< 1 Chronicles 14 >

1 Then sent Hiram the King of Tyrus messengers to Dauid, and cedar trees, with masons and carpenters to builde him an house.
Hiramu mfumu ya ku Turo inatumiza amithenga kwa Davide pamodzi ndi mitengo ya mkungudza ndiponso amisiri a miyala ndi amisiri a matabwa kuti adzamumangire nyumba yaufumu.
2 Therefore Dauid knewe that the Lord had confirmed him King ouer Israel, and that his kingdome was lift vp on hie, because of his people Israel.
Choncho Davide anazindikira kuti Yehova wamukhazikitsa kukhala mfumu ya Israeli ndipo wakuza kwambiri ufumu wake chifukwa cha anthu ake, Aisraeli.
3 Also Dauid tooke moe wiues at Ierusalem, and Dauid begate moe sonnes and daughters.
Davide anakwatira akazi ena ambiri ku Yerusalemu ndipo anabereka ana aamuna ndi aakazi ambiri.
4 And these are the names of the children which he had at Ierusalem, Shammua, and Shobab, Nathan, and Salomon,
Mayina a ana amene anaberekera ku Yerusalemu anali awa: Samua, Sobabu, Natani, Solomoni,
5 And Ibhar, and Elishua, and Elpalet,
Ibihari, Elisua, Elipeleti,
6 And Nogah, and Nepheg, and Iaphia,
Noga, Nefegi, Yafiya,
7 And Elishama, and Beeliada, and Eliphalet.
Elisama, Beeliada ndi Elifeleti.
8 But when the Philistims heard that Dauid was anointed King ouer Israel, all the Philistims came vp to seeke Dauid. And when Dauid heard, he went out against them.
Afilisti atamva kuti Davide wadzozedwa kukhala mfumu ya dziko lonse la Israeli, iwo anapita mwamphamvu kukamusakasaka. Koma Davide atamva zimenezi anapita kukakumana nawo.
9 And the Philistims came, and spred them selues in the valley of Rephaim.
Ndipo Afilisti anabwera ndi kulanda zinthu mʼChigwa cha Refaimu.
10 Then Dauid asked counsel at God, saying, Shall I goe vp against the Philistims, and wilt thou deliuer them into mine hande? And the Lord saide vnto him, Goe vp: for I will deliuer them into thine hande.
Davide anafunsa Mulungu kuti, “Kodi ndipite kukathira nkhondo Afilisti? Kodi mukawapereka mʼmanja mwanga?” Yehova anamuyankha kuti, “Pita, Ine ndidzawapereka mʼmanja mwako.”
11 So they came vp to Baal-perazim, and Dauid smote them there: and Dauid said, God hath deuided mine enemies with mine hande, as waters are deuided: therefore they called the name of that place, Baal-perazim.
Choncho Davide ndi anthu ake anapita ku Baala-Perazimu ndi kugonjetsa Afilistiwo. Iye anati, “Monga amasefukira madzi, Mulungu waphwanya adani anga ine ndikuona.” Motero anawatcha malowa Baala Perazimu.
12 And there they had left their gods: and Dauid said, Let them euen be burnt with fire.
Afilisti anasiya milungu yawo kumeneko ndipo Davide analamulira kuti itenthedwe ndi moto.
13 Againe the Philistims came and spread them selues in the valley.
Nthawi inanso Afilisti anadzalanda katundu mu Chigwamo.
14 And when Dauid asked againe counsell at God, God said to him, Thou shalt not goe vp after them, but turne away from them, that thou mayest come vpon them ouer against the mulberie trees.
Choncho Davide anafunsa Mulungu ndipo Mulunguyo anayankha kuti, “Usapite molunjika, koma uzungulire kumbuyo kwawo. Ukawathire nkhondo patsogolo pa mitengo ya mkandankhuku.
15 And when thou hearest the noyse of one going in the toppes of the mulberie trees, then goe out to battel: for God is gone foorth before thee, to smite the hoste of the Philistims.
Mukakangomva phokoso pa msonga za mitengo ya mkandankhuku, mukapite kukamenyana nawo, chifukwa izi zikasonyeza kuti Mulungu ali patsogolo panu kukantha ankhondo a Afilisti.”
16 So Dauid did as God had commanded him: and they smote the hoste of the Philistims from Gibeon euen to Gezer.
Kotero Davide anachita zimene Mulungu anamulamulira ndipo anakantha ankhondo a Afilisti njira yonse kuchokera ku Gibiyoni mpaka ku Gezeri.
17 And the fame of Dauid went out into all landes, and the Lord brought the feare of him vpon all nations.
Choncho mbiri ya Davide inafalikira dziko lonse, ndipo Yehova anachititsa kuti mayiko ena azimuopa.

< 1 Chronicles 14 >