< Psalms 35 >
1 A psalm of David. Oppose my opponents, Lord; fight those who are fighting against me.
Salimo la Davide. Inu Yehova, mulimbane nawo amene akulimbana nane; mumenyane nawo amene akumenyana nane.
2 Put your armor on, and pick up your shield. Get ready, come and help me.
Tengani chishango ndi lihawo; dzukani ndipo bwerani mundithandize.
3 Draw your spear and your javelin, confront those who are chasing me. Tell me, “I am your salvation!”
Tengani mkondo ndi nthungo, kulimbana ndi iwo amene akundithamangitsa. Uzani moyo wanga kuti, “Ine ndine chipulumutso chako.”
4 Shame them! Humiliate those who are trying to kill me! Turn them back! Disgrace those who are planning to hurt me!
Iwo amene akufunafuna moyo wanga anyozedwe ndi kuchita manyazi; iwo amene akukonza kuti moyo wanga uwonongeke abwerere mʼmbuyo mochititsa mantha.
5 Let them be like chaff blown by the wind; let the angel of the Lord drive them away.
Akhale ngati mankhusu owuluka ndi mphepo pamene mngelo wa Yehova akuwapirikitsa.
6 May their path be dark and slippery, with the angel of the Lord chasing them down.
Njira yawo ikhale ya mdima ndi yoterera pamene mngelo wa Yehova akuwathamangitsa.
7 For no reason they set a net to catch me; for no reason they dug a pit to trap me.
Popeza ananditchera ukonde popanda chifukwa ndipo popanda chifukwa andikumbira dzenje,
8 Let disaster come on them suddenly; let the net they set catch them instead; let the pit they dug trap them instead.
chiwonongeko chiwapeza modzidzimutsa ukonde umene iwo abisa uwakole, agwere mʼdzenje kuti awonongedwe.
9 Then I will be glad in the Lord; I will be happy in his salvation.
Pamenepo moyo wanga udzakondwera mwa Yehova ndi kusangalala ndi chipulumutso chake.
10 Every part of me will say, Who can compare to you, Lord? You rescue the weak from the strong; the poor and needy from robbers.
Thupi langa lidzafuwula mokondwera, “Ndani angafanane nanu Yehova? Mumalanditsa osauka kwa amene ali ndi mphamvu zambiri, osauka ndi osowa kwa iwo amene amawalanda.”
11 Hostile witnesses stand up to testify against me, accusing me of crimes I don't know anything about.
Mboni zopanda chisoni zinayimirira, zinandifunsa zinthu zimene sindikuzidziwa.
12 They pay me back with evil instead of good. I feel like giving up.
Iwo anandibwezera zoyipa pa zabwino ndipo anasiya moyo wanga pa chisoni.
13 But when they were sick, I put on clothes of sackcloth in sympathy. I denied myself through fasting. May my prayer for them return to bless me too.
Koma pamene iwo ankadwala, ine ndinavala chiguduli ndi kudzichepetsa ndekha posala zakudya. Pamene mapemphero anga anabwerera kwa ine osayankhidwa,
14 I was upset for them, as if they were my own friends or family; I bowed down in grief as if I was mourning my own mother.
ndinayendayenda ndi kulira maliro, kumulira ngati bwenzi langa kapena mʼbale wanga. Ndinaweramitsa mutu wanga mosweka mtima kukhala ngati ndikulira amayi anga.
15 But when I was in trouble, they gathered around and laughed at me. Even strangers I don't know attacked me, constantly tearing me apart.
Koma pamene ndinaphunthwa, iwo anasonkhana mosangalala; ondithira nkhondo anasonkhana kutsutsana nane, ineyo osadziwa. Iwo sanasiye kundiyankhulira mawu onyoza.
16 Like irreligious people mocking a cripple they mock me and call me names, gnashing their teeth at me.
Monga anthu osapembedza, iwo anandinyoza mwachipongwe; anandikukutira mano awo.
17 How long, Lord, will you sit by and just watch? Save me from their vicious attacks; defend the only life I have from these lions.
Ambuye, mpaka liti mudzakhala mukungoyangʼana? Landitsani moyo wanga ku chiwonongeko chawo, moyo wanga wopambana ku mikango.
18 Then I will thank you in front of the whole congregation and praise you in front of all the people.
Ndidzakuyamikani mu msonkhano waukulu; pakati pa gulu lalikulu la anthu ndidzakutamandani.
19 Don't let my enemies take pleasure in my troubles, those people who hate me and tell lies about me, gloating over me for no reason.
Musalole adani anga onyenga akondwere chifukwa cha masautso anga; musalole kuti amene amadana nane popanda chifukwa andiyangʼane chamʼmbali mondinyoza.
20 They are not looking for peace; they invent malicious and deceptive schemes against innocent peace-loving people.
Iwowo sayankhula mwamtendere, koma amaganizira zonamizira iwo amene amakhala mwabata mʼdziko.
21 They open their mouths wide to make accusations against me, saying, “Look! Look! We saw it with our own eyes!”
Iwo amandiseka mofuwula ndipo amati, “Haa! Haa! Ndipo ndi maso athuwa ife taziona.”
22 But Lord, you've seen all this! Say something! Don't give up on me, Lord!
Yehova mwaona zimenezi; musakhale chete. Ambuye musakhale kutali ndi ine.
23 Wake up! Get up and defend me, my Lord and my God! Take up my case and make sure justice is done!
Dzukani, ndipo nyamukani kunditeteza! Mulimbane nawo chifukwa cha ine, Mulungu wanga ndi Ambuye anga.
24 Vindicate me, my Lord and my God, because you are just and right. Don't let them gloat over me.
Onetsani kusalakwa kwanga mwa chilungamo chanu, Inu Yehova Mulungu wanga. Musalole kuti akondwere chifukwa cha mavuto anga.
25 Don't let them say to themselves, “Look! We got what we wanted!” Don't let them say, “We completely destroyed him!”
Musalole kuti aganize kuti, “Amati atani, zachitika monga momwe timafunira!” Kapena kunena kuti, “Tamutha ameneyu basi.”
26 Make them totally ashamed, all those who are happy for the trouble I'm in. Let those who are celebrating over me be covered with shame and dishonor.
Onse amene amakondwera ndi masautso anga achite manyazi ndi kusokonezeka. Onse amene amadzikweza kufuna kundipambana, avekedwe manyazi ndi mnyozo ngati zovala.
27 Instead let those who are pleased I've been vindicated celebrate and shout for joy. Let them always say, “How great is the Lord! He is happy when his servants live in peace and have what they need.”
Koma amene amakondwera chifukwa chakuti ndine wosalakwa, afuwule mwachimwemwe ndi chisangalalo. Nthawi zonse azinena kuti, “Yehova akwezeke, Iye amene amakondwera ndi kupeza bwino kwa mtumiki wake.”
28 I will tell others about your character of truth and right, praising you all day long!
Pakamwa panga padzayankhula za chilungamo chanu ndi za matamando anu tsiku lonse.