< Psalms 6 >

1 For the music director. To be accompanied by stringed instruments, according to the sheminith. A psalm of David. Lord, please don't condemn me because you're angry with me; please don't punish me because you're angry with me!
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Pa zoyimbira za zingwe. Molingana ndi seminiti. Salimo la Davide. Inu Yehova, musandidzudzule mu mkwiyo wanu, kapena kundilanga mu ukali wanu.
2 Have mercy on me, Lord, for I am weak; heal me, Lord, for I am sick to the bone.
Ndichitireni chifundo Inu Yehova, pakuti ndalefuka; Inu Yehova chiritseni, pakuti mafupa anga ali pa ululu waukulu.
3 I'm shaking all over in fear. How long will it be, Lord, before you do something?
Moyo wanga uli pa mazunzo aakulu. Mpaka liti, Inu Yehova, mpaka liti?
4 Turn, Lord, and rescue me! Save me because of your trustworthy love!
Tembenukani Inu Yehova, ndipo mundilanditse; pulumutseni chifukwa cha chikondi chanu chosasinthika.
5 For no one remembers you when they're dead. Who is able to praise you from the grave? (Sheol h7585)
Palibe amene amakukumbukirani pamene wamwalira; Amakutamandani ndani ali ku manda? (Sheol h7585)
6 My groaning has exhausted me. Every night I soak my bed with my crying; I drench my couch with my tears.
Ine ndatopa ndi kubuwula; usiku wonse pa bedi panga pamadzaza ndi misozi yanga; ndimanyowetsa pogona panga ndi misozi.
7 With all my crying I can hardly see; my eyes grow weak because of the trouble my enemies cause me.
Maso anga atupa chifukwa cha chisoni; akulephera kuona chifukwa cha adani anga.
8 Leave me alone, all you people who do evil, for the Lord has heard me crying!
Chokani kwa ine inu nonse amene mumachita zoyipa, pakuti Yehova wamva kulira kwanga.
9 The Lord has heard me calling out for help; the Lord answers my prayer.
Yehova wamva kupempha kwanga kofuna chifundo; Yehova walandira pemphero langa.
10 All who hate me will be shamefully defeated and terrified; they will run away in disgrace.
Adani anga onse adzachita manyazi ndipo adzakhala ndi mantha; adzabwerera msangamsanga mwa manyazi.

< Psalms 6 >