< 1 Chronicles 7 >

1 And the sonnes of Issachar were Tola and Puah, Iashub, and Shimron, foure,
Ana a Isakara anali awa: Tola, Puwa, Yasubu ndi Simironi ndipo onse analipo anayi.
2 And the sonnes of Tola, Vzzi, and Rephaiah, and Ieriel, and Iahmai, and Iibsam, and Shemuel, heads in the housholdes of their fathers. Of Tola were valiant men of warre in their generations, whose nomber was in the dayes of Dauid two and twentie thousand, and sixe hundreth.
Ana a Tola ndi awa: Uzi, Refaya, Yerieli, Yahimai, Ibisamu ndi Samueli. Awa anali atsogoleri a mabanja awo. Pa nthawi ya ulamuliro wa Davide zidzukulu za Tola zomwe zinali anthu odziwa kumenya nkhondo zinalipo 22,600.
3 And the sonne of Vzzi was Izrahaiah, and the sonnes of Izrahaiah, Michael, and Obadiah, and Ioel, and Isshiah, fiue men all princes.
Mwana wa Uzi anali Izirahiya. Ana a Izirahiya anali: Mikayeli, Obadiya, Yoweli ndi Isiya. Onse asanu anali atsogoleri a mabanja.
4 And with them in their generations after the houshold of their fathers were bandes of men of warre for battel, sixe and thirtie thousand: for they had many wiues and children.
Monga mwa chiwerengero cha mabanja awo, panali anthu 36,000 odziwa kumenya nkhondo, pakuti iwo anali ndi akazi ndi ana ambiri.
5 And their brethren among all the families of Issachar were valiant men of warre, rekoned in all by their genealogies foure score and seuen thousand.
Abale awo onse a mʼbanja la Isakara amene anali odziwa kumenya nkhondo analipo 87,000, olembedwa potsata mibado yawo.
6 The sonnes of Beniamin were Bela, and Becher, and Iediael, three.
Ana atatu a Benjamini anali awa: Bela, Bekeri ndi Yediaeli.
7 And the sonnes of Bela, Ezbon, and Vzzi, and Vzziel, and Ierimoth, and Iri, fiue heads of the housholds of their fathers, valiant men of warre, and were rekoned by their genealogies, two and twentie thousand and thirtie and foure.
Ana a Bela anali awa: Eziboni, Uzi, Uzieli, Yerimoti ndi Iri. Iwowa anali atsogoleri a mabanja awo ndipo onse pamodzi analipo asanu. Pa mndandanda wa mʼbado wawo panali anthu 22,034 odziwa kumenya nkhondo.
8 And the sonnes of Becher, Zemirah, and Ioash, and Eliezer, and Elioenai, and Omri, and Ierimoth, and Abiah, and Anathoth, and Alameth: all these were the sonnes of Becher.
Ana a Bekeri anali awa: Zemira, Yowasi, Eliezara, Eliyoenai, Omiri, Yeremoti, Abiya, Anatoti ndi Alemeti. Onsewa anali ana a Bekeri.
9 And they were nombred by their genealogies according to their generations, and the chiefe of the houses of their fathers, valiant men of warre, twenty thousand and two hundreth.
Pa mndandanda wa mʼbado wawo panali atsogoleri a mabanja ndi anthu 20,200 odziwa kumenya nkhondo.
10 And the sonne of Iediael was Bilhan, and the sonnes of Bilhan, Ieush, and Beniamin, and Ehud, and Chenaanah, and Zethan, and Tharshish, and Ahishahar.
Mwana wa Yediaeli anali Bilihani. Ana a Bilihani anali awa: Yeusi, Benjamini, Ehudi, Kenaana, Zetani, Tarisisi ndi Ahisahara.
11 All these were the sonnes of Iediael, chiefe of the fathers, valiant men of warre, seuenteene thousand and two hundreth, marching in battel aray to the warre.
Ana onsewa a Yediaeli anali atsogoleri a mabanja. Analipo anthu 17,200 amene anali okonzeka kupita ku nkhondo.
12 And Shuppim, and Huppim were ye sonnes of Ir, but Hushim was the sonne of another.
Asupi ndi Ahupi anali zidzukulu za Iri, ndipo Ahusimu anali zidzukulu za Aheri.
13 The sonnes of Naphtali, Iahziel, and Guni, and Iezer, and Shallum of the sonnes of Bilhah.
Ana a Nafutali anali awa: Yahazieli, Guni, Yezeri ndi Salumu, zidzukulu za Biliha.
14 The sonne of Manasseh was Ashriel whom she bare vnto him, but his concubine of Aram bare Machir the father of Gilead.
Ana a Manase anali awa: Asirieli ndi mwana amene anabereka kwa mzikazi wake wa ku Aramu. Mzikazi yemweyo anaberekanso Makiri abambo ake a Giliyadi.
15 And Machir tooke to wife the sister of Huppim and Shuppim, and the name of their sister was Maachah. And the name of the second sonne was Zelophehad, and Zelophehad had daughters.
Makiri anatenga mkazi wa banja la Ahupi ndi Asupi. Mlongo wake anali Maaka. Mwana wake wina anali Zelofehadi, amene anabereka ana aakazi okhaokha.
16 And Maachah the wife of Machir bare a sonne, and called his name Peresh, and the name of his brother was Sheresh: and his sonnes were Vlam and Rakem.
Maaka mkazi wa Makiri anabereka mwana wamwamuna ndipo anamutcha Perezi. Mʼbale wake anamutcha Seresi, ndipo ana ake anali Ulamu ndi Rakemu.
17 And the sonne of Vlam was Bedan. These were the sonnes of Gilead the sonne of Machir, the sonne of Manasseh.
Mwana wa Ulamu anali Bedani. Awa anali ana a Giliyadi mwana wa Makiri, mwana wa Manase.
18 And his sister Molecheth bare Ishod, and Abiezer, and Mahalah.
Mlongo wake Hamoleketi anabereka Isihodi, Abiezeri ndi Mahila.
19 And the sonnes of Shemida were Ahian, and Shechem, and Likhi, and Aniam.
Ana a Semida anali: Ahiyani, Sekemu, Likihi ndi Aniyamu.
20 The sonnes also of Ephraim were Shuthelah, and Bered his sonne, and Tahath his sonne, and his sonne Eladah, and Tahath his sonne,
Ana a Efereimu anali awa: Sutela, Beredi, Tahati, Eliada, Tahati,
21 And Zabad his sonne, and Shuthelah his sonne, and Ezer, and Elead: and the men of Gath that were borne in the land, slewe them, because they came downe to take away their cattel.
Zabadi, Sutela. Ezeri ndi Eladi anaphedwa ndi anthu a ku Gati, pamene anabwera kudzalanda zoweta zawo.
22 Therefore Ephraim their father mourned many dayes, and his brethren came to comfort him.
Efereimu, abambo awo, anawalira masiku ambiri, ndipo abale ake anabwera kudzamutonthoza.
23 And when he went in to his wife, she conceiued, and bare him a sonne, and he called his name Beriah, because affliction was in his house.
Kenaka anagona ndi mkazi wake, ndipo anakhala woyembekezera nabala mwana wamwamuna. Anamutcha dzina lake Beriya, chifukwa tsoka linagwera banja lake.
24 And his daughter was Sherah, which built Beth-horon the nether, and the vpper, and Vzzen Sheerah.
Mwana wake wamkazi anali Seera, amene anamanga mzinda wa Beti-Horoni Wakumunsi, Wakumtunda kudzanso Uzeni-Seera.
25 And Rephah was his sonne, and Resheph, and Telah his sonne, and Tahan his sonne,
Mwana wina wa Efereimu anali Refa amene zidzukulu zake zinali Resefu, Tela, Tahani,
26 Laadan his sonne, Ammihud his sonne, Elishama his sonne,
Ladani, Amihudi, Elisama,
27 Non his sonne, Iehoshua his sonne.
Nuni ndi Yoswa.
28 And their possessions and their habitations were Beth-el, and the villages thereof, and Eastward Naaran, and Westwarde Gezer with the villages thereof, Shechem also and the villages thereof, vnto Azzah, and the villages thereof,
Malo amene ankakhala anali Beteli ndi midzi yozungulira, cha kummawa kunali Naarani, Gezeri ndi midzi yake ya kumadzulo ndi Sekemu ndi midzi yake mpaka ku Aya ndi midzi yake.
29 And by the places of the children of Manasseh, Beth-shean and her villages, Taanach and her villages, Megiddo and her villages, Dor and her villages. In those dwelt the children of Ioseph the sonne of Israel.
Mʼmbali mwa malire a Manase munali Beti-Seani, Taanaki, Megido ndi Dori, pamodzi ndi midzi yake. Zidzukulu za Yosefe mwana wa Israeli zimakhala mʼmizinda imeneyi.
30 The sonnes of Asher were Imnah, and Isuah, and Ishuai, and Beriah, and Serah their sister.
Ana a Aseri anali awa: Imuna, Isiva, Isivi ndi Beriya. Mlongo wawo anali Sera.
31 And the sonnes of Beriah, Heber, and Malchiel, which is the father of Birzauith.
Ana a Beriya anali awa: Heberi ndi Malikieli amene anabereka Birizaiti.
32 And Heber begate Iaphlet, and Shomer, and Hotham, and Shuah their sister.
Heberi anabereka Yafuleti, Someri, Hotamu ndi Suwa, mlongo wawo.
33 And the sonnes of Iaphlet were Pasach, and Bimhal, and Ashuath: these were the children of Iaphlet.
Ana a Yafuleti anali awa: Pasaki, Bimuhali ndi Asivati. Awa anali ana a Yafuleti.
34 And the sonnes of Shamer, Ahi, and Rohgah, Iehubbah, and Aram.
Ana a Someri anali awa: Ahi, Rohiga, Yehuba ndi Aramu.
35 And the sonnes of his brother Helem were Zophah, and Iimna, and Shelesh and Amal.
Ana a mʼbale wake Helemu anali awa: Zofa, Imuna, Selesi ndi Amali.
36 The sonnes of Zophah, Suah, and Harnepher, and Shual, and Beri, and Imrah,
Ana a Zofa anali awa: Suwa, Harineferi, Suwali, Beri, Imula,
37 Bezer and Hod, and Shamma, and Shilshah, and Ithran, and Beera.
Bezeri, Hodi, Sama, Silisa, Itirani ndi Bera.
38 And the sonnes of Iether, Iephunneh, and Pispa and Ara.
Ana a Yeteri anali awa: Yefune, Pisipa ndi Ara.
39 And the sonnes of Vlla, Harah, and Haniel, and Rizia.
Ana a Ula anali awa: Ara, Hanieli ndi Riziya.
40 All these were the children of Asher, the heads of their fathers houses, noble men, valiant men of warre and chiefe princes, and they were rekoned by their genealogies for warre and for battell to the nomber of sixe and twentie thousand men.
Onsewa anali zidzukulu za Aseri, atsogoleri a mabanja, anthu omveka, ankhondo olimba mtima, ndi akuluakulu pakati pa atsogoleri anzawo. Chiwerengero cha anthu odziwa kumenya nkhondo chomwe chinalembedwa chinali 26,000.

< 1 Chronicles 7 >