< Numbers 34 >
Yehova anawuza Mose kuti,
2 “Give this command to the Israelites: ‘When you enter the country of Canaan, it will be allocated to you to own with the following boundaries:
“Lamula Aisraeli ndipo uwawuze kuti, ‘Pamene mulowa mʼdziko la Kanaani, dziko lomwe lidzaperekedwa kwa inu ngati cholowa chanu, lidzakhale ndi malire awa:
3 The southern extent of your country will be from the Desert of Zin along the border of Edom. Your southern border will run east from the end of the Dead Sea,
“‘Chigawo cha kummwera kwa dziko lanu chidzayambira ku chipululu cha Zini motsatana ndi malire a Edomu. Kummawa malire anu a kummwera adzayambira kummawa, kumathero a Nyanja ya Mchere.
4 cross south of Scorpion Pass, on to Zin, and reach its southern limit south of Kadesh-barnea. Then it will go to Hazar-addar and on to Azmon.
Malirewo adzapita kummwera ndipo adzakwera phiri la Akirabimu mpaka ku Zini. Mathero ake adzakhala kummwera kwa Kadesi-Baranea. Ndipo adzapitenso ku Hazari Adari mpaka kukafika ku Azimoni,
5 There the boundary will turn from Azmon to the Wadi of Egypt, ending at the Mediterranean Sea.
kumene malirewo adzakhote kuchokera ku Azimoni mpaka ku khwawa la ku Igupto ndi kukathera ku Nyanja Yayikulu.
6 Your western border will be the coast of the Mediterranean Sea. This is to be your boundary to the west.
“‘Malire anu a ku madzulo adzakhala ku gombe la Nyanja Yayikulu. Amenewo ndiwo adzakhale malire anu a ku madzulo.
7 Your northern border will run from the Mediterranean Sea straight to Mount Hor.
“‘Malire anu a kumpoto, mzere wake uyambire ku Nyanja Yayikulu mpaka ku phiri la Hori
8 From Mount Hor the boundary will go to Lebo-hamath, then on to Zedad,
ndi kuchokera ku phiri la Hori mpaka ku Lebo Hamati. Malirewa apite ku Zedadi,
9 to Ziphron, ending at Hazar-enan. This will be your boundary to the north.
ndi kupitirira mpaka ku Ziforoni ndi kukathera ku Hazari-Enani. Awa ndiwo adzakhale malire anu a kumpoto.
10 Your eastern border will run straight from Hazar-enan to Shepham
“‘Za malire anu a kummawa, mulembe mzere kuchokera ku Hazari-Enani mpaka kukafika ku Sefamu.
11 Then the boundary will go down from Shepham to Riblah on the east side of Ain. It will pass down along the slopes east of the Sea of Galilee.
Malirewo adzatsikire ku Sefamu mpaka ku Ribila cha kummawa kwa Aini ndi kupitirira mpaka ku matsitso a cha kummawa kwa Nyanja ya Kinereti.
12 Then the boundary will go down along the Jordan, ending at the Dead Sea. This is to be your land with its surrounding borders.’”
Tsono malirewo adzatsika motsatana ndi Yorodani ndi kukathera ku Nyanja ya Mchere. “‘Limeneli lidzakhala dziko lanu ndi malire ake mbali zonse.’”
13 Moses gave the order to the Israelites, “Allocate ownership of this land by lot. The Lord has commanded it to be given to the nine and a half tribes.
Ndipo Mose analamula Aisraeli kuti, “Limeneli ndi dziko limene mudzalilandira pochita maere kuti likhale cholowa chanu. Yehova analamula kuti liperekedwe ku mafuko asanu ndi anayi ndi theka,
14 The tribes of Reuben and Gad, together with the half-tribe of Manasseh, have already received their allocation.
chifukwa mabanja a fuko la Rubeni, fuko la Gadi, ndi theka la fuko la Manase analandiriratu cholowa chawo.
15 These two and a half tribes have received their allocation on the east side of the Jordan opposite Jericho.”
Mafuko awiriwa pamodzi ndi theka la fuko la Manase analandiriratu cholowa chawo patsidya pa mtsinje wa Yorodani ku Yeriko cha kummawa kotulukira dzuwa.”
Yehova anawuza Mose kuti,
17 “These are the names of the men who will be in charge of allocating ownership of the land for you: Eleazar the priest and Joshua, son of Nun.
“Awa ndi mayina a anthu amene adzakugawireni dzikoli kuti likhale cholowa chanu: wansembe Eliezara ndi Yoswa mwana wa Nuni.
18 Have one leader from each tribe help in the distribution of the land.
Musankhe mtsogoleri mmodzi kuchokera ku fuko lililonse kuti athandize kugawa dzikolo.
19 These are their names: From the tribe of Judah: Caleb, son of Jephunneh.
Mayina awo ndi awa: Kalebe mwana wa Yefune, wochokera ku fuko la Yuda,
20 From the tribe of Simeon: Shemuel, son of Ammihud.
Semueli mwana wa Amihudi, wochokera ku fuko la Simeoni;
21 From the tribe of Benjamin: Elidad, son of Chislon.
Elidadi mwana wa Kisiloni, wochokera ku fuko la Benjamini;
22 A leader from the tribe of Dan: Bukki, son of Jogli.
Buki mwana wa Yogili, mtsogoleri wochokera ku fuko la Dani;
23 A leader from the tribe of Manasseh, son of Joseph: Hanniel son of Ephod.
Hanieli mwana wa Efodi, mtsogoleri wochokera ku fuko la Manase, mwana wa Yosefe;
24 A leader from the tribe of Ephraim: Kemuel, son of Shiphtan.
Kemueli mwana wa Sifitani, mtsogoleri wochokera ku fuko la Efereimu, mwana wa Yosefe.
25 A leader from the tribe of Zebulun: Eli-zaphan, son of Parnach.
Elizafani mwana wa Parinaki, mtsogoleri wochokera ku fuko la Zebuloni;
26 A leader from the tribe of Issachar: Paltiel, son of Azzan.
Palitieli mwana wa Azani, mtsogoleri wochokera ku fuko la Isakara,
27 A leader from the tribe of Asher: Ahihud, son of Shelomi.
Ahihudi mwana wa Selomi, mtsogoleri wochokera ku fuko la Aseri;
28 A leader from the tribe of Naphtali: Pedahel, son of Ammihud.”
Pedaheli mwana wa Amihudi, mtsogoleri wochokera ku fuko la Nafutali.”
29 These are the names of those the Lord put in charge of allocating land ownership in the country of Canaan.
Awa ndiwo mayina a anthu amene Yehova analamula kuti agawe cholowa cha Aisraeli mʼdziko la Kanaani.