< Zechariah 6 >

1 Then I looked again and I saw four chariots coming out from between two mountains that looked like bronze.
Ndinayangʼananso ndipo taonani ndinaona magaleta anayi akutuluka pakati pa mapiri awiri, mapiri amkuwa.
2 The first chariot was pulled by red horses, the second by black horses,
Galeta loyamba limakokedwa ndi akavalo ofiira, lachiwiri ndi akavalo akuda,
3 the third by white horses, and the fourth by dappled grey horses—all of them strong horses.
lachitatu ndi akavalo oyera, ndipo lachinayi ndi akavalo otuwa a mawanga ofiirira, onsewa anali akavalo amphamvu kwambiri.
4 “My lord, what are these?” I asked the angel I was talking to.
Ndinafunsa mngelo amene amayankhula nane uja kuti, “Kodi mbuye wanga chimenechi nʼchiyani?”
5 “They are going out to the four winds of heaven, after presenting themselves to the Lord of all the earth,” the angel explained.
Mngeloyo anandiyankha kuti, “Imeneyi ndi mizimu inayi yakumwamba, imene ikuchokera pamaso pa Ambuye wa dziko lonse.
6 The chariot with the black horses went north, the one with the white horses went west, and the one with the dappled grey horses went south.
Galeta la akavalo akuda likupita ku dziko la kumpoto, galeta la akavalo oyera likutsatira, ndipo galeta la akavalo amawanga ofiirira likupita ku dziko la kummwera.”
7 When the strong horses came out they were eager to set off to patrol the earth. And he said, “Go and patrol the earth!” So they left and patrolled the earth.
Pamene akavalo amphamvuwa ankapita, anali ndi changu chofuna kuyendera dziko lapansi. Ndipo iye anati, “Pitani, kayendereni dziko lapansi!”
8 Then the angel called to me, saying, “Look! Those who went north have achieved what the Lord wanted in the land of the north.”
Pamenepo anandiyitana, “Taona, akavalo amene apita ku dziko la kumpoto apumulitsa Mzimu wanga kumeneko.”
9 Then the Lord gave me another message:
Yehova anayankhula nane kuti,
10 Take the gifts brought by Heldai, Tobijah, and Jedaiah, the exiles returning from Babylon, and go immediately to the house of Josiah son of Zephaniah.
“Landira mphatso kuchokera kwa anthu amene abwera ku ukapolo, Helidai, Tobiya ndi Yedaya, amene achokera ku Babuloni. Tsiku lomwelo pita ku nyumba ya Yosiya mwana wa Zefaniya.
11 Use the silver and the gold they brought to make a crown, and place it on the head of Josiah, son of Jehozadak, the high priest.
Tenga siliva ndi golide upange chipewa chaufumu, ndipo uchiyike pamutu pa mkulu wa ansembe, Yoswa mwana wa Yehozadaki.
12 Tell him this is what the Lord Almighty says: Look! The man who is called the Branch will grow from where he is and will build the Lord's Temple.
Muwuze kuti zimene akunena Yehova Wamphamvuzonse ndi izi: ‘Taonani, munthu wotchedwa Nthambi ndi ameneyu, ndipo adzaphuka pomwe alipo ndi kumanga Nyumba ya Yehova.
13 He is the one who will build the Lord's Temple, and he will be the one given the honor to rule from both the royal throne and the priestly throne and there will be peace and understanding between the two roles.
Ndiye amene adzamange Nyumba ya Yehova, adzalandira ulemerero waufumu ndipo adzalamulira pa mpando wake waufumu. Adzakhalanso wansembe pa mpando wake waufumu. Ndipo padzakhala mtendere.’
14 The crown will be kept in the Temple of the Lord as a memorial to Heldai, Tobijah, Jedaiah, and Joshua the son of Zephaniah.
Chipewa cha ufumucho adzachipereka kwa Helemu, Tobiya, Yedaya, ndi kwa Heni mwana wa Zefaniya, kuti chikhale chikumbutso mʼNyumba ya Yehova.
15 People who live in distant lands will come and build the Temple of the Lord, and you will know that the Lord Almighty sent me to you. This will happen if you listen attentively to what the Lord tells you.
Anthu okhala kutali adzabwera kudzathandiza kumanga Nyumba ya Yehova, ndipo iwe udzadziwa kuti Yehova Wamphamvuzonse wandituma kwa iwe. Zimenezi zidzachitika ngati mudzamvera mwachangu Yehova Mulungu wanu.”

< Zechariah 6 >