< 2 Chronicles 11 >
1 And when Rehoboam was come to Ierusalem, he gathered of the house of Iudah and Beniamin nine score thousande chosen men of warre to fight against Israel, and to bring the kingdome againe to Rehoboam.
Rehobowamu atafika ku Yerusalemu anasonkhanitsa asilikali 180,000 a fuko la Yuda ndi Benjamini kuti akachite nkhondo ndi Israeli, kuti abwezeretse ufumu kwa Rehobowamu.
2 But the worde of the Lord came to Shemaiah the man of God, saying,
Koma Yehova anayankhula ndi munthu wa Mulungu Semaya kuti,
3 Speake vnto Rehoboam, the sonne of Salomon King of Iudah, and to all Israel that are in Iudah, and Beniamin, saying,
“Kawuze Rehobowamu mwana wa Solomoni mfumu ya Yuda ndi Aisraeli onse ali mu Yuda ndi Benjamini kuti,
4 Thus sayth the Lord, Ye shall not goe vp, nor fight against your brethren: returne euery man to his house: for this thing is done of me. They obeyed therfore the word of the Lord, and returned from going against Ieroboam.
‘Yehova akuti: Musapite kukamenyana ndi abale anu. Pitani kwanu, aliyense wa inu, pakuti izi ndikuchita ndine.’” Choncho anamvera mawu a Yehova ndi kubwerera osapita kukamenyana ndi Yeroboamu.
5 And Rehoboam dwelt in Ierusalem, and buylt strong cities in Iudah.
Rehobowamu amakhala mu Yerusalemu ndipo anamanga mizinda ya chitetezo iyi mu Yuda:
6 Hee buylt also Beth-lehem, and Etam, and Tekoa,
Betelehemu, Etamu, Tekowa,
7 And Beth-zur, and Shoco, and Adullam,
Beti Zuri, Soko, Adulamu,
8 And Gath, and Maresha, and Ziph,
Gati, Maresa, Zifi,
9 And Adoraim, and Lachish, and Azekah,
Adoraimu, Lakisi, Azeka,
10 And Zorah, and Aialon, and Hebron, which were in Iudah and Beniamin, strong cities.
Zora, Ayaloni ndi Hebroni. Iyi ndiye inali mizinda yotetezedwa ya Yuda ndi Benjamini.
11 And he repaired the strong holdes and put captaines in them, and store of vitaile, and oyle and wine.
Iye anakhwimitsa chitetezo cha mizindayi ndipo anayikamo atsogoleri a ankhondo, pamodzi ndi chakudya, mafuta a olivi ndi vinyo.
12 And in all cities he put shieldes and speares, and made them exceeding strong: so Iudah and Beniamin were his.
Mʼmizinda yonse anayikamo zishango zikuluzikulu ndi mikondo, ndipo anachititsa kuti mizindayo ikhale yamphamvu. Choncho iye amalamulira Yuda ndi Benjamini.
13 And the Priests and the Leuites that were in all Israel, resorted vnto him out of all their coastes.
Ansembe ndi Alevi a mʼmadera onse a Israeli anakhala mbali ya Rehobowamu.
14 For the Leuites left their suburbes and their possession, and came to Iudah and to Ierusalem: for Ieroboam and his sonnes had cast them out from ministring in the Priestes office vnto the Lord.
Alevi anasiya malo awo owetera ziweto ndi katundu wawo, ndi kubwera ku Yuda ndi ku Yerusalemu chifukwa Yeroboamu ndi ana ake anawakana kukhala ansembe a Yehova.
15 And he ordeyned him Priests for the hie places, and for the deuils and for the calues which he had made.
Ndipo iye anasankha ansembe akeake a pa malo opatulika ndi a mafano a mbuzi ndi mwana wangʼombe amene anapanga.
16 And after the Leuites there came to Ierusalem of all the tribes of Israel, such as set their heartes to seeke the Lord God of Israel, to offer vnto the Lord God of their fathers.
Anthu ochokera fuko lililonse la Israeli amene anatsimikiza mitima yawo kufunafuna Yehova Mulungu wa Israeli, ankapitabe ku Yerusalemu kukapereka nsembe kwa Yehova, Mulungu wa makolo awo.
17 So they strengthened the kingdome of Iudah, and made Rehoboam the sonne of Salomon mightie, three yeere long: for three yeere they walked in in the way of Dauid and Salomon.
Iwo analimbikitsa ufumu wa Yuda, ndipo anathandiza Rehobowamu mwana wa Solomoni kwa zaka zitatu. Pa nthawi imeneyi iye amatsatira zochita za Davide ndi Solomoni.
18 And Rehoboam tooke him Mahalath ye daughter of Ierimoth the sonne of Dauid to wife, and Abihail the daughter of Eliab the sonne of Ishai,
Rehobowamu anakwatira Mahalati, amene abambo ake anali Yerimoti, mwana wa Davide, ndipo amayi ake anali Abihaili, mwana wa Eliabu, mwana wa Yese.
19 Which bare him sonnes Ieush, and Shemariah, and Zaham.
Mkaziyo anamubereka ana aamuna awa: Yeusi, Semariya ndi Zahamu.
20 And after her he tooke Maakah ye daughter of Absalom which bare him Abiiah, and Atthai, and Ziza, and Shelomith.
Kenaka anakwatira Maaka, mwana wamkazi wa Abisalomu, amene anamubereka Abiya, Atai, Ziza ndi Selomiti.
21 And Rehoboam loued Maakah ye daughter of Absalom aboue all his wiues and his concubines: for he tooke eighteene wiues, and three score concubines, and begate eyght and twentie sonnes, and three score daughters.
Rehobowamu ankamukonda Maaka mwana wa Abisalomu kuposa aliyense mwa akazi ake ndi azikazi. Iye anali ndi akazi 18, azikazi 60, ana aamuna 28 ndi ana aakazi 60.
22 And Rehoboam made Abiiah the sonne of Maakah the chiefe ruler among his brethren: for he thought to make him King.
Rehobowamu anasankha Abiya mwana wa Maaka kuti akhale mtsogoleri pa abale ake, ndi cholinga choti adzakhale mfumu.
23 And he taught him: and dispersed all his sonnes throughout all the countreis of Iudah and Beniamin vnto euery strong citie: and hee gaue them aboundance of vitaile, and desired many wiues.
Iye anachita mwanzeru, pomwaza ena mwa ana ake ku madera onse a Yuda ndi Benjamini, ndi ku mizinda yonse yotetezedwa. Iye anawapatsa zinthu zambiri ndiponso anawafunira akazi ambiri.