< 2 Chronicles 19 >
1 And Iehoshaphat the King of Iudah returned safe to his house in Ierusalem.
Yehosafati, mfumu ya Yuda itabwerera mwamtendere ku nyumba yake yaufumu ku Yerusalemu,
2 And Iehu the sonne of Hanani the Seer went out to meete him, and said to King Iehoshaphat, Wouldest thou helpe the wicked, and loue them that hate the Lord? therefore for this thing the wrath of the Lord is vpon thee.
mlosi Yehu, mwana wa Hanani, anatuluka kukakumana naye ndipo anati kwa mfumu, “Kodi nʼkoyenera kuthandiza oyipa ndi kukonda iwo amene amadana ndi Yehova? Chifukwa cha zimenezi mkwiyo wa Yehova uli pa inu.
3 Neuertheles good things are found in thee, because thou hast taken away ye groues out of the land, and hast prepared thine heart to seeke God.
Komabe, muli zinthu zina zabwino mwa inu, pakuti inu mwachotsa mʼdziko muno mafano a Asera ndipo mwakhazikitsa mtima wanu pa kufunafuna Mulungu.”
4 So Iehoshaphat dwelt at Ierusalem, and returned and went through the people from Beer-sheba to mount Ephraim, and brought them againe vnto the Lord God of their fathers.
Yehosafati anakakhala ku Yerusalemu, ndipo amayenda pakati pa anthu kuchokera ku Beeriseba mpaka ku dziko lamapiri la Efereimu ndipo anawatembenuzira kwa Yehova, Mulungu wa makolo awo.
5 And hee set iudges in the lande throughout all the strong cities of Iudah, citie by citie,
Iye anasankha oweruza mʼdzikomo, mu mzinda uliwonse wotetezedwa wa Yuda.
6 And said to the iudges, Take heede what ye doe: for yee execute not the iudgements of man, but of the Lord, and he will be with you in the cause and iudgement.
Ndipo anawawuza kuti, “Muganize bwino zimene mukuchita, chifukwa simukuweruza mʼmalo mwa munthu koma Yehova, amene ali nanu pamene mukupereka chiweruzo.
7 Wherefore nowe let the feare of the Lord be vpon you: take heede, and do it: for there is no iniquitie with the Lord our God, neither respect of persons, nor receiuing of reward.
Tsopano kuopsa kwa Yehova kukhale pa inu. Muweruze mosamala, pakuti ndi Yehova Mulungu wathu palibe kupotoza chilungamo kapena kukondera kapenanso kulandira ziphuphu.”
8 Moreouer in Ierusalem did Iehoshaphat set of the Leuites, and of the Priests and of the chiefe of the families of Israel, for the iudgement and cause of the Lord: and they returned to Ierusale.
Mu Yerusalemu, Yehosafati anasankha Alevi ena, ansembe ndi atsogoleri a mabanja a Aisraeli kuti aziyangʼanira Malamulo a Yehova ndi kuweruza milandu. Ndipo iwo amakhala mu Yerusalemu.
9 And he charged them, saying, Thus shall yee doe in the feare of the Lord faithfully and with a perfite heart.
Iye anawalamula kuti, “Inu mutumikire mokhulupirika ndi mtima wanu wonse moopa Yehova.
10 And in euery cause that shall come to you of your brethren that dwel in their cities, betweene blood and blood, betweene law and precept, statutes and iudgements, ye shall iudge them, and admonish them that they trespasse not against the Lord, that wrath come not vpon you and vpon your brethren. This shall ye do and trespasse not.
Pa mlandu uliwonse wobwera kwa inu kuchokera kwa abale anu amene amakhala mʼmizinda, mlandu wokhetsa magazi kapena mlandu wosamvera malamulo kapena malangizo kapena ziphunzitso zina, inu muziwachenjeza kuti asachimwire Yehova pakuti mukapanda kutero mkwiyo wake udzakhala pa inu ndi abale anu. Chitani zimenezi ndipo simudzachimwa.
11 And behold, Amariah the Priest shalbe the chiefe ouer you in all matters of the Lord, and Zebadiah ye sonne of Ishmael, a ruler of the house of Iudah, shalbe for al the Kings affaires, and the Leuites shalbe officers before you. Bee of courage, and doe it, and the Lord shalbe with the good.
“Amariya, mkulu wa ansembe adzakhala wokuyangʼanirani pa zonse zokhudza Yehova, ndipo Zebadiya mwana wa Ismaeli, mtsogoleri wa fuko la Yuda, adzakhala wokuyangʼanirani pa zonse zokhudza mfumu ndipo Alevi adzatumikira ngati okuyangʼanirani. Muchite molimba mtima ndipo Yehova akhale ndi iwo amene adzachita bwino.”