< Psalms 22 >
1 For the music director. To the tune “Doe of the Dawn.” A psalm of David. My God, my God, why have you abandoned me? Why are you so far away when I groan, asking for help?
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Monga mwa “Mbawala yayikazi ya Mmawa.” Salimo la Davide. Mulungu wanga, Mulungu wanga, nʼchifukwa chiyani mwandisiya? Chifuwa chiyani simukundithandiza ndi pangʼono pomwe? Nʼchifukwa chiyani simukumva mawu a kudandaula kwanga?
2 My God, every day I cry out to you, but you don't answer; at night too, but I get no rest.
Inu Mulungu wanga, ine ndimalira masana, koma simuyankha, usikunso, ndipo sindikhala chete.
3 Yet you are holy, and the praises of Israel are your throne.
Inu ndinu Woyera, wokhala pa mpando waufumu; ndinu matamando a Israeli.
4 Our forefathers trusted in you; they trusted and you rescued them.
Pa inu makolo athu anadalira; iwo anadalira ndipo Inu munawapulumutsa.
5 They cried out to you for help, and they were saved. They trusted in you and were not defeated.
Analirira kwa inu ndipo munawapulumutsa. Iwo anakhulupirira Inu ndipo simunawakhumudwitse.
6 But I'm a worm, not a man, scorned and despised by everyone.
Koma ine ndine nyongolotsi osati munthu, wosekedwa ndi wonyozedwa ndi anthu onse.
7 People who see me mock me. They laugh at me and shake their heads, saying,
Onse amene amandiona amandiseka; amandiyankhulira mawu achipongwe akupukusa mitu yawo kunena kuti
8 “He trusts in the Lord—well then, let the Lord save him! If the Lord is such a friend, then let the Lord rescue him!”
“Iyeyu amadalira Yehova, musiyeni Yehovayo amulanditse. Musiyeni Yehova amupulumutse popeza amakondwera mwa Yehovayo.”
9 However, you brought me safely through birth, and led me to trust in you at my mother's breasts.
Komabe Inu ndinu amene munandibadwitsa, munanditulutsa mʼmimba mwa amayi anga. Munachititsa kuti ndizikudalirani ngakhale pa nthawi imene ndinkayamwa.
10 I was entrusted to you from birth; from the time I was born you have been my God.
Chibadwire ine ndinaperekedwa kwa Inu; kuchokera mʼmimba mwa amayi anga Inu mwakhala muli Mulungu wanga.
11 Do not be distant from me, because trouble is close by and no one else can help.
Musakhale kutali ndi ine, pakuti mavuto ali pafupi ndipo palibe wina wondipulumutsa.
12 Enemies surround me like a herd of bulls; strong bulls from Bashan have encircled me.
Ngʼombe zazimuna zandizungulira; ngʼombe zazimuna zamphamvu za ku Basani zandizinga.
13 Like roaring lions tearing at their prey they open their mouths wide against me.
Mikango yobangula pokadzula nyama, yatsekula kwambiri pakamwa pawo kulimbana nane.
14 I feel like I'm being poured out like water. I'm falling apart as if all my bones have become loose. My mind feels like it's wax melting inside me.
Ine ndatayika pansi ngati madzi ndipo mafupa anga onse achoka mʼmalo mwake. Mtima wanga wasanduka phula; wasungunuka mʼkati mwanga.
15 My strength has dried up like a piece of broken pottery. My tongue is stuck to the roof of my mouth. You're burying me as if I'm already dead.
Mphamvu zanga zauma ngati phale, ndipo lilime langa lamamatira ku nsagwada; mwandigoneka mʼfumbi la imfa.
16 Evil men surround me like a pack of dogs. They have pierced my hands and feet.
Agalu andizungulira; gulu la anthu oyipa landizinga. Alasa manja ndi mapazi anga.
17 I'm so thin I can count all my bones. People stare at me and gloat.
Ine nditha kuwerenga mafupa anga onse; anthu amandiyangʼanitsitsa ndi kundidzuma.
18 They divide my clothing among them; they roll dice for my clothes.
Iwo agawana zovala zanga pakati pawo ndi kuchita maere pa zovala zangazo.
19 But you, Lord, don't be far away from me! You are my strength—hurry, come and help me!
Koma Inu Yehova, musakhale kutali; Inu mphamvu yanga, bwerani msanga kuti mudzandithandize.
20 Save me from death by the sword! Save my life—the only one I have—from the dogs!
Pulumutsani moyo wanga ku lupanga, moyo wanga wopambanawu ku mphamvu ya agalu.
21 Rescue me from the mouth of the lion and from the wild bulls!
Ndilanditseni mʼkamwa mwa mikango; pulumutseni ku nyanga za njati.
22 I will tell my people all the wonderful things you have done; I will praise you in the congregation.
Ine ndidzalengeza dzina lanu kwa abale anga; ndidzakutamandani mu msonkhano.
23 Praise the Lord, all who worship him! Honor him, every descendant of Jacob! Be in awe of him, every descendant of Israel!
Inu amene mumaopa Yehova mutamandeni! Inu zidzukulu zonse za Yakobo, mulemekezeni! Muopeni mwaulemu, inu zidzukulu zonse za Israeli!
24 For he has not ridiculed or scorned the suffering of the poor; he has not turned away from them, he has listened to their cries for help.
Pakuti Iye sanapeputse kapena kunyoza kuvutika kwa wosautsidwayo; Iye sanabise nkhope yake kwa iye. Koma anamvera kulira kwake kofuna thandizo.
25 You are the subject of my praise in the great assembly. I will fulfill my promises before those who worship you.
Ndidzakutamandani pa msonkhano waukulu chifukwa cha zimene mwandichitira. Ndidzakwaniritsa lonjezo langa pamaso pa amene amaopa Inu.
26 The poor shall eat, and they shall be satisfied. All who come to the Lord will praise him—may you all live forever!
Osauka adzadya ndipo adzakhuta; iwo amene amafunafuna Yehova adzamutamanda. Mitima yanu ikhale ndi moyo mpaka muyaya!
27 Everyone in the whole world will repent and return to the Lord; all the nations will worship before you.
Malekezero onse a dziko lapansi adzakumbukira Yehova ndi kutembenukira kwa Iye, ndipo mabanja a mitundu ya anthu adzawerama pamaso pake,
28 For kingly power belongs to the Lord; he is the one who rules over the nations.
pakuti ulamuliro ndi wake wa Yehova ndipo Iye amalamulira anthu a mitundu yonse.
29 All who prosper come to feast and worship. Bow down before him, all those destined for the grave—for none can keep themselves alive.
Anthu olemera onse a dziko lapansi adzachita phwando ndi kulambira; onse amene amapita ku fumbi adzagwada pamaso pake; iwo amene sangathe kudzisunga okha ndi moyo.
30 Our descendants will serve him; they will tell the next generation about the Lord.
Zidzukulu zamʼtsogolo zidzamutumikira Iye; mibado ya mʼtsogolo idzawuzidwa za Ambuye.
31 They will come and tell those yet to be born how good the Lord is, and all that he has done!
Iwo adzalengeza za chilungamo chake kwa anthu amene pano sanabadwe pakuti Iye wachita zimenezi.