< 1 Samuel 24 >
1 When Saul was turned from ye Philistims, they told him, saying, Behold, Dauid is in the wildernes of En-gedi.
Sauli atabwera kuchokera kumene amathamangitsa Afilisti anamva kuti, “Davide ali mʼchipululu cha Eni Gedi.”
2 Then Saul tooke three thousande chosen men out of all Israel, and went to seeke Dauid and his men vpon the rocks among the wilde goates.
Tsono Sauli anatenga asilikali 3,000 odziwa kumenya bwino nkhondo kuchokera pakati pa Aisraeli onse ndipo anapita kukafunafuna Davide ndi anthu ake ku Matanthwe a Mbalale.
3 And hee came to the sheepecoates by the way where there was a caue, and Saul went in to do his easement: and Dauid and his men sate in the inward parts of the caue.
Iye anafika ku makola a nkhosa amene anali mʼmbali mwa njira. Kumeneko kunali phanga, ndipo Sauli analowa mʼphangamo kuti akadzithandize. Davide ndi anthu ake ankabisala mʼkati mwenimweni mwa phangalo.
4 And the men of Dauid said vnto him, See, the day is come, whereof the Lord sayde vnto thee, Beholde, I will deliuer thine enemie into thine hande, and thou shalt doe to him as it shall seeme good to thee. Then Dauid arose and cut off the lap of Sauls garment priuily.
Tsono anthu a Davide anamuwuza kuti, “Tsiku lija lafika limene Yehova anakuwuzani kuti, ‘Ndidzapereka mdani wanu mʼmanja mwanu, ndi kumuchita chimene chidzakukomereni.’” Koma Davide anapita mwakachetechete ndi kukadula msonga ya mkanjo wa Sauli.
5 And afterward Dauid was touched in his heart, because he had cut off the lappe which was on Sauls garment.
Atachita izi, Davide anatsutsika mu mtima chifukwa anadula msonga ya mkanjo wa Sauli.
6 And he said vnto his men, The Lord keepe mee from doing that thing vnto my master the Lords Anoynted, to lay mine hand vpon him: for he is the Anoynted of the Lord.
Tsono anawuza anthu ake kuti, “Yehova asalole kuti ndimuchite choyipa mbuye wanga, wodzozedwa wa Yehova. Ndisamupweteke pakuti ndi wodzozedwa wa Yehova.”
7 So Dauid ouercame his seruants with these words, and suffered them not to arise against Saul: so Saul rose vp out of the caue and went away.
Choncho Davide anabweza mitima ya anthu ake ndi mawu amenewa, ndipo sanawalole kuti aphe Sauli. Pambuyo pake Sauli anatuluka mʼphangamo ndipo anachoka.
8 Dauid also arose afterward, and went out of the caue, and cryed after Saul, saying, O my lorde the King. And when Saul looked behinde him, Dauid inclined his face to the earth, and bowed himselfe.
Kenaka Davide anatuluka mʼphanga muja ndipo anayitana Sauli, “Mbuye wanga!” Sauli atayangʼana mʼmbuyo, Davide anawerama ndi kugunditsa nkhope yake pansi.
9 And Dauid saide to Saul, Wherefore giuest thou an eare to mens words, that say, Behold, Dauid seeketh euill against thee?
Anafunsa Sauli kuti, “Nʼchifukwa chiyani mumamvera mawu a anthu kuti, ‘Davide wakukonzerani chiwembu?’
10 Behold, this day thine eyes haue seene, that the Lord had deliuered thee this day into mine hand in the caue, and some bade me kill thee, but I had compassion on thee, and said, I will not lay mine hande on my master: for he is the Lordes Anoynted.
Lero lino inu mwadzionera nokha kuti Yehova anakuperekani mʼmanja mwanga mʼphanga muja. Ena anandiwuza kuti ndikupheni, koma ndakusiyani. Ndinati, ‘Sindidzapha mbuye wanga pakuti ndiye wodzozedwa wa Yehova.’
11 Moreouer my father, behold: behold, I say, the lappe of thy garment in mine hand: for when I cut off the lappe of thy garment, I killed thee not. Vnderstad and see, that there is neither euil nor wickednesse in mee, neither haue I sinned against thee, yet thou huntest after my soule to take it.
Tsono abambo anga, onanitu kansalu ka mkanjo wanu kali mʼdzanja langali! Popeza kuti ndinatha kudula msonga ya mkanjo wanu koma osakuphani, pamenepo mudziwe kuti ine ndilibe maganizo woti ndikuchiteni choyipa kapena kukuwukirani. Sindinakulakwireni ngakhale kuti inu mukufuna moyo wanga kuti mundiphe.
12 The Lord be iudge betweene thee and me, and the Lord auenge me of thee, and let not mine hand be vpon thee.
Yehova aweruze pakati pa inu ndi ine, akulangeni chifukwa cha zoyipa zimene mukundichitazi, koma dzanja langa silidzakukhudzani.
13 According as the olde prouerbe sayeth, Wickednesse proceedeth from the wicked, but mine hand be not vpon thee.
Paja anthu akale anati, ‘Munthu woyipa, ntchito zakenso ndi zoyipa.’ Kotero dzanja langa silidzakukhudzani.
14 After whom is the King of Israel come out? after whome doest thou pursue? after a dead dog, and after a flea?
“Kodi mfumu ya Israeli yadzalondola yani. Inu mukuthamangitsa yani? Galu wakufa kodi? Nsabwe kodi?
15 The Lord therfore be iudge, and iudge betweene thee and me, and see, and pleade my cause, and deliuer me out of thine hand.
Nʼchifukwa chake Yehova agamule, inde aweruze pakati pa inu ndi ine ndi kupeza wolakwa. Yehova anditeteze ndi kundipulumutsa mʼdzanja lanu.”
16 Whe Dauid had made an end of speaking these words to Saul, Saul sayd, Is this thy voyce, my sonne Dauid? and Saul lift vp his voice, and wept,
Davide atatsiriza kuyankhula mawu awa, Sauli anafunsa kuti, “Kodi mawu amenewa ndi akodi mwana wanga Davide?” Sauli anayamba kulira mokweza.
17 And sayd to Dauid, Thou art more righteous then I: for thou hast rendred me good, and I haue rendred thee euill.
Anawuza Davide kuti, “Ndiwe wolungama kuposa ine. Iwe wandikomera mtima pamene ine ndakuchitira zoyipa.
18 And thou hast shewed this day, that thou hast dealt well with me: forasmuch as when the Lord had closed me in thine hands, thou killedst me not.
Iweyo lero lino wandifotokozera zabwino zimene wandichitira. Yehova anandipereka mʼdzanja lako koma iwe sunandiphe.
19 For who shall finde his enemie, and let him depart free? wherefore the Lord render thee good for that thou hast done vnto me this day.
Kodi munthu atapeza mdani wake angamulole kuti apite wosamuvulaza? Motero Yehova akuchitire iwe zabwino chifukwa cha zimene wandichitira lerozi.
20 For now behold, I know that thou shalt be King, and that the kingdome of Israel shall be stablished in thine hand.
Ona tsono, Ine ndikudziwa kuti udzakhala mfumu ndithu ndipo ufumu wa Israeli udzakhazikika mʼmanja mwako.
21 Sweare now therfore vnto me by the Lord, that thou wilt not destroy my seede after me, and that thou wilt not abolish my name out of my fathers house.
Tsopano undilonjeze molumbira lero mʼdzina la Yehova kuti sudzapha zidzukulu zanga ine nditamwalira kapena kufuta dzina langa pa banja la makolo anga.”
22 So Dauid sware vnto Saul, and Saul went home: but Dauid and his men went vp vnto ye hold.
Choncho Davide analumbira pamaso pa Sauli. Pambuyo pake Sauli anabwerera kwawo, koma Davide ndi anthu ake anapitanso ku phanga kuja.