< Proverbs 9 >
1 Wisdom has built her house; she has prepared its seven pillars.
Nzeru inamanga nyumba yake; inayimika nsanamira zake zisanu ndi ziwiri.
2 She has slaughtered her animals for meat; she has mixed her wine; and she has set her table.
Inapha ziweto zake ndipo yasakaniza vinyo wake; inasakaniza vinyo wake ndi kuyala tebulo lake.
3 She has sent out her servant girls with invitations. She calls out from the highest places of the town,
Nzeruyo inatuma adzakazi ake, kuti akakhale pamwamba penipeni pa mzinda ndi kukalengeza kuti,
4 “Everybody who needs to learn, come and see me!” To people who don't have any sense she says,
“Aliyense amene ali munthu wamba, abwere kuno!” Kwa onse opanda nzeru inkanena kuti,
5 “Come, eat my food, and drink the wine I have mixed.
“Bwerani, dzadyeni chakudya changa ndipo dzamweni vinyo amene ndakonza.
6 Leave your foolish ways and you will live; follow the path that makes sense.”
Lekani zopusa zanu kuti mukhale ndi moyo; yendani njira ya nzeru yomvetsa zinthu.”
7 If you correct a mocker all you get are insults; if you argue with the wicked all you get is abuse.
Aliyense amene amayesa kukonza munthu wonyoza amadziputira minyozo; aliyense amene amadzudzula munthu woyipa amadetsa mbiri yake.
8 So don't argue with mockers or they'll only hate you; argue with the wise and they'll love you.
Usadzudzule munthu wonyoza kuti angadzadane nawe; dzudzula munthu wanzeru ndipo adzakukonda.
9 Educate the wise and they'll become even wiser; teach those who live right and they will increase their learning.
Ukalangiza munthu wanzeru ndiye adzapitirira kukhala wanzeru; ukaphunzitsa munthu wolungama ndiye adzawonjezera kuphunzira kwake.
10 Honoring the Lord is the beginning of wisdom; knowledge of the Holy One brings insight.
Kuopa Yehova ndiye chiyambi cha nzeru; kudziwa Woyerayo ndiko kukhala womvetsa bwino zinthu.
11 Through wisdom you'll have many more days, increasing the years of your life.
Chifukwa cha ine nzeru, masiku ako adzachuluka, ndipo zaka za moyo wako zidzawonjezeredwa.
12 If you are wise, you are the one to profit from it; if you scoff, you alone will have to suffer the consequences.
Ngati ndiwe wanzeru, nzeru yakoyo idzakupindulitsa; ngati ndiwe wonyoza ena, udzavutika wekha.
13 Stupidity is like a loud, ignorant woman who doesn't know anything.
Uchitsiru ndi mkazi waphokoso, wopulikira ndiponso wosadziwa zinthu.
14 She sits at the door of her house, on a seat in the high places of the town,
Iye amakhala pa mpando, pa khomo la nyumba yake, pamalo aatali a mu mzinda,
15 calling out to those passing by, going about their business,
kuti aziyitana anthu ongodutsa, amene akunka nayenda njira zawo.
16 “Everybody who needs to learn, come and see me!” To people who don't have any sense she says,
Amati, “Onse amene ndi anthu wamba abwere kuno,” ndipo kwa wopanda nzeru amati,
17 “Stolen water is sweet, and food eaten in secret tastes good!”
“Madzi akuba ndiye amatsekemera; chakudya chodya mobisa ndi chokoma!”
18 But they don't know that the dead are there, that those she's invited are in the depths of the grave. (Sheol )
Koma amunawo sadziwa kuti akufa ali kale komweko, ndi kuti alendo ake alowa kale mʼmanda akuya. (Sheol )