< 1 Kings 3 >

1 Salomon then made affinitie with Pharaoh King of Egypt, and tooke Pharaohs daughter, and brought her into the citie of Dauid, vntill hee had made an ende of buylding his owne house, and the house of the Lord, and the wall of Ierusalem round about.
Solomoni anachita ubale ndi Farao mfumu ya ku Igupto ndipo anakwatira mwana wake wamkazi. Mkaziyo anabwera naye mu Mzinda wa Davide mpaka anatsiriza kumanga nyumba yaufumu ndi Nyumba ya Yehova ndiponso khoma lozungulira Yerusalemu.
2 Only the people sacrificed in the hie places, because there was no house buylt vnto the name of the Lord, vntill those dayes.
Koma anthu ankaperekabe nsembe ku malo achipembedzo osiyanasiyana chifukwa chakuti mpaka pa nthawi imeneyo Dzina la Yehova anali asanalimangire nyumba.
3 And Salomon loued the Lord, walking in the ordinances of Dauid his father: onely he sacrificed and offred incense in the hie places.
Solomoni anaonetsa chikondi chake pa Yehova poyenda motsatira malamulo a abambo ake Davide, kupatula kuti ankapereka nsembe ndi kufukiza lubani ku malo osiyanasiyana achipembedzo.
4 And the King went to Gibeon to sacrifice there, for that was the chiefe hie place: a thousand burnt offrings did Salomon offer vpon that altar.
Mfumu inapita ku Gibiyoni kukapereka nsembe popeza kumeneko ndiye kunali malo oposa malo ofunika kwambiri pachipembedzo. Kumeneko Solomoni anapereka nsembe zopsereza 1,000 pa guwa lansembe.
5 In Gibeon the Lord appeared to Salomon in a dreame by night: and God sayd, Aske what I shall giue thee.
Ku Gibiyoniko Yehova anaonekera kwa Solomoni mʼmaloto usiku, ndipo Mulungu anati, “Pempha chilichonse chimene ukufuna ndipo ndidzakupatsa.”
6 And Salomon sayd, Thou hast shewed vnto thy seruant Dauid my father great mercie, when hee walked before thee in trueth, and in righteousnesse, and in vprightnes of heart with thee: and thou hast kept for him this great mercie, and hast giuen him a sonne, to sit on his throne, as appeareth this day.
Solomoni anayankha kuti, “Inu munaonetsa kukoma mtima kwanu kwakukulu kwa kapolo wanu, abambo anga Davide, chifukwa anali wokhulupirika pamaso panu, wolungama mtima ndiponso wa mtima wangwiro. Inu mukupitirizabe kukoma mtima kwanu kwakukulu kwa iye ndipo mwamupatsa mwana kuti akhale pa mpando wake waufumu lero lino.
7 And now, O Lord my God, thou hast made thy seruant King in steade of Dauid my father: and I am but a yong childe, and know not howe to go out and in.
“Tsopano Inu Yehova Mulungu wanga, mtumiki wanune mwandiyika kukhala mfumu mʼmalo mwa abambo anga Davide. Komatu ndine mwana wamngʼono ndipo sindidziwa kagwiridwe kake ka ntchito yangayi.
8 And thy seruant is in the mids of thy people, which thou hast chosen, euen a great people which cannot be told nor nobred for multitude.
Mtumiki wanu ali pakati pa anthu amene munawasankha, mtundu waukulu, anthu ochuluka kwambiri osatheka kuwawerenga.
9 Giue therefore vnto thy seruant an vnderstanding heart, to iudge thy people, that I may discerne betweene good and bad: for who is able to iudge this thy mightie people?
Choncho mupatseni mtumiki wanu nzeru zolamulira anthu anu ndi kuti azitha kusiyanitsa pakati pa chabwino ndi choyipa. Pakuti ndani amene angathe kulamulira anthu anu ochulukawa?”
10 And this pleased the Lord well, that Salomon had desired this thing.
Ambuye anakondwera kuti Solomoni anapempha zimenezi.
11 And God sayde vnto him, Because thou hast asked this thing, and hast not asked for thy selfe long life, neyther hast asked riches for thy selfe, nor hast asked the life of thine enemies, but hast asked for thy selfe vnderstanding to heare iudgement,
Tsono Mulungu anati kwa Solomoni, “Popeza wapempha zinthu zimenezi osati moyo wautali kapena chuma chako kapena imfa ya adani ako koma nzeru zolamulira anthu mwachilungamo,
12 Beholde, I haue done according to thy wordes: lo, I haue giuen thee a wise and an vnderstanding heart, so that there hath bene none like thee before thee, neither after thee shall arise the like vnto thee.
Ine ndidzakuchitira zimene wapempha. Ndidzakupatsa mtima wanzeru ndi wozindikira zinthu, kotero kuti sipanakhalepo wina wofanana nawe ndipo sipadzapezekanso wina wonga iwe pambuyo pako.
13 And I haue also giuen thee that, which thou hast not asked, both riches and honour, so that among the Kings there shall be none like vnto thee all thy dayes.
Kuwonjeza apo, ndidzakupatsa zimene sunazipemphe: chuma ndi ulemu, kotero kuti pa masiku onse a moyo wako sipadzakhala mfumu yofanana nawe.
14 And if thou wilt walke in my wayes, to keepe mine ordinances and my commandements, as thy father Dauid did walke, I will prolong thy dayes.
Ndipo ngati udzayenda mʼnjira zanga ndi kumvera malamulo anga ndiponso malangizo anga monga abambo ako Davide anachitira, ndidzakupatsa moyo wautali.”
15 And when Salomon awoke, behold, it was a dreame, and he came to Ierusalem, and stoode before the Arke of the couenant of the Lord, and offred burnt offrings and made peace offrings, and made a feast to all his seruants.
Kotero Solomoni anadzuka ndipo anazindikira kuti anali maloto. Iye anabwerera ku Yerusalemu nakayimirira patsogolo pa Bokosi la Chipangano la Ambuye ndipo anapereka nsembe zopsereza ndi nsembe zachiyanjano. Kenaka anakonzera phwando atumiki ake onse.
16 Then came two harlots vnto the King, and stoode before him.
Nthawi ina amayi awiri adama anabwera kwa mfumu ndipo anayima pamaso pake.
17 And the one woman sayd, Oh my lorde, I and this woman dwell in one house, and I was deliuered of a childe with her in the house.
Mmodzi mwa amayiwo anati, “Mbuye wanga, mayi uyu ndi ine timakhala nyumba imodzi. Ine ndinabala mwana tili limodzi ndi mnzangayu.
18 And the third day after that I was deliuered, this woman was deliuered also: and we were in the house together: no stranger was with vs in the house, saue we twaine.
Tsiku lachitatu ine nditabala mwana, mnzangayunso anabereka mwana wake. Tinalipo awiriwiri mʼnyumbamo ndipo munalibe wina aliyense.
19 And this womans sonne died in the night: for she ouerlay him.
“Nthawi ya usiku mwana wa mnzangayu anafa chifukwa anamugonera.
20 And she rose at midnight, and tooke my sonne from my side, while thine handmaide slept, and layde him in her bosome, and layde her dead sonne in my bosome.
Tsono iyeyu anadzuka pakati pa usiku, natenga mwana wanga ku mimba kwanga pamene ine mdzakazi wanu ndinali mʼtulo. Anamuyika mwanayo ku mimba kwake ndi kuyika mwana wake wakufayo ku mimba kwanga.
21 And when I rose in the morning to giue my sonne sucke, beholde, he was dead: and when I had well considered him in the morning, beholde, it was not my sonne, whom I had borne.
Mmawa nditadzuka kuti ndiyamwitse mwana wanga ndinapeza kuti ndi wakufa! Koma kutacha nditamuyangʼanitsitsa ndinaona kuti si mwana amene ine ndinabala.”
22 Then the other woman sayd, Nay, but my sonne liueth, and thy sonne is dead. Againe she sayde, No, but thy sonne is dead, and mine aliue: thus they spake before the King.
Koma mayi winayo anati, “Ayi! Mwana wamoyoyu ndi wanga, mwana wakufayu ndi wako.” Koma mayi woyambayo analimbikira kuti. “Ayi! Mwana wakufayu ndi wako; wamoyoyu ndi wanga.” Motero akaziwa anatsutsana pamaso pa mfumu.
23 Then sayde the King, She sayth, This that liueth is my sonne, and the dead is thy sonne: and the other sayth, Nay, but the dead is thy sonne, and the liuing is my sonne.
Pamenepo mfumu inati, “Wina akuti, ‘Mwana wanga ndi wamoyoyu ndipo mwana wako ndi wakufayu,’ pamene winanso akuti, ‘Ayi! Mwana wako ndi wakufayu wanga ndi wamoyoyu.’”
24 Then the King said, Bring me a sworde: and they brought out a sworde before the King.
Pamenepo mfumu inati, “Patseni lupanga.” Ndipo anabwera nalo lupanga kwa mfumu.
25 And the King sayde, Deuide ye the liuing child in twaine, and giue the one halfe to the one, and the other halfe to the other.
Tsono mfumu inagamula kuti, “Muduleni pakati mwana wamoyoyu ndipo wina mumupatse gawo limodzi, gawo linalo mumupatse winayo.”
26 Then spake the woman, whose the liuing child was, vnto the King, for her compassion was kindled toward her sonne, and she sayde, Oh my lorde, giue her the liuing childe, and slay him not: but the other sayde, Let it be neither mine nor thine, but deuide it.
Mayi amene mwana wake anali moyo anagwidwa ndi chisoni chifukwa cha mwana wakeyo ndipo anawuza mfumu kuti, “Chonde mbuye wanga, mupatseni mnzangayu mwana wamoyoyu! Musamuphe!” Koma winayo anati, “Ayi, asandipatse ine kapena iwe. Muduleni pakati!”
27 Then the King answered, and sayde, Giue her the liuing childe, and slay him not: this is his mother.
Choncho mfumu inagamula kuti, “Perekani mwana wamoyoyu kwa mayi woyambayu. Musamuphe, iyeyu ndiye mayi wake wa mwanayu.”
28 And all Israel heard the iudgement, which the King had iudged, and they feared the King: for they sawe that the wisedome of God was in him to doe iustice.
Pamene Aisraeli onse anamva za chigamulo chimene mfumu inapereka, anaopa mfumuyo kwambiri, chifukwa anaona kuti mfumu inali ndi nzeru zochokera kwa Mulungu zoweruzira mwachilungamo.

< 1 Kings 3 >