< Psalms 38 >

1 A psalm of David, for a memorial. Lord, please don't condemn me because you're angry with me; don't punish me because you're furious with me!
Salimo la Davide. Kupempha. Yehova musandidzudzule mutapsa mtima kapena kundilanga muli ndi ukali.
2 Your arrows have pierced me deeply, your hand has come down hard on me.
Pakuti mivi yanu yandilasa, ndipo dzanja lanu latsika ndipo landifikira.
3 Because you're so upset with me, not a single part of my body is healthy; I am completely sick because of my sins.
Chifukwa cha ukali wanu mulibe thanzi mʼthupi langa; mafupa anga alibe mphamvu chifukwa cha tchimo langa.
4 I'm drowning in guilt—the burden is too heavy to bear.
Kulakwa kwanga kwandipsinja ngati katundu wolemera kwambiri kuposa mphamvu zanga.
5 My wounds are infected—they're smelling—all because of my stupidity.
Mabala anga akuwola ndipo akununkha chifukwa cha uchitsiru wa moyo wanga wauchimo.
6 I am bent over, doubled up in pain. The whole day I walk around crying my eyes out.
Ine ndapindika msana ndipo ndawerama kwambiri; tsiku lonse ndimangolira.
7 Inside I'm burning up with fever; no part of my body is healthy.
Msana wanga wagwidwa ndi ululu wosasimbika, mulibe thanzi mʼthupi langa.
8 I'm worn out, totally down. I groan because of the anguish I feel in my heart.
Ndilibe mphamvu ndipo ndakunthidwa kwathunthu; ndikubuwula ndi ululu wa mumtima.
9 Lord, you know what I desperately want, you hear every sigh I make.
Zokhumba zanga zonse zili poonekera pamaso panu Ambuye, kusisima kwanga sikunabisike kwa Inu.
10 My heart is racing, leaving me with no strength; my eyesight is failing.
Mtima wanga ukugunda, mphamvu zanga zikutha; ngakhale kuwala kwachoka mʼmaso mwanga.
11 My loved ones and my friends don't come near me because they're afraid of what I've got. Even my family keeps me at a distance.
Abwenzi anga ndi anzanga akundipewa chifukwa cha mabala anga; anansi anga akhala kutali nane.
12 Those who are trying to kill me set traps for me; those who want to hurt me make threats against me, working on their deceitful schemes all day long.
Iwo amene akufunafuna moyo wanga atchera misampha yawo, oti andipwetekewo amayankhula za kuwonongeka kwanga; tsiku lonse amakonza zachinyengo.
13 I act as if I'm deaf to what they're saying, and pretend to be dumb so I don't have to speak.
Ine ndili ngati munthu wosamva amene sangamve, monga wosayankhula, amene sangathe kutsekula pakamwa pake;
14 Like a man who can't hear, and who doesn't reply—that's me!
Ndakhala ngati munthu amene samva, amene pakamwa pake sipangathe kuyankha.
15 For I'm waiting on you, Lord! You will answer for me, my Lord and my God.
Ndikudikira Inu Yehova; mudzayankha, Inu Ambuye Mulungu wanga.
16 I'm asking you, Lord, please don't let my enemies gloat over me, don't let them be glad when I trip up.
Pakuti Ine ndinati, “Musawalole kuti akondwere kapena kudzikweza okha pa ine pamene phazi langa laterereka.”
17 For I'm about ready to collapse—the pain never stops.
Pakuti ndili pafupi kugwa, ndipo ndikumva kuwawa nthawi zonse.
18 I do confess my sins; I am terribly sorry for what I've done.
Ndikuvomereza mphulupulu zanga; ndipo ndavutika ndi tchimo langa.
19 I have many powerful enemies—they are very active, hating me for no reason.
Ambiri ndi adani anga amphamvu; amene amandida popanda chifukwa alipo ochuluka kwambiri.
20 They pay me back evil for good; they accuse me for the good I try to do.
Iwo amene amandibwezera zoyipa mʼmalo mwa zabwino amandinyoza pamene nditsatira zabwino.
21 Don't give up on me, my Lord and my God, don't stay away from me.
Inu Yehova, musanditaye; musakhale kutali ndi ine Mulungu wanga.
22 Hurry, come and help me, Lord my salvation.
Bwerani msanga kudzandithandiza, Inu Ambuye Mpulumutsi wanga.

< Psalms 38 >