< Zechariah 13 >

1 On that day a spring will be opened and continually flow for the house of David and for the people of Jerusalem to wash away their sin and impurity.
“Pa tsiku limenelo nyumba ya Davide adzayitsekulira kasupe wa madzi pamodzi ndi okhala mu Yerusalemu, kuti awachotsere tchimo lawo ndi chodetsa chawo.
2 On that day, declares the Lord Almighty, I will wipe out idol worship from the land—the idols will not be remembered any longer. I will remove the false prophets and the spirit of impurity from the land.
“Pa tsiku limenelo, ndidzafafaniziratu mayina a mafano mʼdziko, ndipo sadzawakumbukiranso,” akutero Yehova Wamphamvuzonse. “Ndidzachotsa mʼdziko aneneri pamodzi ndi mzimu wonyansa.
3 If anyone continues to prophesy, his father and mother to whom he was born will tell him, “You shall not live, because you have told lies in the Lord's name.” Then his parents shall kill him because he has prophesied.
Ndipo ngati wina aliyense adzafuna kunenera, abambo ndi amayi ake amene anamubereka, adzamuwuza kuti, ‘Uyenera kufa, chifukwa wayankhula bodza mʼdzina la Yehova.’ Pamene anenera, makolo ake omwe adzamubaya.
4 On that day such prophets will be too humiliated to prophesy their supposed visions. In order to deceive they will not put on their prophet's clothes made of coarse hair.
“Pa tsiku limenelo mneneri aliyense adzachita manyazi chifukwa cha masomphenya ake. Sadzavala chovala chake chaubweya ndi cholinga chonamiza anthu.
5 They will say, “I'm not a prophet, I'm a farmer. I've worked on the land since I was a child.”
Iye adzati, ‘Sindine mneneri. Ndine mlimi; ndakhala ndi kulima munda kuyambira ubwana wanga.’
6 If somebody asks him, “What are those wounds on your back?” he will answer, “I was wounded in my friend's house.”
Ngati wina adzamufunsa, ‘Zilonda zili mʼthupi lakoli ndi chiyani?’ Iye adzayankha kuti, ‘Zilondazi ndinazilandira mʼnyumba ya abwenzi anga.’
7 Wake up, my sword! Attack my shepherd, the man who stands beside me! declares the Lord. Strike the shepherd and the sheep will be scattered, and I will raise my hand against the lambs.
“Dzambatuka iwe lupanga, ukanthe mʼbusa wanga, ukanthe munthu amene ali pafupi ndi Ine!” akutero Yehova Wamphamvuzonse. Kantha mʼbusa ndipo nkhosa zidzabalalika, ndipo ndidzatambalitsa dzanja langa kuwononga zazingʼono.
8 Two thirds of the people of the land will be cut down, only one third will remain, says the Lord.
Mʼdziko monse, akutero Yehova Wamphamvuzonse, “zigawo ziwiri mwa zigawo zitatu za anthu zidzakanthidwa ndi kuwonongeka; koma chigawo chimodzi chidzatsala mʼdzikomo.
9 I will place this one third in the fire, and I will refine them as silver is refined, and test them as gold is tested. They will call on me for help, and I will answer them. I will say, “These are my people,” and they will say, “The Lord is my God.”
Chigawo chachitatuchi ndidzachiyika pa moto; ndidzawayeretsa monga momwe amayeretsera siliva ndi kuwayesa monga momwe amayesera golide. Adzayitana pa dzina langa ndipo Ine ndidzawayankha; Ine ndidzanena kuti, ‘Awa ndi anthu anga,’ ndipo iwo adzanena kuti, ‘Yehova ndiye Mulungu wathu.’”

< Zechariah 13 >