< 1 Chronicles 13 >

1 And Dauid counselled with the captaines of thousandes and of hundreths, and with all the gouernours.
Davide anakambirana ndi akuluakulu ake, atsogoleri a anthu 1,000 ndi atsogoleri a anthu 100.
2 And Dauid said to all the Congregation of Israel, If it seeme good to you, and that it proceedeth of the Lord our God, we will sende to and from vnto our brethren, that are left in all the lande of Israel (for with them are the Priests and the Leuites in the cities and their suburbes) that they may assemble them selues vnto vs.
Ndipo anati kwa gulu lonse la Israeli, “Ngati kukukomerani komanso ngati chili chifuniro cha Yehova Mulungu wathu, tiyeni titumize uthenga kulikonse kumene kuli abale athu ena onse ku dziko lonse la Israeli ndiponso kwa ansembe ndi Alevi amene ali nawo mʼmidzi yawo ndi madera odyetsera ziweto, kuti abwere adzakhale nafe.
3 And we will bring againe the Arke of our God to vs: for we sought not vnto it in the dayes of Saul.
Tiyeni tibweretsenso Bokosi la Mulungu wathu kuno kwathu, pakuti nthawi ya Sauli sitinafunse za bokosili.”
4 And all the Congregation answered, Let vs doe so: for the thing seemed good in the eyes of all the people.
Gulu lonse linavomereza izi, pakuti anthu onse anaona kuti kunali kofunika kutero.
5 So Dauid gathered all Israel together from Shihor in Egypt, euen vnto the entring of Hamath, to bring the Arke of God from Kiriath-iearim.
Kotero Davide anasonkhanitsa Aisraeli onse, kuchokera ku mtsinje wa Sihori ku Igupto mpaka ku Lebo Hamati, kuti abweretse Bokosi la Mulungu kuchokera ku Kiriati-Yearimu.
6 And Dauid went vp and all Israel to Baalath, in Kiriath-iearim, that was in Iudah, to bring vp from thence the Arke of God the Lord that dwelleth betweene the Cherubims, where his Name is called on.
Davide pamodzi ndi Aisraeli onse anapita ku Baalahi (Kiriati-Yearimu) ku Yuda kukatenga Bokosi la Yehova Mulungu, amene amakhala pakati pa akerubi. Limeneli ndiye Bokosi la Chipangano lomwe limadziwika ndi Dzina lake.
7 And they caryed the Arke of God in a newe cart out of the house of Abinadab: and Vzza and Ahio guided the cart.
Iwo anachotsa Bokosi la Mulungu ku nyumba ya Abinadabu pa ngolo yatsopano. Uza ndi Ahiyo ndiwo ankayendetsa ngoloyo.
8 And Dauid and all Israel played before God with all their might, both with songes and with harpes, and with violes, and with timbrels and with cymbales and with trumpets.
Davide pamodzi ndi Aisraeli onse ankakondwerera ndi mphamvu zawo zonse pamaso pa Mulungu, poyimba nyimbo pogwiritsa ntchito azeze, apangwe, matambolini, maseche ndi malipenga.
9 And when they came vnto the thresshing floore of Chidon, Vzza put forth his hand to holde the Arke, for the oxen did shake it.
Atafika pa malo opunthira tirigu ku Kidoni, Uza anatambalitsa dzanja lake kuti agwire bokosilo, chifukwa ngʼombe zinkafuna kugwa.
10 But the wrath of the Lord was kindled against Vzza, and he smote him, because he layed his hande vpon the Arke: so he dyed there before God.
Yehova anapsera mtima Uza ndipo anamukantha chifukwa chogwira bokosilo. Choncho iyeyo anafera pomwepo pamaso pa Mulungu.
11 And Dauid was angrie, because the Lord had made a breach in Vzza, and he called the name of that place Perez-vzza vnto this day.
Ndipo Davide anakhumudwa chifukwa Yehova anakantha Uza ndipo mpaka lero malowo amatchedwa Perezi Uza.
12 And Dauid feared God that day, saying, Howe shall I bring in to me the Arke of God?
Tsiku limenelo Davide anachita mantha ndi Mulungu ndipo anafunsa kuti, “Kodi Bokosi la Mulungu lingafike bwanji kwathu?”
13 Therefore Dauid brought not the Arke to him into the citie of Dauid, but caused it to turne into the house of Obed Edom the Gittite.
Iye sanapitenso nalo Bokosi la Mulungu ku Mzinda wa Davide. Mʼmalo mwake anapita nalo ku nyumba ya Obedi-Edomu Mgiti.
14 So the Arke of God remained in the house of Obed Edom, euen in his house three moneths: and the Lord blessed the house of Obed Edom, and all that he had.
Ndipo Bokosi la Mulungu linakhala mʼbanja la Obedi-Edomu mʼnyumba mwake kwa miyezi itatu ndipo Yehova anadalitsa nyumba yake ndi chilichonse chimene anali nacho.

< 1 Chronicles 13 >