< Psalms 114 >

1 At the time of the exodus of Israel from Egypt, when the descendants of Jacob left that foreign country,
Pamene Israeli anatuluka mu Igupto, nyumba ya Yakobo kuchoka ku mtundu wa anthu a chiyankhulo chachilendo,
2 the land of Judah became the Lord's sanctuary, Israel his kingdom.
Yuda anasanduka malo opatulika a Mulungu, Israeli anasanduka ufumu wake.
3 The Red Sea saw them and ran away; the Jordan River retreated.
Nyanja inaona ndi kuthawa, mtsinje wa Yorodani unabwerera mʼmbuyo;
4 Mountains jumped in fright like rams, hills startled like lambs.
mapiri analumphalumpha ngati nkhosa zazimuna, timapiri ngati ana ankhosa.
5 Red Sea—why did you run away? Jordan River—why did you retreat?
Nʼchifukwa chiyani iwe unathawa? iwe mtsinje wa Yorodani unabwereranji mʼmbuyo?
6 Mountains—why did you jump in fright? Hills—why did you startle like lambs?
inu mapiri, munalumphalumphiranji ngati nkhosa zazimuna, inu timapiri, ngati ana ankhosa?
7 Earth, tremble in the presence of the Lord, tremble in the presence of the God of Jacob!
Njenjemera pamaso pa Ambuye iwe dziko lapansi, pamaso pa Mulungu wa Yakobo,
8 He is the one who turned the rock into a pool of water; making water flow from the hard rock.
amene anasandutsa thanthwe kukhala chitsime, thanthwe lolimba kukhala akasupe a madzi.

< Psalms 114 >