< Numbers 23 >

1 Then Balaam told Balak, “Build seven altars for me here, and prepare seven bulls and seven rams for me to sacrifice.”
Balaamu anati kwa Balaki, “Mundimangire maguwa ansembe asanu ndi awiri pano, ndipo mukonzenso ngʼombe zazimuna zisanu ndi ziwiri ndi nkhosa zazimuna zisanu ndi ziwiri.”
2 Balak did as Balaam had said, and together they offered a bull and a ram on each altar.
Balaki anachita monga Balaamu ananenera ndipo awiriwo anapereka ngʼombe imodzi ndi nkhosa yayimuna imodzi pa guwa lansembe lililonse.
3 Balaam said to Balak, “Wait here beside your burnt offering while I go and see if perhaps the Lord will come and meet with me. Whatever he reveals to me, I'll share with you.” Then Balaam left to climb up a rocky crag.
Kenaka Balaamu anati kwa Balaki, “Khalani pano pafupi ndi nsembe yanu ineyo ndipite pambali. Mwina Yehova adzabwera kuti akumane nane. Chilichonse chimene akandionetse ndidzakuwuzani” Choncho anapita ku malo okwera a chipululu.
4 God met with him there, and Balaam said. “I have built seven altars and on each altar I have offered a bull and a ram.”
Mulungu anakumana naye ndipo Balaamu anati, “Ndakonza maguwa asanu ndi awiri ndipo pa guwa lililonse ndaperekapo nsembe ya ngʼombe yayimuna imodzi ndi nkhosa yayimuna imodzinso.”
5 The Lord gave Balaam a message to share. He told him, “Go back to Balak and this is what you are to say to him.”
Yehova anawuza Balaamu kuti, “Bwerera kwa Balaki ndipo ukamuwuze uthenga uwu.”
6 So he went back to Balak, who was waiting there beside his burnt offering, along with all the Moabite leaders.
Ndipo anabwerera kwa iye namupeza atayima pafupi ndi nsembe yake pamodzi ndi akuluakulu onse a Mowabu.
7 This is the declaration that Balaam gave: “Balak brought me from Aram; the king of Moab brought me from the mountains of the east. He said, ‘Come and curse Jacob for me! Come and condemn Israel!’
Ndipo Balaamu ananena uthenga wake: “Balaki ananditenga kuchoka ku Aramu, mfumu ya ku Mowabu kuchokera ku mapiri a kummawa. Iye anati, ‘Bwera, temberera Yakobo mʼmalo mwanga, pita nyoza Israeli.’
8 But how can I curse what God has not cursed? How can I condemn what the Lord has not condemned?
Ndingatemberere bwanji amene Mulungu sanawatemberere? Ndinganyoze bwanji amene Yehova sanawanyoze?
9 For I'm looking down on them from the top of rocky crags; I'm watching them from the hills. I see a people who live on their own, different from the other nations.
Kuchokera pamwamba pa mapiri ndikuona anthu, ndikuwaona kuchokera pa zitunda. Ndikuona anthu okhala pawokha, osakhala mʼgulu limodzi ndi mitundu ina.
10 Who can count Jacob's descendants? They are so many they're like dust! Who can count even a quarter of the Israelites? I would like to die as a good person dies! Let the end of my life be like their end!”
Ndani angawerenge zidzukulu za Yakobo zochuluka ngati fumbi, kapena chimodzi mwa zigawo zinayi za Israeli? Lekeni ndife imfa ya oyera mtima, ndi chimaliziro changa chikhale ngati chawo!”
11 Then Balak complained to Balaam, “What on earth have you done to me? I brought you here to curse my enemies, and now look! All you have done is bless them!”
Balaki anati kwa Balaamu, “Wandichitira chiyani? Ndinakuyitana kuti utemberere adani anga, ndipo taona, sunachite chilichonse koma kuwadalitsa!”
12 But Balaam replied, “Don't you think I should I say precisely what the Lord tells me?”
Iye anayankha kuti, “Kodi sindinayenera kuyankhula zimene Yehova anandiwuza?”
13 Then Balak said to him, “Please come with me to another place where you can see them. But you'll only see a part of their camp—you won't see all of them. You can curse them for me from there.”
Kenaka Balaki anawuza Balaamu kuti, “Tiye tipite limodzi ku malo ena komwe ungawaone. Udzangoona gulu limodzi osati onsewo. Ndipo pamenepo, ukawatemberere mʼmalo mwanga.”
14 He took him to the field of Zophim at the top of Mount Pisgah. There he built seven altars and offered a bull and a ram on each altar.
Tsono anamutengera ku munda wa Zofimu pamwamba pa phiri la Pisiga ndipo kumeneko anamanga maguwa ansembe asanu ndi awiri ndipo anapereka nsembe ngʼombe yayimuna imodzi ndi nkhosa yayimuna imodzi pa guwa lansembe lililonse.
15 Balaam told Balak, “Wait here beside your burnt offering while I meet the Lord over there.”
Balaamu anawuza Balaki kuti, “Khalani pano pafupi ndi nsembe yanu pamene ine ndikukakumana ndi Mulungu cha uko.”
16 The Lord met Balaam and gave him a message to share. He told him, “Go back to Balak and this is what you are to say to him.”
Yehova anakumana ndi Balaamu ndipo anamuyankhula kuti, “Bwerera kwa Balaki ndipo ukamuwuze uthenga uwu.”
17 So he went back to Balak, who was waiting there beside his burnt offering, along with all the Moabite leaders. “What did the Lord say?” Balak asked.
Ndipo anapita kwa iye ndipo anamupeza atayimirira pafupi ndi nsembe yake pamodzi ndi akuluakulu a ku Mowabu. Balaki anafunsa Balaamu kuti, “Yehova wayankhula chiyani?”
18 This is the prophecy that Balaam delivered: “Stand up, Balak, and pay attention! Listen to me, son of Zippor!
Pamenepo Balaamu ananena uthenga wake: “Nyamuka Balaki ndipo tamvera; Undimvere iwe mwana wa Zipori.
19 God isn't a human being who would lie. He's not a mere mortal who changes his mind. Does he say he's going to do something but doesn't? Does he make promises he doesn't carry out?
Mulungu si munthu kuti aname, kapena mwana wa munthu kuti asinthe maganizo ake. Kodi amayankhula koma osachita? Kodi amalonjeza koma osakwaniritsa?
20 Look, I have been ordered to give a blessing. God has blessed, and I can't change that.
Wandilamula kuti ndidalitse, Iyeyo wadalitsa ndipo sindingasinthe.
21 He's not expecting anything bad will happen to Jacob; he doesn't foresee any trouble for Israel. The Lord their God is with them; they celebrate him as their king.
“Palibe kuwukira kulikonse kumene wakuona mwa Yakobo, sanaone chovuta mu Israeli. Yehova Mulungu wawo ali nawo: mfuwu wa mfumu uli pakati pawo.
22 God led them out of Egypt with great power, as strong as an ox.
Mulungu wowatulutsa mʼdziko la Igupto, ali ndi mphamvu ngati za njati.
23 No spell can be cast against Jacob; no magic can be used against Israel. People will talk about Jacob and Israel, saying, ‘What amazing things God has done for them!’
Palibe matsenga amene angalimbane ndi Yakobo, palibe mawula amene angalimbane ndi Israeli. Tsopano za Yakobo ndi Israeli adzanena kuti, ‘Onani zimene Mulungu wachita!’
24 Look! The Israelites go out hunting like a lioness; they chase like a lion. They don't rest until they eat their prey, and drink the blood of their dead victim.”
Taonani, anthu anyamuka ngati mkango waukazi; adzuka okha ngati mkango waumuna umene supuma mpaka utadya nyama imene wagwira ndi kumwa magazi a nyama yogwidwayo.”
25 Then Balak said to Balaam, “If you can't give them any curses then at least don't give them any blessings!”
Ndipo Balaki anati kwa Balaamu, “Usawatemberere ndi pangʼono pomwe kapena kuwadalitsa!
26 But Balaam replied, “Didn't I explain to you that I have to do whatever the Lord tells me?”
“Balaamu anayankha Balaki kuti, ‘Kodi sindinakuwuzeni kuti ndiyenera kuchita zimene Yehova wanena?’”
27 “Please come with me and I will take you somewhere else,” Balak said. “Maybe God would let you curse them for me from there.”
Kenaka Balaki anati kwa Balaamu, “Bwera ndikutengere ku malo ena. Mwina chidzamukondweretsa Mulungu kuti uwatemberere kumeneko mʼmalo mwanga.”
28 Balak took Balaam to the top of Mount Peor, which looks down on the wastelands.
Ndipo Balaki anamutengera Balaamu pamwamba pa Peori, poyangʼanana ndi chipululu.
29 Balaam told Balak, “Build seven altars for me here, and prepare seven bulls and seven rams for me to sacrifice.”
Balaamu anati kwa Balaki, “Mundimangire maguwa ansembe asanu ndi awiri pano ndipo mundikonzere ngʼombe zazimuna zisanu ndi ziwiri, nkhosa zazimuna zisanu ndi ziwiri.”
30 Balak what Balaam told him, and he offered a bull and a ram on each altar.
Balaki anachita monga Balaamu ananenera ndipo anapereka nsembe ngʼombe imodzi yayimuna ndi nkhosa imodzi yayimuna pa guwa lililonse.

< Numbers 23 >