< 1 Kings 12 >
1 And Rehoboam went to Shechem: for al Israel were come to Sheche, to make him king
Rehobowamu anapita ku Sekemu, pakuti Aisraeli onse nʼkuti atapita kumeneko kukamulonga ufumu.
2 And whe Ieroboam ye sonne of Nebat heard of it (who was yet in Egypt, whither Ieroboam had fled from king Salomon, and dwelt in Egypt)
Yeroboamu mwana wa Nebati anamva zimenezi. Nthawi imeneyo nʼkuti Yeroboamuyo akukhala ku Igupto, pakuti atathawa Mfumu Solomoni iyeyo anakakhala ku Igupto.
3 Then they sent and called him: and Ieroboam and all the Congregation of Israel came, and spake vnto Rehoboam, saying,
Tsono anthu anayitanitsa Yeroboamu, ndipo iye pamodzi ndi gulu lonse la ku Israeli anapita kwa Rehobowamu ndipo anamuwuza kuti,
4 Thy father made our yoke grieuous: now therefore make thou the grieuous seruitude of thy father, and his sore yoke which he put vpon vs, lighter, and we will serue thee.
“Abambo anu anatisenzetsa goli lolemetsa kwambiri, koma inu chepetsani ntchito yowawa pa ife ndipo peputsani goli lolemetsa limene anatisenzetsa. Mukatero tidzakutumikirani.”
5 And he said vnto them, Depart yet for three dayes, then come againe to me. And the people departed.
Rehobowamu anayankha kuti, “Pitani, ndipo pakatha masiku atatu, mudzabwerenso.” Choncho anthuwo anapitadi.
6 And King Rehoboam tooke counsell with the olde men that had stande before Salomon his father, while he yet liued, and sayde, What counsell giue ye, that I may make an answere to this people?
Ndipo Mfumu Rehobowamu anapempha nzeru kwa akuluakulu amene ankatumikira Solomoni abambo ake pamene anali ndi moyo. Iye anawafunsa kuti, “Kodi mungandilangize zotani kuti ndiwayankhe anthu amenewa?”
7 And they spake vnto him, saying, If thou be a seruant vnto this people this day, and serue them, and answere them, and speake kinde wordes to them, they will be thy seruants for euer.
Iwo anayankha kuti, “Ngati lero mudzakhala mtumiki wa anthu amenewa ndi kuwatumikira ndipo mukawayankha bwino, iwowo adzakhala atumiki anu nthawi zonse.”
8 But he forsooke the counsell that the olde men had giuen him, and asked counsell of the yong men that had bene brought vp with him, and waited on him.
Koma Rehobowamu anakana malangizo amene akuluakuluwo anamupatsa ndipo anafunsira nzeru kwa anyamata anzake amene anakulira nawo limodzi omwe ankamutumikira.
9 And he said vnto them, What counsell giue ye, that we may answere this people, which haue spoken to me, saying, Make the yoke, which thy father did put vpon vs, lighter?
Iye anawafunsa kuti, “Kodi malangizo anu ngotani? Kodi ndiwayankhe chiyani anthu amene akunena kwa ine kuti, ‘Peputsani goli limene abambo anu anatisenzetsa’?”
10 Then the yong men that were brought vp with him, spake vnto him, saying, Thus shalt thou say vnto this people, that haue spoken vnto thee, and said, Thy father hath made our yoke heauie, but make thou it lighter vnto vs: euen thus shalt thou say vnto them, My least part shalbe bigger then my fathers loynes.
Anyamata anzake amene anakula nawo limodzi aja anamuyankha kuti, “Anthu amene ananena kwa iwe kuti, ‘Abambo anu anatisenzetsa goli lolemetsa, koma inu peputsani goli lathu,’ uwawuze kuti ‘Chala changa chakanise nʼchachikulu kupambana chiwuno cha abambo anga.
11 Now where as my father did burden you with a grieuous yoke, I will yet make your yoke heauier: my father hath chastised you with rods, but I will correct you with scourges.
Abambo anga ankakusenzetsani goli lolemetsa koma ine ndidzachititsa kuti likhale lolemera kwambiri. Abambo anga ankakukwapulani ndi zikoti wamba koma ine ndidzakukwapulani ndi zinkhanira.’”
12 Then Ieroboam and all the people came to Rehoboam the third day, as the king had appointed, saying, Come to me againe ye thirde day.
Patapita masiku atatu, Yeroboamu pamodzi ndi anthu onse anabwera kwa Rehobowamu, monga momwe inanenera mfumu kuti, “Mudzabwere pakatha masiku atatu.”
13 And the king answered the people sharpely, and left the old mens counsell that they gaue him,
Mfumuyo inawayankha anthuwo mwankhanza. Kukana malangizo amene akuluakulu anayipatsa.
14 And spake to them after the counsell of the yong men, saying, My father made your yoke grieuous, and I will make your yoke more grieuous: my father hath chastised you with rods, but I will correct you with scourges.
Anatsatira malangizo amene anyamata anzake anamupatsa ndipo anati “Abambo anga ankakusenzetsani goli lolemetsa. Ine ndidzachititsa kuti likhale lolemera kwambiri. Abambo anga ankakukwapulani ndi zikoti wamba koma ine ndidzakukwapulani ndi zinkhanira.”
15 And the King hearkened not vnto the people: for it was the ordinance of the Lord, that he might perfourme his saying, which the Lord had spoken by Ahiiah the Shilonite vnto Ieroboam the sonne of Nebat.
Choncho mfumu sinamvere pempho la anthuwo, pakuti zinthu izi zinali zochokera kwa Yehova, kukwaniritsa mawu amene Yehova anayankhula kwa Yeroboamu mwana wa Nebati kudzera mwa Ahiya wa ku Silo.
16 So when all Israel sawe that the King regarded them not, the people answered the King thus, saying, What portion haue we in Dauid? we haue none inheritance in the sonne of Ishai. To your tents, O Israel: nowe see to thine owne house, Dauid. So Israel departed vnto their tents.
Aisraeli onse ataona kuti mfumu yakana kumva zopempha zawo, iwo anayankha mfumu kuti, “Kodi ife tili ndi gawo lanji mwa Davide, ndi gawo lanjinso mwa mwana wa Yese? Inu Aisraeli, bwererani ku matenti anu! Ziyangʼanira nyumba yako, Iwe Davide!” Kotero Aisraeli anachoka napita ku nyumba zawo.
17 Howbeit ouer the children of Israel, which dwelt in the cities of Iudah, did Rehoboam reigne still.
Koma Aisraeli amene ankakhala mʼmizinda ya Yuda ankalamuliridwa ndi Rehobowamu.
18 Nowe the King Rehoboam sent Adoram the receiuer of the tribute, and all Israel stoned him to death: then King Rehoboam made speede to get him vp to his charet, to flee to Ierusalem.
Mfumu Rehobowamu anatuma Adoramu amene ankayangʼanira ntchito yathangata, koma Aisraeli onse anamugeda ndi miyala mpaka kumupha. Koma Mfumu Rehobowamu anakwera msangamsanga galeta wake nathawira ku Yerusalemu.
19 And Israel rebelled against the house of Dauid vnto this day.
Choncho Aisraeli akhala akuwukira nyumba ya Davide mpaka lero lino.
20 And when all Israel had heard that Ieroboam was come againe, they sent and called him vnto the assemblie, and made him King ouer all Israel: none followed the house of Dauid, but the tribe of Iudah onely.
Aisraeli onse atamva kuti Yeroboamu wabwerera kuchokera ku Igupto, anatumiza mawu okamuyitana kuti abwere ku msonkhano ndipo anamuyika kukhala mfumu ya Aisraeli onse. Fuko la Yuda lokha ndi lomwe linkatsatira nyumba ya Davide.
21 And when Rehoboam was come to Ierusalem, he gathered all the house of Iudah with the tribe of Beniamin an hundreth and foure score thousand of chosen men (which were good warriours) to fight against the house of Israel, and to bring the kingdome againe to Rehoboam the sonne of Salomon.
Rehobowamu atafika ku Yerusalemu, anasonkhanitsa nyumba yonse ya Yuda ndi fuko la Benjamini, nasankha ankhondo okwanira 180,000, kuti akamenyane ndi nyumba ya Israeli kuti amubwezere Rehobowamu mwana wa Solomoni ufumu wake.
22 But the worde of God came vnto Shemaiah the man of God, saying,
Koma Mulungu anayankhula ndi Semaya, munthu wa Mulungu kuti,
23 Speake vnto Rehoboam the sonne of Salomon King of Iudah, and vnto all the house of Iudah and Beniamin, and the remnant of the people, saying,
“Nena kwa Rehobowamu mwana wa Solomoni mfumu ya Yuda, kwa nyumba yonse ya Yuda ndi Benjamini, ndiponso kwa anthu ena onse kuti,
24 Thus saith the Lord, Ye shall not go vp, nor fight against your brethren the children of Israel: returne euery man to his house: for this thing is done by me. They obeyed therefore the worde of the Lord and returned, and departed, according to the worde of the Lord.
‘Yehova akuti: Musapite kukamenyana ndi abale anu Aisraeli. Aliyense wa inu abwerere kwawo, pakuti zimenezi ndachita ndine.’” Choncho anthuwo anamvera mawu a Yehova ndi kubwerera kwawo, monga analamulira Yehova.
25 Then Ieroboam built Shechem in mount Ephraim, and dwelt therein, and went from thence, and built Penuel.
Tsono Yeroboamu anamanga mzinda wa Sekemu mʼdziko la mapiri la Efereimu ndipo anakhala kumeneko. Kuchokera kumeneko anapita kukamanga mzinda wa Penueli.
26 And Ieroboam thought in his heart, Nowe shall the kingdome returne to the house of Dauid.
Yeroboamu anaganiza mu mtima mwake kuti, “Ndithu, ufumuwu udzabwereranso ku nyumba ya Davide.
27 If this people goe vp and doe sacrifice in the house of the Lord at Ierusalem, then shall the heart of this people turne againe vnto their lorde, euen to Rehoboam King of Iudah: so shall they kill me and goe againe to Rehoboam King of Iudah.
Ngati anthuwa azipitabe kukapereka nsembe ku Nyumba ya Yehova ku Yerusalemu, adzayambanso kutsatira mbuye wawo Rehobowamu, mfumu ya Yuda. Adzandipha ndi kubwerera kwa Mfumu Rehobowamu.”
28 Whereupon the King tooke counsell, and made two calues of golde, and saide vnto them, It is too much for you to goe vp to Ierusalem: beholde, O Israel, thy gods, which brought thee vp out of the lande of Egypt.
Itapempha nzeru, mfumuyo inapanga mafano awiri a ana angʼombe. Mfumuyo inati kwa anthuwo, “Mwakhala mukupita ku Yerusalemu nthawi yayitali. Iwe Israeli, nayi milungu yako imene inakutulutsa mʼdziko la Igupto.”
29 And he set the one in Beth-el, and the other set he in Dan.
Fano lina analiyika ku Beteli ndipo lina analiyika ku Dani.
30 And this thing turned to sinne: for the people went (because of the one) euen to Dan.
Ndipo zimenezi zinachimwitsa anthu pakuti anthu ankapita mpaka ku Dani kukapembedza fano limene linali kumeneko.
31 Also he made an house of hie places, and made Priestes of the lowest of the people, which were not of the sonnes of Leui.
Yeroboamu anamanga Nyumba za Mulungu pa malo azipembedzo nasankha ansembe kuchokera pakati pa anthu wamba, ngakhale sanali Alevi.
32 And Ieroboam made a feast the fifteenth day of the eight moneth, like vnto the feast that is in Iudah, and offred on the altar. So did he in Beth-el and offered vnto the calues that he had made: and he placed in Beth-el the Priestes of the hie places, which he had made.
Iye anakhazikitsa chikondwerero pa tsiku la 15 la mwezi wachisanu ndi chitatu, lofanana ndi tsiku la chikondwerero cha ku Yuda, ndipo ankapereka nsembe pa guwa. Izi ankachita ku Beteli, kupereka nsembe kwa ana angʼombe amene anapanga. Ndipo ku Beteliko anayikako ansembe pa malo achipembedzo amene anamanga.
33 And he offered vpon the altar, which he had made in Beth-el, the fifteenth day of the eight moneth, (euen in the moneth which he had forged of his owne heart) and made a solemne feast vnto the children of Israel: and he went vp to the altar, to burne incense.
Tsiku la 15 la mwezi wachisanu ndi chitatu, mwezi umene anawusankha yekha, anapereka nsembe pa guwa limene analimanga ku Beteli. Motero anakhazikitsa chikondwerero cha Aisraeli ndipo iye ankapita kukapereka nsembe yofukiza lubani pa guwa.