< Numbers 28 >
Yehova anawuza Mose kuti,
2 “Give the following regulations to the Israelites: ‘You are to present to me at the appropriate times my food offerings for me to accept.
“Lamula Aisraeli kuti, ‘Onetsetsani kuti mukupereka kwa Ine pa nthawi yoyikika, chopereka cha chakudya chotentha pa moto monga fungo lokoma kwa Ine.’
3 Tell them you are to present to the Lord every day two male lambs a year old as a continual burnt offering.
Awuze kuti, ‘Nsembe ya chakudya imene muzipereka pa moto kwa Yehova tsiku ndi tsiku ndi iyi: Ana ankhosa a chaka chimodzi awiri, wopanda chilema.
4 Offer one lamb in the morning and one in the evening before it gets dark,
Mmawa muzipereka mwana wankhosa mmodzi ndipo winayo madzulo.
5 along with one tenth of an ephah of best flour for a grain offering, mixed with a quarter of a hin of pressed olive oil.
Muziperekanso kilogalamu imodzi ya ufa wosalala wosakaniza ndi lita imodzi ya mafuta a olivi.
6 This is a continual burnt offering that was begun at Mount Sinai as an offering acceptable to the Lord.
Iyi ndi nsembe yopsereza ya tsiku ndi tsiku imene analamula pa phiri la Sinai kuti ikhale fungo lokoma, nsembe yopsereza pa moto yopereka kwa Yehova.
7 The drink offering that accompanies each lamb is to be a quarter of a hin. Pour out the offering of fermented drink to the Lord in the sanctuary.
Chopereka chachakumwa chikhale lita imodzi yachakumwa chaukali pa nkhosa iliyonse. Muzithira pamalo opatulika, kupereka kwa Yehova.
8 Offer the second lamb in the evening before it gets dark, along with the same grain and drink offerings as in the morning. It is a burnt offering acceptable to the Lord.
Muzipereka mwana wankhosa winayo madzulo, pamodzi ndi chopereka chachakudya monga poyamba paja ndi chopereka chachakumwa monga mmawa. Ichi ndi chopereka chachakudya, fungo lokoma kwa Yehova.’”
9 On the Sabbath day, present male lambs two years old, without defects, along with a grain offering of two-tenths of an ephah of the best flour mixed with olive oil, and its drink offering.
“‘Pa tsiku la Sabata, muzipereka nsembe ana ankhosa awiri a chaka chimodzi wopanda chilema, pamodzi ndi chopereka chachakumwa ndi chopereka chachakudya chokwana makilogalamu awiri a ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta.
10 This burnt offering is to be presented every Sabbath in addition to the continual burnt offering and its drink offering.
Iyi ndi nsembe yopsereza ya pa Sabata iliyonse, kuwonjezera pa nsembe yopsereza ya nthawi zonse ndi chopereka chake chachakumwa.’”
11 At the start of every month, you are to present to the Lord a burnt offering of two young bulls, one ram, and seven male lambs a year old, all of them without defects,
“Pa tsiku loyamba la mwezi uliwonse muzipereka kwa Yehova nsembe yopsereza ya ana angʼombe aamuna awiri, nkhosa yayimuna imodzi, ana ankhosa aamuna asanu ndi awiri a chaka chimodzi, onse wopanda chilema.
12 along with grain offerings consisting of three-tenths of an ephah of the best flour mixed with olive oil for each bull, two-tenths of an ephah of the best flour mixed with olive oil for the ram,
Pa ngʼombe yayimuna iliyonse pakhale chopereka cha chakudya cha makilogalamu atatu a ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta; ndi nkhosa yayimuna, chopereka cha chakudya cha makilogalamu awiri a ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta;
13 and one tenth of an ephah of the best flour mixed with olive oil for each of the lambs. This is a burnt offering acceptable to the Lord.
ndipo pa mwana wankhosa aliyense, chopereka cha ufa wa kilogalamu imodzi ya ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta, izi ndi za nsembe yopsereza, fungo lokoma, nsembe yotentha pa moto ya kwa Yehova.
14 Their respective drink offerings shall be a half a hin of wine for each bull, a third of a hin for the ram, and a quarter of a hin for each lamb. This is the monthly burnt offering to be presented every month during the year.
Pa ngʼombe yayimuna iliyonse pakhale chopereka cha chakumwa cha malita awiri a vinyo; ndipo pa nkhosa yayimuna, lita limodzi ndi theka, ndipo pa mwana wankhosa, lita limodzi. Iyi ndi nsembe yopsereza ya mwezi ndi mwezi yoperekedwa pa mwezi watsopano mʼkati mwa chaka.
15 As well as the continual burnt offering with its drink offering, present a male goat to the Lord as a sin offering.
Powonjezera pa nsembe yopsereza ya nthawi zonse ndi chopereka chake cha chakumwa, mbuzi yayimuna imodzi iperekedwe kwa Yehova ngati nsembe yopepesera machimo.
16 The Lord's Passover is on the fourteenth day of the first month.
“‘Pa tsiku la 14 la mwezi woyamba muzichita Paska wa Yehova.
17 There shall be a festival on the fifteenth day of this month, and for seven days only eat bread without yeast.
Pa tsiku la 15 la mwezi womwewo pazikhala chikondwerero. Muzidya buledi wopanda yisiti kwa masiku asanu ndi awiri.
18 Hold a holy meeting on the first day of the festival. Don't do any of your normal work.
Pa tsiku loyamba muzichita msonkhano wopatulika ndipo musamagwire ntchito iliyonse.
19 Present to the Lord the following offerings: a burnt offering of two young bulls, one ram, and seven male lambs a year old, all of them without defects.
Koma muzipereka kwa Yehova nsembe yotentha pa moto, nsembe yopsereza ya ana angʼombe aamuna awiri, nkhosa yayimuna imodzi ndi ana ankhosa asanu ndi awiri aamuna a chaka chimodzi, onsewo wopanda chilema.
20 Their grain offerings shall be made of the best flour mixed with olive oil: three-tenths of an ephah for each bull, two-tenths of an ephah for the ram,
Pamodzi ndi ngʼombe yayimuna iliyonse, muzikonza chopereka cha chakudya cha makilogalamu atatu a ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta; makilogalamu awiri pa nkhosa yayimuna iliyonse.
21 and one tenth of an ephah for each of the seven lambs.
Kilogalamu imodzi pa mwana wankhosa aliyense mwa ana ankhosa asanu ndi awiri aja.
22 Also present a male goat as a sin offering to make you right.
Muziphatikizapo mbuzi yayimuna monga nsembe yopepesera machimo anu.
23 You are to present these offerings in addition to the continual morning burnt offering.
Muzikonza zimenezi nthawi zonse, powonjezera pa nsembe yopsereza ya mmawa.
24 Present the same offerings every day for seven days as burnt offerings to be accepted by the Lord. They are to be offered with their drink offering and the continual burnt offering.
Motere muzikonza chakudya cha nsembe yopsereza ya tsiku ndi tsiku pa masiku asanu ndi awiri ngati fungo lokomera Yehova. Zimenezi ziziperekedwa kuwonjezera pa nsembe yopsereza ya nthawi zonse pamodzi ndi nsembe yachakumwa.
25 Hold a holy meeting on the seventh day of the festival. Don't do any of your normal work.
Pa tsiku lachisanu ndi chiwiri muzichita msonkhano wopatulika ndipo musamagwire ntchito iliyonse.
26 During the time you celebrate the Festival of Weeks, hold a holy meeting on the day of firstfruits when you present an offering of new grain to the Lord. Don't do any of your normal work.
“‘Pa tsiku la zipatso zoyambirira kucha, pamene mukupereka chopereka cha chakudya chatsopano kwa Yehova, pa nthawi ya chikondwerero cha Masabata, muzichita msonkhano wopatulika ndipo musagwire ntchito zolemetsa.
27 Present a burnt offering of two young bulls, one ram, and seven male lambs a year old to be accepted by the Lord.
Muzipereka nsembe zopsereza za ana angʼombe aamuna awiri, nkhosa imodzi yayimuna ndi ana ankhosa aamuna asanu ndi awiri a chaka chimodzi monga fungo lokomera Yehova.
28 They are to be accompanied by their grain offerings of the best flour mixed with olive oil: three-tenths of an ephah for each bull, two-tenths of an ephah for the ram,
Pa ngʼombe yayimuna iliyonse pazikhala chopereka cha chakudya cha makilogalamu atatu a ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta, pa nkhosa yayimuna iliyonse makilogalamu awiri.
29 and one tenth of an ephah for each of the seven lambs.
Ndipo pa mwana wankhosa aliyense mwa asanu ndi awiri aja, kilogalamu imodzi.
30 Also present a male goat as an offering to make you right.
Muziperekanso mbuzi yayimuna imodzi kuti izikhala nsembe yopepesera machimo anu.
31 Present these offerings along with their drink offerings in addition to the continual burnt offering and its grain offering. Make sure the animals sacrificed have no defects.”
Muzipereka zimenezi pamodzi ndi zopereka za zakumwa ndi nsembe yake ya chakudya. Onetsetsani kuti nyamazo zilibe chilema.