< 1 Samuel 9 >
1 There was nowe a man of Beniamin, mightie in power named Kish, the sonne of Abiel, the sonne of Zeror, the sonne of Bechorath, the sonne of Aphiah, the sonne of a man of Iemini.
Panali munthu wina wa fuko la Benjamini, wotchuka, dzina lake Kisi, mwana wa Abieli, mwana wa Zerori, mwana wa Bekorati, mwana wa Afiya.
2 And he had a sonne called Saul, a goodly yong man and a faire: so that among the children of Israel there was none goodlier then he: from the shoulders vpwarde he was hier then any of the people.
Iyeyu anali ndi mwana dzina lake Sauli, mnyamata wa maonekedwe abwino. Pakati pa Aisraeli onse panalibe wofanana naye. Anali wamtali kotero kuti anthu onse ankamulekeza mʼmapewa.
3 And the asses of Kish Sauls father were lost: therefore Kish said to Saul his sonne, Take nowe one of the seruants with thee, and arise, goe, and seeke the asses.
Tsono abulu a Kisi, abambo ake a Sauli anasowa. Choncho Kisi anati kwa mwana wake Sauli, “Tenga wantchito mmodzi ndipo mupite mukafunefune abuluwo.”
4 So he passed through mount Ephraim, and went through the lande of Shalishah, but they found them not. Then they went through the land of Shalim, and there they were not: he went also through ye land of Iemini, but they found the not.
Choncho iwo anadutsa dziko la mapiri a Efereimu ndi dera la Salisa, koma sanawapeze. Anadutsa ku Saalimu koma abuluwo sanawapeze. Kenaka anadutsa dziko la Benjamini, koma osawapezabe.
5 When they came to the lande of Zuph, Saul saide vnto his seruant that was with him, Come and let vs returne, lest my father leaue the care of asses, and take thought for vs.
Atafika ku dera la Zufi, Sauli anawuza mnyamata wake kuti, “Tiye tibwerere, mwina abambo anga angasiye kudandaula za abulu ndipo adzayamba kudandaula za ife.”
6 And he said vnto him, Behold nowe, in this citie is a man of God, and he is an honorable man: all that he saith commeth to passe: let vs nowe goe thither, if so be that he can shewe vs what way we may goe.
Koma mnyamatayo anayankha kuti, “Taonani, mu mzinda uwo muli munthu wa Mulungu. Anthu amamupatsa ulemu kwambiri, ndipo zonse zimene amanena zimachitika. Tiyeni tipite kumeneko tsopano. Mwina adzatiwuza kumene tiyenera kulowera.”
7 Then saide Saul to his seruant, Well then, let vs goe: but what shall we bring vnto the man? For the bread is spent in our vessels, and there is no present to bring to the man of God: what haue we?
Sauli anafunsa mnyamata wake kuti, “Tikapita tikamupatsa chiyani munthuyo pakuti chakudya chimene chinali mʼmatumba mwathu chatha? Tilibe mphatso iliyonse yoti timutengere munthu wa Mulungu. Nanga tili ndi chiyani?”
8 And the seruant answered Saul againe, and said, Beholde, I haue founde about me the fourth part of a shekell of siluer: that will I giue the man of God, to tell vs our way.
Mnyamatayo anayankha kuti, “Onani, ndili ndi kandalama kakangʼono ka siliva. Ndikamupatsa munthu wa Mulunguyo ndipo akatidziwitsa kumene kuli abuluwo.”
9 (Beforetime in Israel when a man went to seeke an answere of God, thus he spake, Come, and let vs goe to the Seer: for he that is called nowe a Prophet, was in the olde time called a Seer)
(Kale mu Israeli ngati munthu afuna kukapempha nzeru kwa Mulungu ankanena kuti, “Tiyeni tipite kwa mlosi.” Ndiye kuti munthu amene lero akutchedwa mneneri, kale ankatchedwa mlosi).
10 Then saide Saul to his seruant, Well saide, come, let vs goe: so they went into the citie where the man of God was.
Tsono Sauli anawuza mnyamata wake kuti, “Chabwino, tiye tipite.” Ndipo ananyamuka kupita ku mzinda umene kunali munthu wa Mulunguyo.
11 And as they were going vp the hie way to the citie, they found maydes that came out to draw water, and said vnto them, Is there here a Seer?
Akukwera phiri kupita ku mzindawo anakumana ndi atsikana akutuluka mu mzindamo kukatunga madzi, ndipo anawafunsa kuti, “Kodi mlosi uja alipo?”
12 And they answered them, and said, Yea: loe, he is before you: make haste nowe, for he came this day to the citie: for there is an offering of the people this day in the hie place.
Iwo anayankha, “Inde alipo. Ali kutsogolo kwanuku, fulumirani tsopano, wangobwera kumene mu mzinda wathu uno lero, chifukwa lero anthu akupereka nsembe ku phiri.
13 When ye shall come into the citie, ye shall finde him straightway yet he come vp to the hie place to eate: for the people will not eate vntill he come, because he will blesse the sacrifice: and then eate they that be bidden to the feast: nowe therefore goe vp: for euen now shall ye find him.
Mukangolowa mu mzindawo mumupeza asanapite ku phiri kukadya. Anthu sangayambe kudya iye asanabwere chifukwa iyeyu ayenera kudalitsa nsembeyo. Kenaka anthu oyitanidwa adzayamba kudya. Pitani tsopano, chifukwa muyenera kumupeza nthawi ino.”
14 Then they went vp into the citie, and when they were come into the middes of the citie, Samuel came out against them, to goe vp to the hie place.
Choncho anapita ku mzinda kuja. Akulowa mu mzindamo, anaona Samueli akutuluka mu mzindamo akubwera kumene kunali iwo, koma amapita ku phiri, ku malo wopatulika.
15 But the Lord had reueiled to Samuel secretly (a day before Saul came) saying,
Koma chadzulo lake Sauli asanafike, Yehova anali atamuwuza kale Samueli za zimenezi kuti,
16 To morow about this time I will send thee a man out of the land of Beniamin: him shalt thou anoint to be gouernour ouer my people Israel, that he may saue my people out of the hands of the Philistims: for I haue looked vpon my people, and their crie is come vnto me.
“Mawa nthawi ngati yomwe ino ndidzakutumizira munthu wochokera ku dziko la Benjamini. Udzamudzoze kuti akhale mtsogoleri wa anthu anga, Aisraeli. Iye adzawapulumutsa mʼdzanja la Afilisti. Ine ndaona kuzunzika kwawo ndipo ndamva kulira kwawo.”
17 When Samuel therefore sawe Saul, the Lord answered him, See, this is the man whom I spake to thee of, he shall rule my people.
Samueli atamuona Sauli, Yehova anamuwuza kuti, “Munthu ndinakuwuza uja ndi uyu. Iyeyu adzalamulira anthu anga.”
18 Then went Saul to Samuel in the middes of the gate, and said, Tell me, I pray thee, where the Seers house is.
Tsono Sauli anayandikira Samueli pa chipata ndipo anamufunsa, “Kodi mungandiwuze kumene kuli nyumba ya mlosi?”
19 And Samuel answered Saul, and saide, I am the Seer: goe vp before me vnto the hie place: for ye shall eate with me to day. and to morowe I will let thee goe, and will tell thee all that is in thine heart.
Samueli anayankha, “Ine ndine mlosiyo. Tsogolani kupita ku phiri pakuti lero mudya ndi ine, ndipo mawa mmawa ndidzakuwuzani zonse zimene zili mu mtima mwanu.
20 And as for thine asses that were lost three dayes ago, care not for them: for they are founde. and on whom is set all the desire of Israel? is it not vpon thee and on all thy fathers house?
Musadere nkhawa za abulu anu amene akhala akusowa masiku atatu apitawa, poti apezeka kale. Kodi Aisraeli onse akufunitsitsa ndani? Kodi si ndiwe ndi nyumba yonse ya abambo ako?”
21 But Saul answered, and said, Am not I the sonne of Iemini of the smallest tribe of Israel? and my familie is the least of all the families of the tribe of Beniamin. Wherefore then speakest thou so to me?
Sauli anayankha, “Inetu ndine Mbenjamini, fuko lalingʼono la mafuko onse a Israeli, ndipo banja langa ndi lalingʼono pakati pa mabanja a fuko la Benjamini. Nanga nʼchifukwa chiyani mukunena zimenezi kwa ine?”
22 And Samuel tooke Saul and his seruant, and brought them into the chamber, and made them sit in the chiefest place among them that were bidden: which were about thirtie persons.
Ndipo Samueli anatenga Sauli ndi mnyamata wake uja ndi kulowa nawo mʼchipinda chachikulu ndipo anawakhazika kutsogolo kwa anthu oyitanidwa. Onse pamodzi analipo anthu makumi atatu.
23 And Samuel saide vnto the cooke, Bring foorth the portion which I gaue thee, and whereof I said vnto thee, Keepe it with thee.
Tsono Samueli anati kwa wophika, “Bwera nayo nyama imene ndinakupatsa, imene ndinakuwuza kuti uyisunge pambali.”
24 And the cooke tooke vp the shoulder, and that which was vpon it, and set it before Saul. And Samuel said, Beholde, that which is left, set it before thee and eate: for hitherto hath it bene kept for thee, saying, Also I haue called the people. So Saul did eate with Samuel that day.
Kotero wophikayo anatenga mwendo wa nyama ndipo anawuyika patsogolo pa Sauli. Samueli anati “Nayi nyama imene ndinakusungira kuti pa nthawi yake udye pamodzi ndi anthu amene ndawayitana.” Ndipo Sauli anadya tsiku limenelo ndi Samueli.
25 And when they were come downe from the hie place into the citie, he communed with Saul vpon the top of the house.
Atatsika kuchoka ku phiri kuja, Samueli anamukonzera Sauli malo ogona pa denga la nyumba yake, ndipo Sauli anagona pamenepo.
26 And when they arose early about ye spring of the day, Samuel called Saul to the top of the house, saying, Vp, that I may send thee away. And Saul arose, and they went out, both he, and Samuel.
Tsono mʼbandakucha Samueli anayitana Sauli pa dengapo nati, “Konzeka ndipo ine ndikuperekeza.” Choncho Sauli anadzuka ndipo onse awiri, Samueli ndi Sauli anakalowa mu msewu.
27 And when they were come downe to the ende of the citie, Samuel said to Saul, Bid the seruant goe before vs, (and he went) but stand thou still nowe, that I may shewe thee the worde of God.
Atakafika ku mathero a mzindawo, Samueli anati kwa Sauli, “Muwuzeni mnyamata wanu kuti atsogole, koma inuyo muyime pangʼono kuti ndikuwuzeni mawu ochokera kwa Mulungu.”