< Psalms 92 >

1 A psalm. A song for the Sabbath day. How good it is to thank the Lord, to sing praises to you, Most High,
Salimo. Nyimbo ya pa tsiku la Sabata. Nʼkwabwino kutamanda Yehova ndi kuyimbira nyimbo dzina lanu, Inu Wammwambamwamba,
2 to tell of your trustworthy love in the morning, and your faithfulness in the night,
Kulengeza chikondi chanu mmawa, ndi kukhulupirika kwanu nthawi ya usiku,
3 to the music of a ten-stringed harp and the melody of a lyre.
kuyimbira nyimbo choyimbira cha zingwe khumi ndi mayimbidwe abwino a zeze.
4 You've made me so happy, Lord, because of all you've done for me! I sing for joy at what you've done!
Pakuti Inu mumandisangalatsa ndi ntchito zanu, Inu Yehova; Ine ndikuyimba mwachimwemwe pa ntchito ya manja anu.
5 Lord, what you do is amazing; your thoughts are very profound!
Ndi yayikuludi ntchito yanu Yehova, maganizo anu ndi ozamadi!
6 Only senseless people and fools don't know and understand this:
Munthu wopanda nzeru sadziwa, zitsiru sizizindikira,
7 even though the wicked grow up quickly like grass, and even though people who do evil flourish, they will be destroyed forever!
kuti ngakhale anthu oyipa aphuka ngati udzu ndipo anthu onse ochita zoyipa apindula, adzawonongedwa kwamuyaya.
8 But you, Lord, rule on high forever.
Koma Inu Yehova, ndinu wokwezedwa kwamuyaya.
9 Your enemies, Lord, your enemies will die; everyone who does evil will be destroyed!
Zoonadi adani anu Yehova, zoonadi adani anu adzawonongeka; onse ochita zoyipa adzabalalitsidwa.
10 But you have made me as powerful as a wild bull; you have anointed me with the best olive oil.
Inu mwakweza nyanga yanga ngati nyanga ya njati; mafuta abwino akhuthulidwa pamutu wanga.
11 My eyes look with pleasure to see my enemies defeated; my ears have heard the downfall of those who tried to attack me.
Maso anga aona kugonjetsedwa kwa olimbana nane, makutu anga amva za kugwa kwa amaliwongo anga oyipa.
12 Those who live right flourish like a palm tree; they grow tall like a cedar tree in Lebanon.
Anthu olungama adzaphuka ngati mtengo wa mgwalangwa, adzakula ngati mkungudza wa ku Lebanoni;
13 They are planted in the house of the Lord; they thrive in the courts of our God.
odzalidwa mʼnyumba ya Yehova, adzakula bwino mʼmabwalo a Mulungu wathu.
14 Even when they are old they will still produce fruit, staying fresh and green.
Iwo adzaberekabe zipatso mu ukalamba wawo, adzakhala anthete ndi obiriwira,
15 They will declare, “The Lord does what is right! He is my rock! There is no wrong in him!”
kulengeza kuti, “Yehova ndi wolungama; Iye ndiye Thanthwe langa, ndipo mwa Iye mulibe choyipa.”

< Psalms 92 >