< 1 Chronicles 27 >

1 The children of Israel also after their nomber, euen the chiefe fathers and captaines of thousandes and of hundreths, and their officers that serued the King by diuers courses, which came and in went out, moneth by moneth throughout al the moneths of the yeere: in euery course were foure and twentie thousand.
Uwu ndi mndandanda wa Aisraeli, atsogoleri a mabanja, olamulira asilikali 1,000, olamulira asilikali 100 ndi akuluakulu awo, amene ankatumikira mfumu mʼzonse zokhudza magulu a ankhondo, amene amagwira ntchito mwezi ndi mwezi chaka chonse. Gulu lililonse linali ndi anthu 24,000.
2 Ouer the first course for the first moneth was Iashobeam the sonne of Zabdiel: and in his course were foure and twentie thousand.
Amene amalamulira gulu loyamba pa mwezi woyamba anali Yasobeamu mwana wa Zabidieli. Pa gulu lake panali asilikali 24,000.
3 Of the sonnes of Perez was the chiefe ouer all the princes of the armies for the first moneth.
Iyeyu anali chidzukulu cha Perezi ndipo anali mkulu wa atsogoleri onse a ankhondo mwezi woyamba.
4 And ouer the course of the second moneth was Dodai, an Ahohite, and this was his course, and Mikloth was a captaine, and in his course were foure and twentie thousand.
Amene amalamulira gulu lachiwiri pa mwezi wachiwiri anali Dodai Mwahohi; Mikiloti ndiye anali mtsogoleri wa gulu lake. Pa gulu lake panali asilikali 24,000.
5 The captaine of the thirde hoste for the third moneth was Benaiah the sonne of Iehoiada the chiefe Priest: and in his course were foure and twentie thousand.
Wolamulira ankhondo wachitatu, pa mwezi wachitatu anali Benaya, mwana wa wansembe Yehoyada. Iye anali mtsogoleri ndipo pa gulu lake panali ankhondo 24,000.
6 This Benaiah was mightie among thirtie and aboue the thirtie, and in his course was Amizabad his sonne.
Uyu ndi Benaya uja amene anali wamphamvu pa gulu la anthu makumi atatu ndipo ndiye amatsogolera anthu makumi atatu aja. Mwana wake Amizabadi ndiye amatsogolera gulu lake.
7 The fourth for the fourth moneth was Asahel the brother of Ioab, and Zebadiah his sonne after him: and in his course were foure and twentie thousand.
Wachinayi pa mwezi wachinayi anali Asaheli mʼbale wake wa Yowabu; ndipo mwana wake Zebadiya ndiye analowa mʼmalo mwake. Pa gulu lake panali asilikali 24,000.
8 The fift for ye fift moneth was prince Shamhuth the Izrahite: and in his course foure and twentie thousand.
Wachisanu pa mwezi wachisanu anali Samihuti, mdzukulu wa Izira. Pa gulu lake panali asilikali 24,000.
9 The sixt for the sixt moneth was Ira the sonne of Ikkesh the Tekoite: and in his course foure and twentie thousand.
Wa 6 pa mwezi wa 6 anali Ira mwana wa Ikesi wa ku Tekowa. Pa gulu lake panali asilikali 24,000.
10 The seuenth for the seuenth moneth was Helez the Pelonite, of the sonnes of Ephraim: and in his course foure and twentie thousand.
Wa 7 pa mwezi wa 7 anali Helezi Mpeloni wa fuko la Efereimu. Pa gulu lake panali asilikali 24,000.
11 The eight for the eight moneth was Sibbecai the Hushathite of the Zarhites: and in his course foure and twentie thousand.
Wa 8 pa mwezi wa 8 anali Sibekai Mhusati, wa mbumba ya Zera. Pa gulu lake panali asilikali 24,000
12 The ninth for the ninth moneth was Abiezer the Anethothite of the sonnes of Iemini: and in his course foure and twentie thousand.
Wa 9 pa mwezi wa 9 anali Abiezeri wa banja la Anatoti, wa fuko la Benjamini. Pa gulu lake panali asilikali 24,000.
13 The tenth for the tenth moneth was Maharai, the Netophathite of the Zarhites: and in his course foure and twentie thousand.
Wa khumi pa mwezi wa khumi anali Mahazayi wa ku Netofa, wa mbumba ya Zera. Pa gulu lake panali asilikali 24,000.
14 The eleueth for the eleuenth moneth was Benaiah the Pirathonite of the sonnes of Ephraim: and in his course foure and twentie thousand.
Mtsogoleri wa 11, pa mwezi wa 11 anali Benaya wa ku Piratoni, wa fuko la Efereimu. Pa gulu lake panali asilikali 24,000.
15 The twelft for the twelft moneth was Heldai the Netophathite, of Othniel: and in his course foure and twentie thousand.
Mtsogoleri wa 12, pa mwezi wa 12 anali Helidai Mnetofa, wa banja la Otanieli. Pa gulu lake panali asilikali 24,000.
16 Moreouer the rulers ouer the tribes of Israel were these: ouer the Reubenites was ruler, Eliezer the sonne of Zichri: ouer the Shimeonites, Shephatiah the sonne of Maachah:
Akuluakulu amene amatsogolera mafuko a Israeli ndi awa: Mtsogoleri wa fuko la Rubeni: Eliezara mwana wa Zikiri; mtsogoleri wa fuko la Simeoni: Sefatiya mwana wa Maaka;
17 Ouer the Leuites, Hashabiah the sonne of Remuel: ouer them of Aharon, and Zadok:
mtsogoleri wa fuko la Levi: Hasabiya mwana wa Kemueli, mtsogoleri wa banja la Aaroni: Zadoki;
18 Ouer Iudah, Elihu of the brethren of Dauid: ouer Issachar, Omri the sonne of Michael:
mtsogoleri wa fuko la Yuda: Elihu, mʼbale wake wa Davide; mtsogoleri wa fuko la Isakara: Omuri mwana wa Mikayeli;
19 Ouer Zebulun, Ishmaiah the sonne of Obadiah: ouer Naphtali, Ierimoth the sonne of Azriel:
mtsogoleri wa fuko la Zebuloni: Isimaiya mwana wa Obadiya; mtsogoleri wa fuko la Nafutali: Yerimoti mwana wa Azirieli;
20 Ouer the sonnes of Ephraim, Hoshea the sonne of Azazziah: ouer the halfe tribe of Manasseh, Ioel the sonne of Pedaiah:
mtsogoleri wa fuko la Efereimu: Hoseya mwana wa Azaziya; mtsogoleri wa fuko la theka la Manase: Yoweli mwana wa Pedaya;
21 Ouer the other halfe of Manasseh in Gilead, Iddo the sonne of Zechariah: ouer Beniamin, Iaasiel the sonne of Abner:
mtsogoleri wa fuko la theka la Manase limene linali ku Giliyadi: Ido mwana wa Zekariya; mtsogoleri wa fuko la Benjamini: Yaasieli mwana wa Abineri;
22 Ouer Dan, Azariel the sonne of Ieroham. these are the princes of the tribes of Israel.
mtsogoleri wa fuko la Dani: Azareli mwana wa Yerohamu. Awa anali akuluakulu a mafuko a Israeli.
23 But Dauid tooke not the nober of them from twentie yeere olde and vnder, because the Lord had sayde that he would increase Israel like vnto the starres of the heauens.
Davide sanawerenge amuna amene anali ndi zaka makumi awiri kapena kucheperapo, chifukwa Yehova analonjeza kuti adzachulukitsa Aisraeli ngati nyenyezi zamumlengalenga.
24 And Ioab the sonne of Zeruiah beganne to nomber: but hee finished it not, because there came wrath for it against Israel, neither was the nomber put into the Chronicles of King Dauid.
Yowabu mwana wa Zeruya anayamba kuwerenga amuna koma sanamalize. Mkwiyo unagwera Aisraeli chifukwa cha zimenezi ndipo chiwerengerochi sanachilowetse mʼbuku la mbiri ya mfumu Davide.
25 And ouer the Kings treasures was Azmaueth the sonne of Adiel: and ouer the treasures in the fieldes, in the cities and in the villages and in the towers was Iehonathan the sonne of Vzziah:
Azimaveti mwana wa Adieli ankayangʼanira nyumba zosungiramo katundu wa mfumu. Yonatani mwana wa Uziya ankayangʼanira nyumba zosungiramo katundu wa maboma ozungulira, mizinda, midzi ndi malo olondera.
26 And ouer the workemen in the fielde that tilled the ground, was Ezri the sonne of Chelub:
Eziri mwana wa Kelubi ankayangʼanira anthu ogwira ntchito yolima ku munda.
27 And ouer them that dressed the vines, was Shimei the Ramathite: and ouer that which apperteined to the vines, and ouer the store of the wine was Sabdi the Shiphmite:
Simei wa ku Rama ankayangʼanira minda ya mpesa. Zabidi wa ku Sifamu ankayangʼanira mphesa ndi mosungiramo mwake.
28 And ouer the oliue trees and mulberie trees that were in the valleys, was Baal Hanan the Gederite: and ouer the store of the oyle was Ioash:
Baala-Hanani wa ku Gederi ankayangʼanira mitengo ya olivi ndi ya mikuyu ya ku Sefela. Yowasi ankayangʼanira mafuta a Olivi.
29 And ouer the oxen that fed in Sharon, was Shetrai the Sharonite: and ouer the oxen in the valleyes was Shaphat the sonne of Adlai:
Sitirayi wa ku Saroni ankayangʼanira ziweto zimene amaweta ku Saroni. Safati mwana wa Adilayi ankayangʼanira ngʼombe zakuzigwa.
30 And ouer the camels was Obil the Ishmaelite: and ouer the asses was Iehdeiah the Meronothite:
Obili Mwismaeli ankayangʼanira ngamira. Yehideya Mmerenoti ankayangʼanira abulu.
31 And ouer the sheepe was Iaziz the Hagerite: all these were the rulers of the substance that was King Dauids.
Yazizi Mhagiri akayangʼanira nkhosa ndi mbuzi. Onsewa anali akuluakulu oyangʼanira chuma cha mfumu Davide.
32 And Iehonathan Dauids vncle a man of counsell and vnderstanding (for he was a scribe) and Iehiel the sonne of Hachmoni were with the Kings sonnes.
Yonatani, malume wake wa Davide, anali phungu wake ndipo anali munthu wanzeru komanso analinso mlembi. Yehieli mwana wa Hakimoni ankasamalira ana a mfumu.
33 And Ahitophel was the Kings counseller, and Hushai the Archite the Kings friend.
Ahitofele anali phungu wa mfumu. Husai Mwariki anali bwenzi la mfumu.
34 And after Ahitophel was Iehoiada the sonne of Benaiah and Abiathar: and captaine of the Kings armie was Ioab.
Ahitofele atamwalira mʼmalo mwake munalowa Yehoyada mwana wa Benaya ndi Abiatara. Yowabu anali mtsogoleri wa gulu lankhondo la mfumu.

< 1 Chronicles 27 >