< Psalms 81 >

1 For the music director. On the gittith. A psalm of Asaph. Sing aloud to God our strength; shout for joy to the God of Jacob.
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Potsata mayimbidwe a gititi. Salimo la Asafu. Imbani mwachimwemwe kwa Mulungu mphamvu yathu; Fuwulani mokweza kwa Mulungu wa Yakobo!
2 Start the song! Play the tambourine, sweet-sounding lyre, and harp.
Yambani nyimbo, imbani tambolini imbani pangwe wolira bwino ndi zeze.
3 Blow the trumpet at the new moon, and at full moon, to begin our festivals,
Imbani lipenga la nyanga ya nkhosa yayimuna pa mwezi watsopano, ndi pamene mwezi waoneka wonse, pa tsiku la phwando;
4 for this is a rule for Israel, a regulation of the God of Jacob.
ili ndi lamulo kwa Israeli, langizo la Mulungu wa Yakobo.
5 God made this statute for Joseph when he opposed the land of Egypt. I heard a voice I didn't know, saying:
Iye anapereka lamulolo kwa zidzukulu za Yosefe pamene anatuluka kulimbana ndi Igupto, kumene tinamva chiyankhulo chimene sitinachidziwe.
6 “I took the load from your shoulders; I freed your hands from carrying heavy baskets.
Iye akunena kuti, “Ine ndinachotsa zolemetsa pa mapewa awo; Manja awo anamasulidwa mʼdengu.
7 In your suffering you cried out to me, and I saved you. I answered you from the thundercloud. I tested you at the waters of Meribah. (Selah)
Pa mavuto anu munayitana ndipo ndinakulanditsani, ndinakuyankhani kuchokera mʼmitambo ya mabingu; ndinakuyesani pa madzi a ku Meriba. (Sela)
8 My people, listen to my warnings! Israel, please listen to me!
“Imvani anthu anga, ndipo ndidzakuchenjezani ngati mungathe kumvetsera, Inu Israeli!
9 There must not be a strange god among you; you must never bow down to foreign gods and worship them.
Musadzakhale ndi mulungu wachilendo pakati panu; musadzagwadire mulungu wina.
10 I am the Lord your God who brought you out of the land of Egypt. Open your mouth wide and I will fill it.
Ine ndine Yehova Mulungu wanu, amene ndinakutulutsani mʼdziko la Igupto. Yasamani kukamwa kwanu ndipo ndidzakudyetsani.
11 But my people didn't listen to me. Israel didn't want anything to do with me.
“Koma anthu anga sanandimvere; Israeli sanandigonjere.
12 So I sent them away to follow their stubborn thinking, living as they chose.
Kotero ndinawasiya ndi mitima yawo yosamverayo kuti atsate zimene ankafuna.
13 If only my people would listen to me; if only Israel would follow my ways!
“Anthu anga akanangondimvera, Israeli akanatsatira njira zanga,
14 It wouldn't take me long to conquer their enemies, to strike down their foes.
nʼkanafulumira motani kuti ndigonjetse adani awo ndi kutembenuza mkono wanga kulimbana ndi amaliwongo!
15 Those who hate the Lord would cringe before him, forever doomed.
Iwo amene amadana ndi Yehova akanakhwinyata pamaso pake, ndipo chilango chawo chinakakhala mpaka kalekale.
16 But I would feed you the best wheat and satisfy you with honey from the rock.”
Koma inu mukanadyetsedwa tirigu wabwino kwambiri; ndikanakukhutitsani ndi uchi wochokera pa thanthwe.”

< Psalms 81 >