< Psalms 47 >
1 For the music director. A psalm of the sons of Korah. Everyone, clap your hands! Shout with joy to the Lord!
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la ana a Kora. Ombani mʼmanja, inu anthu onse; fuwulani kwa Mulungu ndi mawu achimwemwe.
2 For the Lord Most High is awe-inspiring; he is the great King of all the earth.
Ndi woopsadi Yehova Wammwambamwamba; Mfumu yayikulu ya dziko lonse lapansi!
3 He subdues other peoples under us; he puts nations under our feet.
Iye anatigonjetsera mitundu yambirimbiri ya anthu; anayika anthu pansi pa mapazi athu.
4 He chose the land for us to own; the proud possession of Jacob's descendants whom he loves. (Selah)
Iye anatisankhira cholowa chathu, chonyaditsa cha Yakobo, amene anamukonda. (Sela)
5 God ascends his throne with a great shout, the Lord is accompanied by the sound of the trumpet.
Mulungu wakwera, anthu akumufuwulira mwachimwemwe, Yehova wakwera, akumuyimbira malipenga.
6 Sing praises to God, sing praises; sing praises to our King, sing praises!
Imbani matamando kwa Mulungu, imbani matamando; imbani matamando kwa mfumu yathu, imbani matamando.
7 For God is King of all the earth; sing praises with a psalm!
Pakuti Mulungu ndi mfumu ya dziko lonse lapansi; imbirani Iye salimo la matamando.
8 God rules over the nations; he sits on his holy throne.
Mulungu akulamulira mitundu ya anthu; Mulungu wakhala pa mpando wake waufumu woyera.
9 The rulers of the nations gather together with the people of the God of Abraham, for the defenders of the earth belong to God. He is highly honored everywhere.
Anthu otchuka mwa anthu a mitundu ina asonkhana monga anthu a Mulungu wa Abrahamu, pakuti mafumu a dziko lapansi ndi ake a Mulungu; Iye wakwezedwa kwakukulu.