga kotheratu, inatha kupulumutsa anthu ake mʼdzanja langa? Nanga tsono Mulungu wanuyo adzakupulumutsani mʼdzanja langa motani?
15 Nowe therefore let not Hezekiah deceiue you, nor seduce you after this sort, neither beleeue ye him: for none of all the gods of any nation or kingdome was able to deliuer his people out of mine hande and out of the hande of my fathers: howe much lesse shall your gods deliuer you out of mine hande?
Choncho inu musalole kuti Hezekiya akunamizeni ndi kukusocheretsani motere. Musamukhulupirire, pakuti palibe mulungu wa mtundu wina uliwonse kapena ufumu wina uliwonse umene unatha kupulumutsa anthu ake kuchoka mʼdzanja langa kapena mʼdzanja la makolo anga. Nanga bwanji Mulungu wanuyo, sadzatha kukupulumutsani kuchoka mʼdzanja langa!”
16 And his seruants spake yet more against the Lord God, and against his seruant Hezekiah.
Atsogoleri a ankhondo a Senakeribu anapitiriza kuyankhula zotsutsana ndi Yehova Mulungu ndi mtumiki wake Hezekiya.
17 He wrote also letters, blaspheming the Lord God of Israel and speaking against him, saying, As the gods of the nations of other countreies could not deliuer their people out of mine hand, so shall not the God of Hezekiah deliuer his people out of mine hande.
Mfumunso inalemba makalata onyoza Yehova, Mulungu wa Israeli, ndipo inanena zotsutsana naye izi: “Monga momwe milungu ya anthu a mayiko ena sinathe kuwapulumutsa kuchoka mʼdzanja langa, chonchonso Mulungu wa Hezekiya sadzapulumutsa anthu ake kuchoka mʼdzanja langa.”
18 Then they cryed with a loude voyce in the Iewes speach vnto the people of Ierusalem that were on the wall, to feare them and to astonish them, that they might take the citie.
Kenaka iwo anafuwula mu Chihebri kwa anthu a mu Yerusalemu amene anali pa khoma, kuwaopseza ndi kuwachititsa mantha ndi cholinga choti alande mzindawo.
19 Thus they spake against the God of Ierusalem, as against the gods of the people of the earth, euen the workes of mans hands,
Iwo anayankhula za Mulungu wa Yerusalemu monga anayankhulira za milungu ya anthu ena a pa dziko lapansi, ntchito ya manja a anthu.
20 But Hezekiah the King, and the Prophet Isaiah the sonne of Amoz prayed against this and cryed to heauen.
Mfumu Hezekiya ndi mneneri Yesaya mwana wa Amozi anafuwulira kumwamba mʼpemphero chifukwa cha zimenezi.
21 And the Lord sent an Angel which destroyed all the valiant men, and the princes and captaines of the hoste of the King of Asshur: so he returned with shame to his owne lande. And when he was come into the house of his god, they that came foorth of his owne bowels, slewe him there with the sworde.
Ndipo Yehova anatumiza mngelo amene anadzapha anthu onse odziwa nkhondo ndi atsogoleri ndiponso oyangʼanira misasa ya mfumu ya ku Asiriya. Choncho Senakeribu anabwerera kwawo wamanyazi. Ndipo atalowa mʼnyumba ya mulungu wake, ena mwa ana ake anamupha ndi lupanga.
22 So the Lord saued Hezekiah and the inhabitants of Ierusalem from the hande of Saneherib King of Asshur, and from the hande of all other, and maintained them on euery side.
Kotero Yehova anapulumutsa Hezekiya ndi anthu a ku Yerusalemu kuchoka mʼdzanja la Senakeribu mfumu ya ku Asiriya ndi mʼdzanja la anthu ena. Yehova anawateteza ku mbali zonse.
23 And many brought offrings vnto the Lord to Ierusalem, and presents to Hezekiah King of Iudah, so that he was magnified in the sight of all nations from thencefoorth.
Anthu ambiri anabweretsa zopereka kwa Yehova ku Yerusalemu ndi mphatso zamtengowapatali kwa Hezekiya mfumu ya Yuda. Kuyambira nthawi imeneyo Hezekiya ankalemekezedwa kwambiri ndi mitundu ina yonse.
24 In those dayes Hezekiah was sicke vnto the death, and prayed vnto the Lord, who spake vnto him, and gaue him a signe.
Pa nthawi imeneyo Hezekiya anadwala ndipo anali pafupi kufa. Iye anapemphera kwa Yehova, amene anamuyankha ndi kumupatsa chizindikiro chodabwitsa.
25 But Hezekiah did not render according to the rewarde bestowed vpon him: for his heart was lift vp, and wrath came vpon him, and vpon Iudah and Ierusalem.
Koma Hezekiya anali ndi mtima wonyada ndipo sanachite molingana ndi kukoma mtima kumene Mulungu anamuonetsera. Choncho mkwiyo wa Yehova unali pa iye ndi pa Yuda ndi Yerusalemu.
26 Notwithstanding Hezekiah humbled him selfe (after that his heart was lifted vp) he and the inhabitants of Ierusalem, and the wrath of the Lord came not vpon them in the dayes of Hezekiah.
Koma kenaka Hezekiya analapa za kunyada kwakeko, monga anachitanso anthu a mu Yerusalemu. Choncho mkwiyo wa Yehova sunafike pa iwo pa nthawi ya Hezekiya.
27 Hezekiah also had exceeding much riches and honour, and he gate him treasures of siluer, and of golde, and of precious stones, and of sweete odours, and of shieldes, and of all pleasant vessels:
Hezekiya anali ndi chuma ndi ulemu wambiri ndipo anamanga nyumba zosungiramo chuma cha siliva wake ndi golide ndi za miyala yokongola, zokometsera zakudya, zishango ndi mtundu uliwonse wa zinthu zamtengowapatali.
28 And of store houses for the increase of wheat and wine and oyle, and stalles for all beasts, and rowes for the stables.
Iye anamanganso nyumba zosungiramo tirigu, vinyo watsopano ndi mafuta a olivi, ndiponso anamanga nyumba zodyeramo ngʼombe zosiyanasiyana, ndi makola a nkhosa.
29 And he made him cities, and had possession of sheepe and oxen in abundance: for God had giuen him substance exceeding much.
Iyeyo anamanga midzi ndipo anali ndi nkhosa ndi ngʼombe zambiri, pakuti Mulungu anamupatsa chuma chambiri.
30 This same Hezekiah also stopped the vpper water springs of Gihon, and led them streight vnderneath towarde the citie of Dauid Westwarde. so Hezekiah prospered in all his workes.
Ndi Hezekiya amene anatseka ku mtunda kwa kasupe wa Gihoni, ndi kumuwongolera kuti madzi ake apite mbali ya kumadzulo kwa Mzinda wa Davide. Iye ankachita bwino pa ntchito iliyonse imene ankagwira.
31 But because of the ambassadours of the princes of Babel, which sent vnto him to enquire of the wonder that was done in the lande, God left him to trie him, and to knowe all that was in his heart.
Koma pamene nthumwi zotumizidwa ndi atsogoleri a ku Babuloni zinabwera kudzamufunsa za chizindikiro chozizwitsa chimene chinachitika mʼdzikomo, Mulungu anamusiya yekha, kumuyesa kuti adziwe zonse zimene zinali mu mtima mwake.
32 Concerning the rest of the actes of Hezekiah, and his goodnesse, beholde, they are written in the vision of Ishiah the Prophet, the sonne of Amoz, in the booke of the Kings of Iudah and Israel.
Zina ndi zina zokhudza ulamuliro wa Hezekiya ndi ntchito za kudzipereka kwake zalembedwa mʼmasomphenya a Yesaya mwana wa Amozi, mʼbuku la mafumu a Yuda ndi Israeli.
33 So Hezekiah slept with his fathers, and they buryed him in the highest sepulchre of the sonnes of Dauid: and all Iudah and the inhabitants of Ierusalem did him honour at his death: and Manasseh his sonne reigned in his stead.
Hezekiya anamwalira ndipo anayikidwa mʼmanda pa phiri pamene pali manda a zidzukulu za Davide. Ayuda onse ndi anthu a mu Yerusalemu anamulemekeza atamwalira. Ndipo Manase mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.