< 2 Chronicles 26 >

1 Then all the people of Iudah tooke Vzziah, which was sixteene yeere olde, and made him King in the steade of his father Amaziah.
Kenaka anthu onse a ku Yuda anatenga Uziya amene anali wa zaka 16, namuyika kukhala mfumu mʼmalo mwa Amaziya abambo ake.
2 He buylt Eloth, and restored it to Iudah after that the King slept with his fathers.
Iye anamanganso mzinda wa Eloti ndi kuwubwezeranso ku Yuda abambo ake atamwalira.
3 Sixteene yeere olde was Vzziah, when he began to reigne, and he reigned two and fiftie yere in Ierusalem, and his mothers name was Iecoliah of Ierusalem.
Uziya anali wa zaka 16 pamene anakhala mfumu ndipo analamulira mu Yerusalemu kwa zaka 70. Dzina la amayi ake linali Yekoliya wa ku Yerusalemu.
4 And hee did vprightly in the sight of the Lord, according to al that his father Amaziah did.
Iye anachita zolungama pamaso pa Yehova, monga momwe anachitira Amaziya abambo ake.
5 And he sought God in the dayes of Zechariah (which vnderstoode the visions of God) and when as he sought the Lord, God made him to prosper.
Iye anapembedza Mulungu nthawi ya Zekariya, amene ankamulangiza za kuopa Mulungu amene anamupatsa chipambano.
6 For he went forth and fought against the Philistims and brake downe the wall of Gath, and the wall of Iabneh, and the wall of Ashdod, and built cities in Ashdod, and among the Philistims.
Iyeyo anapita kukachita nkhondo ndi Afilisti ndipo anagwetsa makoma a Gati, Yabine ndi Asidodi. Ndipo kenaka anamanganso mizinda ya pafupi ndi Asidodi ndi malo ena pafupi ndi Afilisti.
7 And God helped him against ye Philistims, and against the Arabians that dwelt in Gur-baal and Hammeunim.
Mulungu anamuthandiza polimbana ndi Afilisti ndi Aarabu amene amakhala ku Guri-Baala ndiponso polimbana ndi Ameuni.
8 And the Ammonites gaue gifts to Vzziah, and his name spred to the entring in of Egypt: for he did most valiantly.
Aamoni ankabweretsa msonkho kwa Uziya ndipo mbiri yake inamveka mpaka ku malire a dziko la Igupto chifukwa anali wamphamvu kwambiri.
9 Moreouer Uzziah buylt towres in Ierusalem at the corner gate, and at the valley gate, and at the turning, and made them strong.
Uziya anamanga nsanja ku Yerusalemu ku Chipata Chapangodya, ku Chigwa cha Chipata ndi pokhotera mpanda, ndipo anayikamo chitetezo.
10 And he built towres in the wildernesse, and digged many cisternes: for he had much cattell both in the valleyes and playnes, plowmen, and dressers of vines in the mountaines, and in Carmel: for he loued husbandrie.
Iye anamanganso nsanja ku chipululu ndi kukumbanso zitsime zambiri chifukwa anali ndi ziweto zambiri mʼmbali mwa phiri ndi ku zigwa. Iye anali ndi anthu amene ankagwira ntchito mʼminda yake ndiponso mʼminda yake ya mphesa mʼphiri ndi malo achonde, pakuti ankakonda nthaka.
11 Vzziah had also an hoste of fighting men that went out to warre by bandes, according to the count of their nomber vnder the hande of Ieiel the Scribe, and Maaseiah the ruler, and vnder the hand of Hananiah, one of the Kings captaines.
Uziya anali ndi gulu lankhondo lophunzitsidwa bwino, lokonzekera kupita ku nkhondo mʼmagulu monga mwa chiwerengero chawo chimene mlembi Yeiyeli ndi Maaseya anasonkhanitsa motsogozedwa ndi Hananiya mmodzi mwa akuluakulu a mfumu.
12 The whole nomber of the chiefe of the families of the valiant men were two thousande and sixe hundreth.
Chiwerengero chonse cha atsogoleri a mʼmabanja oyangʼanira anthu ochita nkhondo chinali 2,600.
13 And vnder their hande was the armie for warre, three hundreth and seuen thousand, and fiue hundreth that fought valiantly to helpe the King against the enemie.
Pansi pa ulamuliro wawo panali asilikali 307,500 ophunzitsidwa nkhondo, gulu lamphamvu lothandiza mfumu kulimbana ndi adani ake.
14 And Vzziah prepared them throughout all the hoste, shieldes, and speares, and helmets, and brigandines, and bowes, and stones to sling.
Uziya anawapangira asilikaliwo zishango, mikondo, zipewa zankhondo, malaya ankhondo achitsulo, mauta ndi miyala yogendera.
15 He made also very artificial engins in Ierusalem, to be vpon the towres and vpon the corners, to shoote arrowes and great stones: and his name spred farre abroade, because God did helpe him marueilously, till he was mightie.
Mu Yerusalemu anapanga makina okonzedwa ndi anthu aluso amene amagwiritsidwa ntchito pa malo otetezera a pa nsanja ndi pa ngodya kuponyera mivi ndi kugubuduzira miyala. Mbiri yake inamveka kutali ndi ponseponse pakuti anathandizidwa kwambiri mpaka anakhala wamphamvu kwambiri.
16 But when he was strong, his heart was lift vp to his destruction: for he transgressed against the Lord his God, and went into the Temple of the Lord to burne incense vpon the altar of incense.
Koma pamene Uziya anakhala wamphamvu kwambiri, kunyada kwake kunamuwononga. Iye sanakhulupirike kwa Yehova Mulungu wake, ndipo analowa mʼNyumba ya Yehova kukafukiza lubani pa guwa lofukizira.
17 And Azariah the Priest went in after him, and with him foure score Priests of the Lord, valiant men.
Wansembe Azariya pamodzi ndi ansembe a Yehova ena 80 olimba mtima anamutsatira.
18 And they withstoode Vzziah the King, and said vnto him, It perteineth not to thee, Vzziah, to burne incense vnto the Lord, but to the Priests the sonnes of Aaron, that are consecrated for to offer incense: goe forth of the Sanctuarie: for thou hast transgressed, and thou shalt haue none honour of the Lord God.
Iwo anatsutsana naye ndipo anati, “Sibwino kuti inu mfumu muzifukiza lubani koma zidzukulu za Aaroni, zimene zinapatulidwa kuti zizifukiza lubani. Chokani pa malo opatulika ano, pakuti inu mwakhala osakhulupirika, ndipo simudzalemekezedwa ndi Yehova Mulungu.”
19 Then Vzziah was wroth, and had incense in his hand to burne it: and while he was wroth with the Priestes, the leprosie rose vp in his forehead before the Priestes in the house of the Lord beside the incense altar.
Uziya, amene anali ndi chofukizira mʼmanja mwake wokonzeka kuti afukize lubani, anapsa mtima. Iye anakwiyira ansembewo. Ndipo ansembe aja akuona patsogolo pa guwa lofukizira lubani mʼNyumba ya Mulungu, khate linayamba pamphumi pake.
20 And when Azariah the chiefe Priest with al the Priestes looked vpon him, behold, he was leprous in his forehead, and they caused him hastily to depart thence: and he was euen compelled to go out, because the Lord had smitten him.
Azariya, mkulu wa ansembe pamodzi ndi ansembe ena onse atamuyangʼana anaona kuti anali ndi khate pamphumi pake, ndipo anamutulutsa mofulumira. Ndipo iye mwini anafulumira kutuluka, chifukwa Yehova anamulanga.
21 And Vzziah the king was a leper vnto the day of his death, and dwelt as a leper in an house apart, because he was cut off from the house of ye Lord: and Iotham his sonne ruled ouer the Kings house, and iudged the people of the land.
Mfumu Uziya anali ndi khate mpaka tsiku limene anamwalira. Iye amakhala mʼnyumba ya yekha ngati wakhate, ndipo samalowa mʼNyumba ya Yehova. Yotamu mwana wake ndiye amayangʼanira nyumba yaufumu ndipo ankalamulira anthu a mʼdzikomo.
22 Concerning the rest of the acts of Vzziah, first and last, did Isaiah the Prophet the sonne of Amoz write.
Ntchito zina za mfumu Uziya, kuyambira pachiyambi mpaka pa mapeto, zinalembedwa ndi mneneri Yesaya mwana wa Amozi.
23 So Vzziah slept with his fathers, and they buryed him with his fathers in the fielde of the burial, which perteined to the kings: for they said, He is a leper. And Iotham his sonne reigned in his steade.
Uziya analondola makolo ake, ndipo anamuyika pamodzi ndi makolo ake ku malo a manda a mafumu, koma osati mʼmanda mwawomo poti anthu anati, “Iyeyu anali ndi khate.” Ndipo Yotamu mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.

< 2 Chronicles 26 >