< 1 Kings 20 >

1 Then Ben-hadad the King of Aram assembled all his armie, and two and thirtie Kings with him, with horses, and charets, and went vp and besieged Samaria, and fought against it.
Tsono Beni-Hadadi mfumu ya ku Aramu inasonkhanitsa magulu ake onse a ankhondo. Iye pamodzi ndi mafumu 32, akavalo awo ndi magaleta awo, anapita kukawuzungulira mzinda wa Samariya ndi kuwuthira nkhondo.
2 And he sent messengers to Ahab King of Israel, into the citie,
Iye anatuma amithenga ake mu mzindamo kwa Ahabu mfumu ya Israeli, kukanena kuti,
3 And sayd vnto him, Thus sayth Ben-hadad, Thy siluer and thy golde is mine: also thy women, and thy fayre children are mine.
“Beni-Hadadi akuti, ‘Siliva wako ndi golide wako ndi wanga, ndipo akazi ako okongola ndi ana ako ndi anganso.’”
4 And the King of Israel answered, and sayd, My lord King, according to thy saying, I am thine, and all that I haue.
Mfumu ya Israeli inayankha kuti, “Monga mmene mwanenera, mbuye wanga mfumu, ine pamodzi ndi zonse zomwe ndili nazo ndi zanu.”
5 And when the messengers came againe, they said, Thus commandeth Ben-hadad, and saith, When I shall send vnto thee, and command, thou shalt deliuer me thy siluer and thy golde, and thy women, and thy children,
Amithenga aja anabwereranso kwa Ahabu ndipo anamuwuza kuti, “Beni-Hadadi akuti, ‘Ine ndinakulamula kuti undipatse siliva wako ndi golide wako, akazi ako ndi ana ako.
6 Or els I will sende my seruants vnto thee by to morow this time: and they shall search thine house, and the houses of thy seruants: and whatsoeuer is pleasant in thine eyes, they shall take it in their handes, and bring it away.
Koma mawa nthawi ngati yomwe ino ndidzatuma atumiki anga kudzafufuza mʼnyumba yako yaufumu ndi nyumba za akuluakulu ako. Iwo adzatenga chilichonse chimene umachidalira ndi kupita nacho.’”
7 Then the King of Israel sent for all the Elders of the land, and sayd, Take heede, I pray you, and see how he seeketh mischiefe: for he sent vnto me for my wiues, and for my children, and for my siluer, and for my golde, and I denyed him not.
Pamenepo mfumu ya Israeli inayitanitsa akuluakulu a mʼdzikomo niwawuza kuti, “Taonani momwe munthuyu akufunira kutibweretsera mavuto! Atatumiza mawu oti ndimupatse akazi anga ndi ana anga, siliva wanga ndi golide wanga, ine sindinamukanize.”
8 And all the Elders, and all the people sayd to him, Hearken not vnto him, nor consent.
Akuluakulu onse ndi anthu onse anayankha kuti, “Musamumvere kapena kuvomereza zofuna zake.”
9 Wherefore hee sayde vnto the messengers of Ben-hadad, Tell my lorde the King, All that thou didddest sende for to thy seruant at the first time, that I will doe, but this thing I may not do. And the messengers departed, and brought him an answere.
Tsono Ahabu anayankha amithenga a Beni-Hadadi kuti, “Kamuwuzeni mbuye wanga mfumu kuti, ‘Mtumiki wanu adzachita zonse zimene munazifuna nthawi yoyamba ija, koma izi mwazifunazi sindingazikwanitse.’” Iwo anachoka nakapereka yankho kwa Beni-Hadadi.
10 And Ben-hadad sent vnto him, and sayde, The gods do so to me and more also, if the dust of Samaria be ynough to all the people that follow me, for euery man an handfull.
Pamenepo Beni-Hadadi anatumizanso uthenga wina kwa Ahabu kuti, “Milungu indilange koopsa, ngati mu Samariya mudzakhale fumbi loti nʼkudzaza dzanja la aliyense wa anthu anga.”
11 And the King of Israel answered, and sayd, Tell him, Let not him that girdeth his harneis, boast himselfe, as he that putteth it off.
Mfumu ya Israeli inayankha kuti, “Kamuwuzeni kuti, ‘Mwamuna mnzako nʼpachulu, nʼkulinga utakwerapo.’”
12 And when he heard that tidings, as he was with the Kings drinking in the pauilions, he sayd vnto his seruants, Bring forth your engines, and they set them against the citie.
Beni-Hadadi anamva uthenga umenewu pamene iye ankamwa ndi mafumu anzake mʼmatenti awo, ndipo analamula anthu ake kuti, “Konzekerani kukathira nkhondo.” Choncho anakonzekera kukathira nkhondo mzindawo.
13 And beholde, there came a Prophet vnto Ahab King of Israel, saying, Thus sayeth the Lord, Hast thou seene all this great multitude? beholde, I will deliuer it into thine hande this day, that thou mayest knowe, that I am the Lord.
Ndipo taonani, mneneri wina anabwera kwa Ahabu mfumu ya Israeli nadzalengeza kuti, “Yehova akuti, ‘Kodi ukuchiona chigulu chachikulu cha ankhondochi? Taona, ndikuchipereka chimenechi lero mʼdzanja lako, ndipo pamenepo udzadziwa kuti Ine ndine Yehova.’”
14 And Ahab sayd, By whome? And he sayde, Thus sayth the Lord, By the seruants of the princes of the prouinces. He sayde againe, Who shall order the battel? And he answered, Thou.
Ahabu anafunsa kuti, “Koma ndani adzachita zimenezi?” Mneneri anayankha kuti, “Yehova akuti, ‘Adzachita zimenezi ndi asilikali a nduna za mʼzigawo.’” Ndipo iye anafunsa kuti, “Kodi ndani adzayambe nkhondoyi?” Mneneriyo anayankha kuti, “Ndinu.”
15 Then he nombred the seruantes of the princes of the prouinces, and they were two hundreth, two and thirtie: and after them he nombred the whole people of all the children of Israel, euen seuen thousand.
Choncho Ahabu anawerenga asilikali achinyamata a nduna za mʼzigawo ndipo onse analipo 232. Ndipo anawerenganso ankhondo a ku Israeli ndipo onse analipo 7,000.
16 And they went out at noone: but Ben-hadad did drinke till he was drunken in the tentes, both he and the Kings: for two and thirtie Kings helped him.
Iwo ananyamuka nthawi yamasana pamene Beni-Hadadi ndi mafumu 32 othandizana naye ankamwa mpaka kuledzera mʼmatenti awo.
17 So the seruants of the princes of the prouinces went out first: and Ben-hadad sent out, and they shewed him, saying, There are men come out of Samaria.
Asilikali achinyamata a nduna za mʼzigawo ndiwo amene anayamba kupita ku nkhondo. Nthawi imeneyi Beni-Hadadi nʼkuti atatumiza anthu oti akazonde, amene anadzafotokoza kuti, “Anthu ankhondo akubwera kuchokera ku Samariya.”
18 And he sayde, Whether they be come out for peace, take them aliue: or whether they bee come out to fight, take them yet aliue.
Iye anati, “Kaya akubwera mwamtendere kapena mwankhondo, muwagwire amoyo.”
19 So they came out of the citie, to wit, the seruants of the princes of the prouinces, and the hoste which followed them.
Choncho asilikali achinyamata a nduna za mʼzigawo anatuluka mu mzinda, gulu lankhondo lili pambuyo pawo.
20 And they slew euery one his enemie: and the Aramites fled, and Israel pursued them: but Ben-hadad ye King of Aram escaped on an horse with his horsemen.
Ndipo aliyense wa iwo anapha munthu wake. Ataona izi, Aaramu anathawa Aisraeli ali pambuyo pawo kuwapirikitsa. Koma Beni-Hadadi mfumu ya ku Aaramu anathawa atakwera pa kavalo pamodzi ndi ankhondo ena okweranso pa akavalo.
21 And the King of Israel went out, and smote the horses and charets, and with a great slaughter slew he the Aramites.
Mfumu ya Israeli inapita chitsogolo ndi kugwira akavalo ndi magaleta ndipo Aaramu ambiri anaphedwa.
22 (For there had come a Prophet to the King of Israel, and had sayd vnto him, Goe, be of good courage, and consider, and take heede what thou doest: for when the yeere is gone about, the King of Aram wil come vp against thee)
Zitachitika izi, mneneri wina anabwera kwa mfumu ya Israeli ndipo anati, “Mulimbike ndipo muganize bwino zoti mudzachite, chifukwa chaka chikudzachi mfumu ya Aramu idzakuthiraninso nkhondo.”
23 Then the seruants of the King of Aram said vnto him, Their gods are gods of the moutaines, and therefore they ouercame vs: but let vs fight against them in the playne, and doubtlesse we shall ouercome them.
Nthawi imeneyi, akuluakulu a mfumu ya Aramu anamulangiza kuti, “Milungu ya anthu a ku Israeli ndi milungu ya mʼmapiri. Nʼchifukwa chake anali ndi mphamvu zotipambana ife. Koma ngati tidzamenyana nawo ku chigwa, ndithudi ife tidzakhala ndi mphamvu kuposa iwo.
24 And this doe, Take the Kings away, euery one out of his place, and place captaines for them.
Inu chitani izi: chotsani mafumu onse pa maudindo awo ndipo mʼmalo mwawo muyikemo atsogoleri a ankhondo.
25 And nomber thy selfe an armie, like the armie that thou hast lost, with such horses, and such charets, and we wil fight against them in the plaine, and doubtlesse we shall ouercome them: and he hearkened vnto their voyce, and did so.
Musonkhanitsenso gulu lankhondo lofanana ndi lomwe linaphedwa lija, akavalo monga omwe anaphedwa aja, ndi magaleta monga omwe anawonongedwa aja, kuti tikamenyane ndi Israeli ku chigwa. Pamenepo, ife tidzapambana iwowo.” Beni-Hadadi anagwirizana nawo ndipo anachita momwemo.
26 And after the yeere was gone about, Ben-hadad nombred the Aramites, and went vp to Aphek to fight against Israel.
Chaka chinacho Beni-Hadadi anasonkhanitsa Aaramu, napita ku Afeki kukamenyana ndi Israeli.
27 And the children of Israel were nombred, and were all assembled and went against them, and the children of Israel pitched before them, like two litle flockes of kiddes: but the Aramites filled the countrey.
Aisraeli atasonkhananso, napatsidwa zakudya zawo anapita kukakumana nawo. Aisraeli anamanga misasa yawo moyangʼanana ndi Aaramu ndipo ankaoneka ngati timagulu tiwiri ta mbuzi, pomwe Aaramu anali atakuta dera lonselo.
28 And there came a man of God, and spake vnto the King of Israel, saying, Thus sayeth the Lord, Because the Aramites haue sayd, The Lord is the God of the mountaines, and not God of the valleis, therefore will I deliuer all this great multitude into thine hand, and ye shall know that I am the Lord.
Munthu wa Mulungu anabwera, nawuza mfumu ya Israeli kuti, “Yehova akuti, ‘Popeza Aaramu akuganiza kuti Yehova ndi mulungu wa ku mapiri, osati wa ku zigwa, Ine ndidzapereka chigulu chonsechi kwa iwe, ndipo iwe udzadziwa kuti Ine ndine Yehova.’”
29 And they pitched one ouer against the other seuen dayes, and in the seuenth day the battel was ioyned: and the children of Israel slew of the Aramites an hundreth thousand footemen in one day.
Kwa masiku asanu ndi awiri anakhala moyangʼanana mʼmisasa yawo, ndipo pa tsiku lachisanu ndi chiwiri nkhondo inayambika. Aisraeli anapha Aaramu okwana 100,000 tsiku limodzi lokha.
30 But the rest fled to Aphek into the citie: and there fel a wall vpon seuen and twentie thousand men that were left: and Ben-hadad fled into the citie, and came into a secret chamber.
Ena onse otsala anathawira ku Afeki, kumene khoma linagwera anthu 27,000. Ndipo Beni-Hadadi anathawira mu mzinda, nakabisala mʼchipinda chamʼkati.
31 And his seruants sayd vnto him, Beholde nowe, we haue heard say that the Kings of the house of Israel are mercifull Kings: we pray thee, let vs put sacke cloth about our loynes, and ropes about our heads, and goe out to the King of Israel: it may be that he will saue thy life.
Atumiki ake anamuwuza kuti, “Taonani, ife tamva kuti mafumu a fuko la Israeli ndi achifundo. Tiyeni tipite kwa mfumu ya ku Israeli titavala ziguduli mʼchiwuno mwathu ndi kumanga zingwe mʼmakosi mwathu. Mwina iye sakakuphani.”
32 Then they gyrded sackecloth about their loynes, and put ropes about their heads, and came to the King of Israel, and sayd, Thy seruant Ben-hadad sayth, I pray thee, let me liue: and he sayd, Is he yet aliue? he is my brother.
Atavala ziguduli mʼchiwuno mwawo ndi kumanga zingwe mʼmakosi mwawo, anapita kwa mfumu ya ku Israeli ndipo anayiwuza kuti, “Mtumiki wanu Beni-Hadadi akunena kuti, ‘Chonde loleni kuti ndikhale moyo.’” Mfumu inayankha kuti, “Kodi iye akanali ndi moyo? Iye ujatu ndi mʼbale wanga.”
33 Now the men tooke diliget heede, if they could catch any thing of him, and made haste, and sayd, Thy brother Ben-hadad. And he sayd, Go, bring him. So Ben-hadad came out vnto him, and he caused him to come vp vnto the chariot.
Anthuwo ankaganiza kuti mawuwo anali abwino ndipo anavomereza mawuwa mofulumira. Iwo anati, “Inde, Beni-Hadadi ndi mʼbale wanu!” Mfumu inati, “Pitani kamutengeni.” Beni-Hadadi atatuluka, Ahabu anamukweza mʼgaleta lake.
34 And Ben-hadad sayd vnto him, The cities, which my father tooke from thy father, I wil restore, and thou shalt make streetes for thee in Damascus, as my father did in Samaria. Then said Ahab, I will let thee goe with this couenant. So he made a couenant with him, and let him goe.
Beni-Hadadi anawuza Ahabu kuti, “Ndidzabweza mizinda imene abambo anga analanda abambo anu. Ndipo mutha kumanga nyumba zanu zamalonda mu Damasiko, monga anachitira abambo anga ku Samariya.” Ahabu anati, “Chifukwa cha mgwirizano umenewu, ine ndidzakumasula.” Choncho anachita naye mgwirizano, ndipo anamulola kuti apite.
35 Then a certaine man of the children of the Prophets sayd vnto his neighbour by the comandement of the Lord, Smite me, I pray thee. But the man refused to smite him.
Molamulidwa ndi Yehova, mmodzi mwa ana a aneneri anawuza mnzake kuti, “Chonde, menye ndi chida chako,” koma mnzakeyo anakana.
36 Then sayd he vnto him, Because thou hast not obeyed the voyce of the Lord, beholde, as soone as thou art departed from me, a lyon shall slay thee. So when he was departed from him, a lyon found him and slew him.
Choncho mneneriyo anati, “Chifukwa sunamvere Yehova, ukangochoka pano, mkango ukupha.” Ndipo munthuyo atangochoka pamenepo, mkango unamupeza ndi kumupha.
37 Then he founde another man, and sayde, Smite mee, I pray thee. And the man smote him, and in smiting wounded him.
Mneneriyo anapeza munthu wina ndipo anamuwuza kuti, “Chonde, menye.” Choncho munthuyo anamumenya ndi kumuvulaza.
38 So the Prophet departed, and wayted for the King by the way, and disguised himselfe with ashes vpon his face.
Pamenepo mneneriyo anapita nakayima pa msewu kudikirira mfumu. Iye anadzibisa nakulunga nsalu nkhope yake.
39 And when the King came by, he cried vnto the King, and said, Thy seruant went into the middes of the battel: and beholde, there went away a man, whom another man brought vnto me, and sayd, Keepe this man: if he be lost, and want, thy life shall go for his life, or els thou shalt pay a talent of siluer.
Mmene mfumu inkadutsa pamenepo, mneneriyo anafuwula kwa mfumuyo kuti, “Ine mtumiki wanu ndinalowa pakati pa nkhondo, ndipo munthu wina anabwera kwa ine atatenga mmodzi mwa anthu ogwidwa pa nkhondo, nandiwuza kuti, ‘Sunga munthu uyu. Ngati asowa, ndiye kuti ndidzakupha, kapena udzalipira ndalama 3,000 za siliva.’
40 And as thy seruant had here and there to do, he was gone: And the King of Israel said vnto him, So shall thy iudgement be: thou hast giuen sentence.
Pamene ine mtumiki wanu ndinali wotanganidwa apa ndi apa, munthuyo anasowa.” Mfumu ya Israeli inati, “Chimenechi ndiye chilango chako. Iwe wadziweruza wekha.”
41 And hee hasted, and tooke the ashes away from his face: and the King of Israel knewe him that he was of the Prophets:
Pamenepo mneneriyo anachotsa msangamsanga nsalu yomwe anakulunga pa nkhope yake, ndipo mfumu ya Israeli inamuzindikira kuti ndi mmodzi mwa aneneri.
42 And he said vnto him, Thus saith the Lord, Because thou hast let goe out of thine handes a man whom I appoynted to dye, thy life shall goe for his life, and thy people for his people.
Iye anawuza mfumu kuti, “Yehova akuti, ‘Chifukwa chakuti mwamasula munthu amene Ine ndinati ndi woyenera kuphedwa, inuyo ndi amene mudzaphedwe mʼmalo mwa iyeyo, anthu anu mʼmalo mwa anthu ake.’”
43 And the King of Israel went to his house heauie and in displeasure, and came to Samaria.
Mwachisoni ndi mokwiya, mfumu ya Israeli inapita ku nyumba yake yaufumu ku Samariya.

< 1 Kings 20 >