< Psalms 98 >
1 A psalm. Sing the Lord a new song, for he has done wonderful things: by his powerful right hand and his strong arm he has won the victory.
Salimo. Imbirani Yehova nyimbo yatsopano, pakuti Iyeyo wachita zinthu zodabwitsa; dzanja lake lamanja ndi mkono wake woyera zamuchitira chipulumutso.
2 The Lord has revealed his salvation to the nations, and shown them his goodness.
Yehova waonetsa chipulumutso chake ndipo waulula chilungamo chake kwa anthu a mitundu ina.
3 He has not forgotten to show his trustworthy love and faithfulness to the descendants of Israel. Our God has made his salvation clear to the ends of the earth.
Iye wakumbukira chikondi chake ndi kukhulupirika kwake pa Aisraeli; malekezero onse a dziko lapansi aona chipulumutso cha Mulungu wathu.
4 Everyone on earth, shout in triumph to the Lord; break out in joyful songs of praise!
Fuwulani mwachimwemwe kwa Yehova, dziko lonse lapansi, muyimbireni nyimbo mofuwula ndi mokondwera.
5 Sing praises to the Lord with the harp, with the harp and melodious voices;
Imbirani Yehova nyimbo ndi zeze, ndi zeze ndi mawu a kuyimba,
6 with trumpets and the sound of the ram's horn sing in happiness before the Lord, the King.
ndi malipenga ndi kuliza kwa nyanga ya nkhosa yayimuna fuwulani mwachimwemwe pamaso pa Yehova Mfumu.
7 Let the sea and everything in it shout with praise, together with the earth and everything living in it.
Nyanja ikokome pamodzi ndi zonse zili mʼmenemo, dziko lonse ndi onse amene amakhala mʼmenemo.
8 Let the rivers celebrate, let the hills join in the celebration
Mitsinje iwombe mʼmanja mwawo, mapiri ayimbe pamodzi mwachimwemwe;
9 before the Lord, for he is coming to judge the earth. He will judge the world justly, and the nations fairly.
izo ziyimbe pamaso pa Yehova, pakuti Iye akubwera kudzaweruza dziko lapansi. Adzaweruza dziko lonse mwachilungamo, ndi mitundu ya anthu mosakondera.