< Numbers 8 >

1 The Lord told Moses,
Yehova anawuza Mose kuti,
2 “Tell Aaron, ‘When you place the seven lamps on the lampstand, make sure they shine towards the front.’”
“Yankhula ndi Aaroni kuti pamene uyimika nyale zisanu ndi ziwiri, nyalezo ziziyaka kutsogolo kwa choyikapo nyale.”
3 So that's what Aaron did. He placed the lamps facing towards the front of the lampstand, as the Lord had ordered Moses.
Aaroni anachitadi zomwezo. Anayimika nyale ndi kuziyangʼanitsa kumene kunali choyikapo nyale monga Yehova analamulira Mose.
4 The lampstand was made of hammered gold from its base to the flower decorations on the top, in accordance with the design that the Lord had shown Moses.
Choyikapo nyalecho chinapangidwa motere: chinasulidwa kuchokera ku golide, kuyambira pa tsinde pake mpaka ku maluwa ake. Choyikapo nyalecho chinapangidwa monga momwe Yehova anaonetsera Mose.
5 The Lord told Moses,
Yehova anawuza Mose kuti,
6 “Separate the Levites from the other Israelites and purify them.
“Tenga Alevi pakati pa Aisraeli ndipo uwayeretse.
7 This is how you will purify them. Sprinkle on them the water of purification. They are to shave off all the hair from their bodies and wash their clothes so they will be clean.
Powayeretsa uchite izi: uwawaze madzi oyeretsa ndipo amete thupi lawo lonse ndi kuchapa zovala zawo kuti adziyeretse.
8 Have them bring a young bull with its grain offering of the best flour mixed with olive oil, and you are to bring a second young bull as a sin offering.
Atenge ngʼombe yayimuna yayingʼono ndi chopereka cha chakudya cha ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta. Atengenso ngʼombe ina yayimuna, yayingʼono, ya chopereka chopepesera machimo.
9 Take the Levites and have them stand in front of the Tent of Meeting and have all the Israelites gather there.
Ubwere nawo Aleviwo kutsogolo kwa tenti ya msonkhano ndipo usonkhanitse gulu la Aisraeli.
10 When you bring the Levites to the Lord the Israelites are to place their hands upon them.
Ubwere nawo pamaso pa Yehova, ndipo Aisraeli asanjike manja awo pa iwo.
11 Aaron shall present the Levites to the Lord as a wave offering from the Israelites so that they can do the Lord's work.
Aaroni apereke Alevi aja pamaso pa Yehova ngati chopereka choweyula kuchokera kwa Aisraeli kuti akhale okonzeka kugwira ntchito ya Yehova.
12 The Levites are to place their hands on the heads of the bulls. One is to be sacrificed as a sin offering to the Lord, and the other as a burnt offering to set the Levites right with the Lord.
“Alevi akatsiriza kusanjika manja awo pa mitu ya ngʼombe zazimuna, imodzi ikhale ya nsembe yopepesera machimo ndipo inayo ikhale ya nsembe yopsereza ya kwa Yehova, kupepesera machimo a Alevi.
13 Have the Levites stand in front of Aaron and his sons and present them to the Lord as a wave offering.
Uyimiritse Aleviwo pamaso pa Aaroni ndi ana ake aamuna ndipo uwapereke ngati nsembe yoweyula kwa Yehova.
14 This is how you are to separate the Levites from the rest of the Israelites, and the Levites will belong to me.
Pochita zimenezi mudzapatula Alevi pakati pa Aisraeli ndipo Aleviwo adzakhala anga.
15 They can come and serve at the Tent of Meeting once you've purified them and presented them as a wave offering.
“Utatha kuyeretsa ndi kupereka Aleviwo monga nsembe yoweyula, apite kukagwira ntchito yawo ku tenti ya msonkhano.
16 The Levites have been completely given over to me by the Israelites. I have accepted them as mine in place of all the firstborn sons of the Israelites.
Iwo ndiwo Aisraeli amene aperekedwa kwathunthu kwa Ine. Ndawatenga kuti akhale anga mʼmalo mwa mwana wamwamuna aliyense woyamba kubadwa wa Mwisraeli aliyense wamkazi.
17 Every firstborn male in Israel belongs to me, both human and animal. I reserved them for myself at the time when I killed all the firstborn in Egypt.
Mwana aliyense wamwamuna woyamba kubadwa mu Israeli, kaya wa munthu kapena wa ziweto, ndi wanga. Pamene ndinakantha ana oyamba kubadwa ku Igupto, ndinawapatulira kwa Ine mwini.
18 I have taken the Levites in place of all the firstborn sons of the Israelites.
Ndipo ndatenga Alevi mʼmalo mwa ana aamuna onse oyamba kubadwa mu Israeli.
19 Of all the Israelites, the Levites are a gift from me to Aaron and his sons to serve the Israelites at the Tent of Meeting, and on their behalf to set them right, so that nothing bad will happen to them when they come to the sanctuary.”
Mwa Aisraeli onse, ndapereka Alevi kuti akhale mphatso kwa Aaroni ndi ana ake aamuna kugwira ntchito ya ku tenti ya msonkhano mʼmalo mwa Aisraeli onse kuti azikapereka nsembe yopepesera machimo, kuti mliri usadzaphe Aisraeli pamene ayandikira ku malo wopatulika.”
20 Moses, Aaron, and all the Israelites did everything that the Lord had ordered Moses that they should do regarding the Levites.
Mose, Aaroni pamodzi ndi gulu lonse la Israeli anachita kwa Alevi monga momwe Yehova analamulira Mose.
21 The Levites purified themselves and washed their clothes. Then Aaron presented them as a wave offering to the Lord. Aaron also presented the sacrifice to make them right with the Lord so they would be clean.
Alevi anadziyeretsa ndi kuchapa zovala zawo. Kenaka Aaroni anawapereka ngati nsembe yoweyula pamaso pa Yehova ndi kuchita nsembe yopepesera machimo yowayeretsa.
22 Afterwards the Levites came to perform their service at the Tent of Meeting under the direction of Aaron and his sons. They followed all the instructions regarding the Levites that the Lord had given to Moses.
Zitatha zimenezi, Alevi anapita kukagwira ntchito yawo ku tenti ya msonkhano motsogozedwa ndi Aaroni ndi ana ake aamuna. Anachita kwa Alevi monga momwe Yehova analamulira Mose.
23 The Lord told Moses,
Yehova anawuza Mose kuti,
24 “This rule applies to the Levites. Those twenty-five or older shall serve at the Tent of Meeting.
“Ntchito za Alevi ndi izi: Amuna a zaka 24 kapena kuposera pamenepa ndiye azibwera kudzagwira ntchito ku tenti ya msonkhano.
25 However, once they reach the age of fifty they need to retire from the work and won't serve any longer.
Koma akakwana zaka makumi asanu, apume pa ntchito yawo ya tsiku ndi tsiku ndi kulekeratu kugwira ntchitoyo.
26 They can still help their fellow Levites in their assignments, but they are not to do the actual work themselves. These are the arrangements in the case of the Levites.”
Atha kuthandiza abale awo kugwira ntchito za ku tenti ya msonkhano, koma iwowo asamagwire ntchitoyo. Mmenemu ndimo ugawire ntchito yomwe azigwira Alevi.”

< Numbers 8 >