< 1 Kings 4 >

1 And King Salomon was King ouer all Israel.
Ndipo Mfumu Solomoni inakhala mfumu ya Aisraeli onse.
2 And these were his princes, Azariah the sonne of Zadok the Priest,
Nduna zake zikuluzikulu zinali izi: Azariya mwana wa Zadoki anali wansembe;
3 Elihoreph and Ahiah the sonnes of Shisha scribes, Iehoshaphat the sonne of Ahilud, the recorder,
Elihorefe ndi Ahiya, ana a Sisa, anali alembi; Yehosafati mwana wa Ahiludi, anali mlembi wa zochitika;
4 And Benaiah the sonne of Iehoiada was ouer the hoste, and Zadok and Abiathar Priests,
Benaya mwana wa Yehoyada, anali mtsogoleri wa ankhondo; Zadoki ndi Abiatara, anali ansembe;
5 And Azariah the sonne of Nathan was ouer the officers, and Zabud the sonne of Nathan Priest was the Kings friend,
Azariya mwana wa Natani, anali woyangʼanira nduna za mʼzigawo; Zabudi mwana wa Natani, anali wansembe ndi bwenzi la mfumu;
6 And Ahishar was ouer the houshold: and Adoniram the sonne of Abda was ouer the tribute.
Ahisara, anali mkulu woyangʼanira nyumba ya mfumu; Adoniramu mwana wa Abida, anali mkulu woyangʼanira ntchito za thangata.
7 And Salomon had twelue officers ouer all Israel, which prouided vitailes for the King and his housholde: eche man had a moneth in the yeere to prouide vitailes.
Solomoni analinso ndi abwanamkubwa khumi ndi awiri amene ankayangʼanira zigawo zonse za dziko la Israeli. Iwo ankapereka chakudya kwa mfumu ndiponso ku banja laufumu. Bwanamkubwa aliyense ankapereka chakudya mwezi umodzi pa chaka.
8 And these are their names: the sonne of Hur in mount Ephraim:
Mayina awo ndi awa: Beni-Huri, wa ku dziko la mapiri la Efereimu;
9 The sonne of Dekar in Makaz, and in Shaalbim and Beth-shemesh, and Elon and Beth-hanan:
Beni-Dekeri, woyangʼanira mizinda ya Makazi, Saalibimu, Beti-Semesi ndi Eloni Beti-Hanani;
10 The sonne of Hesed in Aruboth, to whom perteined Sochoh, and all the land of Hepher:
Beni-Hesedi, woyangʼanira mizinda ya Aruboti (Soko ndi dziko lonse la Heferi);
11 The sonne of Abinadab in all the region of Dor, which had Taphath the daughter of Salomon to wife.
Beni-Abinadabu, woyangʼanira Nafoti Dori (iye anakwatira Tafati mwana wa Solomoni);
12 Baana the sonne of Ahilud in Taanach, and Megiddo, and in all Beth-shean, which is by Zartanah beneath Izreel, from Beth-shean to Abelmeholah, eue til beyond ouer against Iokmeam:
Baana mwana wa Ahiludi, anali woyangʼanira Taanaki ndi Megido, ndi ku Beti Sani konse, kufupi ndi ku Zaretani kumunsi kwa Yezireeli, kuyambira ku Beti-Seani mpaka ku Abeli-Mehola kukafika mpaka ku Yokineamu;
13 The sonne of Geber in Ramoth Gilead, and his were the townes of Iair, the sonne of Manasseh, which are in Gilead, and vnder him was the region of Argob, which is in Bashan: threescore great cities with walles and barres of brasse.
Beni-Geberi, anali woyangʼanira Ramoti Giliyadi (midzi ya Yairi inali ya mwana wa Manase ku Giliyadi, pamodzinso ndi chigawo cha Arigobu ku Basani ndiponso mizinda yake yayikulu makumi asanu ndi umodzi yokhala ndi malinga ndi mipiringidzo yamkuwa).
14 Ahinadab the sonne of Iddo had to Mahanaim:
Ahinadabu mwana wa Ido, anali woyangʼanira Mahanaimu;
15 Ahimaaz in Naphtali, and he tooke Basmath the daughter of Salomon to wife:
Ahimaazi anali woyangʼanira Nafutali (iyeyu anakwatira Basemati mwana wa Solomoni);
16 Baanah the sonne of Hushai in Asher and in Aloth:
Baana mwana wa Husai, anali woyangʼanira Aseri ndi Bealoti;
17 Iehoshaphat the sonne of Paruah in Issachar.
Yehosafati mwana wa Paruwa, anali woyangʼanira Isakara;
18 Shimei the sonne of Elah in Beniamin:
Simei mwana wa Ela, anali woyangʼanira Benjamini;
19 Geber the sonne of Vri in the countrey of Gilead, the land of Sihon King of the Amorites, and of Og King of Bashan, and was officer alone in the land.
Geberi mwana wa Uri, anali woyangʼanira Giliyadi (dziko la Sihoni mfumu ya Aamori ndi dziko la Ogi mfumu ya Basani). Iye ankayangʼanira chigawo chonsechi yekha.
20 Iudah and Israel were many, as the sand of the sea in number, eating, drinking, and making merry.
Anthu a ku Yuda ndi ku Israeli anali ochuluka ngati mchenga wa mʼmbali mwa nyanja. Ankadya ndi kumwa ndipo ankasangalala.
21 And Salomon reigned ouer all kingdomes, from the Riuer vnto the lande of the Philistims, and vnto the border of Egypt, and they brought presents, and serued Salomon all the dayes of his life.
Ndipo Solomoni analamulira mayiko onse kuyambira ku mtsinje wa Yufurate mpaka ku dziko la Afilisti, kukafika mpaka ku malire a dziko la Igupto. Mayikowa ankabweretsa mphatso ndipo anali pansi pa ulamuliro wa Solomoni moyo wake wonse.
22 And Salomons vitailes for one day were thirtie measures of fine floure, and threescore measures of meale:
Chakudya cha tsiku ndi tsiku cha Solomoni chinali madengu 150 a ufa wosalala ndi madengu 300 a mgayiwa,
23 Ten fat oxen, and twentie oxen of the pastures, and an hundreth sheepe, beside hartes, and buckes, and bugles, and fat foule.
ngʼombe khumi zonenepa zodyetsera mʼkhola, ngʼombe za ku busa makumi awiri, ndiponso nkhosa ndi mbuzi 100, pamodzinso ndi mbawala, agwape, mphoyo ndi mbalame zoweta zonona.
24 For he ruled in all the region on the other side of the Riuer, from Tiphsah euen vnto Azzah, ouer all the Kings on the other side the Riuer: and he had peace round about him on euery side.
Pakuti ankalamulira dziko lonse la kumadzulo kwa mtsinje wa Yufurate kuyambira ku Tifisa mpaka ku Gaza, mafumu onse a kumadzulo kwa Mtsinje, ndipo anali pa mtendere ndi mayiko onse ozungulira.
25 And Iudah and Israel dwelt without feare, euery man vnder his vine, and vnder his fig tree, from Dan, euen to Beer-sheba, all the dayes of Salomon.
Pa nthawi ya Solomoni, Yuda ndi Israeli anali pa mtendere, kuyambira ku Dani mpaka ku Beeriseba. Munthu aliyense ankangodzikhalira pansi pa mpesa wake ndi mtengo wake wa mkuyu.
26 And Salomon had fourtie thousande stalles of horses for his charets, and twelue thousand horsemen.
Solomoni anali ndi zipinda 4,000 zodyeramo akavalo okoka magaleta ake ndi anthu 12,000 oyendetsa magaleta.
27 And these officers prouided vitaile for king Salomon, and for all that came to King Salomons table, euery man his moneth, and they suffred to lacke nothing.
Abwanamkubwa a zigawo aja, aliyense pa mwezi wake, ankapereka chakudya cha Mfumu Solomoni ndi cha anthu onse amene ankadya naye. Iwo ankaonetsetsa kuti pasasowe kalikonse.
28 Barley also and strawe for the horses and mules brought they vnto the place where the officers were, euery man according to his charge.
Ankabweretsanso ku malo ake ofunikira muyeso wawo wa barele ndi udzu wa akavalo okoka magaleta ndiponso akavalo ena.
29 And God gaue Salomon wisdome and vnderstanding exceeding much, and a large heart, euen as the sand that is on the sea shore,
Mulungu anamupatsa Solomoni nzeru ndi luntha losaneneka ndipo nzeru zake zinali zochuluka ngati mchenga wa mʼmbali mwa nyanja.
30 And Salomons wisdome excelled the wisedome of all the children of the East and all the wisedome of Egypt.
Nzeru za Solomoni zinali zoposa nzeru za anthu onse a Kummawa ndiponso nzeru zonse za ku Igupto.
31 For he was wiser then any man: yea, then were Ethan the Ezrahite, the Heman, then Chalcol, then Darda the sonnes of Mahol: and he was famous throughout all nations round about.
Iye anali wanzeru kuposa munthu wina aliyense, kuposa ngakhale Etani wa banja la Ezara, Hemani, Kalikoli ndi Darida, ana a Maholi. Ndipo mbiri yake inamveka kwa mitundu yonse ya anthu ozungulira.
32 And Salomon spake three thousand prouerbs: and his songs were a thousand and fiue.
Solomoni anapeka miyambi 3,000 ndi kulemba nyimbo 1,005.
33 And he spake of trees, from the cedar tree that is in Lebanon, euen vnto the hyssope that springeth out of the wall: he spake also of beasts, and of foules, and of creeping thinges, and of fishes.
Iye ankaphunzitsa za mitengo, kuyambira mtengo wa mkungudza wa ku Lebanoni mpaka kachitsamba ka hisope khomera pa khoma. Iye ankaphunzitsanso za nyama ndi mbalame, zinthu zokwawa pansi ndiponso za nsomba.
34 And there came of all people to heare the wisedome of Salomon, from all Kings of the earth, which had heard of his wisedome.
Anthu a mitundu yonse ankabwera kudzamva nzeru za Solomoni. Anthu amenewa ankatumizidwa ndi mafumu onse a dziko lapansi amene anamvapo za nzeru zakezo.

< 1 Kings 4 >