< Nehemiah 11 >

1 The leaders of the people were already living in Jerusalem. The rest of the people cast lots to bring one out of ten to come and live in Jerusalem, the holy city, while the other nine would stay in their own cities.
Nthawi imeneyo atsogoleri a anthu ankakhala ku Yerusalemu. Tsono anthu ena onse anachita maere kuti apeze munthu mmodzi pa anthu khumi aliwonse kuti azikhala ku Yerusalemu, mzinda wopatulika. Anthu asanu ndi anayi otsalawo ankakhala mʼmidzi yawo.
2 Everyone praised those who were willing to move to Jerusalem.
Anthu anayamikira onse amene anadzipereka kuti azikhala mu Yerusalemu.
3 This is a list of the leaders of the province who came to live in Jerusalem. (Most of the Israelites lived on their own property in the towns of Judah. This included the priests, the Levites, the Temple servants, and the descendants of Solomon's servants who lived in their home towns.
Aisraeli wamba, ansembe, Alevi, ogwira ntchito ku Nyumba ya Mulungu ndiponso zidzukulu za antchito a Solomoni ankakhala mʼmidzi yawo, aliyense mu dera lake. Koma atsogoleri a chigawo cha Yuda anali atakhazikika mu Yerusalemu.
4 However, some of the people of Judah and Benjamin moved to Jerusalem.) From the tribe of Judah: Athaiah the son of Uzziah, son of Zechariah, son of Amariah, son of Shephatiah, son of Mahalalel, of the sons of Perez;
Ku Yerusalemu kunkakhalanso anthu ena a mafuko a Yuda ndi Benjamini. Ena mwa zidzukulu za Yuda ndi awa: Ataya, mwana wa Uziya, mwana wa Zekariya, mwana wa Amariya mwana wa Sefatiya, mwana wa Mahalaleli. Onsewa anali ana a Perezi.
5 and Maaseiah, son of Baruch, son of Col-hozeh, son of Hazaiah, son of Adaiah, son of Joiarib, son of Zechariah, a descendant of Shelah.
Ena ndi awa: Maaseya mwana wa Baruki, mwana wa Koli-Hoze mwana wa Hazaya, mwana wa Adaya, mwana wa Yowaribu, Zekariya mwana wa Msiloni.
6 The total of the sons of Perez who lived in Jerusalem was 468 men of ability.
Zidzukulu zonse za Perezi, anthu amphamvu zawo amene ankakhala ku Yerusalemu analipo anthu okwanira 468.
7 From the tribe of Benjamin: Sallu, son of Meshullam, son of Joed, son of Pedaiah, son of Kolaiah, son of Maaseiah, son of Ithiel, son of Jeshaiah,
Nazi zidzukulu za Benjamini: Salu mwana wa Mesulamu, mwana wa Yowedi, mwana wa Pedaya, mwana wa Kolaya, mwana wa Maaseiya, mwana wa Itieli, mwana wa Yesaiya.
8 and after him Gabbai and Sallai, a total of 928.
Abale ake anali Gabayi ndi Salaya. Onse pamodzi anali 928.
9 Joel son of Zichri was the officer in charge of them, and Judah son of Hassenuah was in second-in-command of the city.
Yoweli mwana wa Zikiri ndiye anali mtsogoleri wawo, ndipo Yuda mwana wa Hasenuya ndiye amayangʼanira chigawo cha chiwiri cha mzinda.
10 From the priests: Jedaiah, son of Joiarib, Jachin;
Ansembe anali awa: Yedaya mwana wa Yowaribu; Yakini;
11 Seraiah, son of Hilkiah, son of Meshullam, son of Zadok, son of Meraioth, son of Ahitub, chief administrator of the Temple of God,
Seraya mwana wa Hilikiya mwana wa Mesulamu, mwana wa Zadoki, mwana wa Merayoti, mwana wa Ahitubi amene anali woyangʼanira Nyumba ya Mulungu,
12 and their fellow priests who served at the Temple, a total of 822; Adaiah son of Jeroham, son of Pelaliah, son of Amzi, son of Zechariah, son of Pashhur, son of Malchijah,
ndi abale awo, amene ankagwira ntchito ku Nyumba ya Mulungu. Onse pamodzi anali 822. Panalinso Adaya mwana wa Yerohamu, mwana wa Pelaliya, mwana wa Amizi, mwana wa Zekariya, mwana wa Pasi-Huri, mwana wa Malikiya,
13 and those who worked with him, family leaders, a total of 242; and Amashsai, son of Azarel, son of Ahzai, son of Meshillemoth, son of Immer,
ndi abale ake, amene anali atsogoleri a mabanja. Onse pamodzi anali 242. Kuphatikiza apo panalinso Amasisai mwana wa Azaireli, mwana wa Ahazayi, mwana wa Mesilemoti, mwana wa Imeri
14 and those who worked with him, a total of 128 strong warriors. Zabdiel, son of Haggedolim, was in charge of them.
ndi abale ake. Onse pamodzi anali 128 ndipo anali anthu olimba mtima kwambiri. Mtsogoleri wawo wamkulu anali Zabidieli mwana wa Hagedolimu.
15 From the Levites: Shemaiah, son of Hasshub, son of Azrikam, son of Hashabiah, son of Bunni;
Alevi anali awa: Semaya mwana wa Hasubu, mwana wa Azirikamu, mwana wa Hasabiya, mwana wa Buni.
16 and Shabbethai and Jozabad, Levite leaders who were in charge of the outside work of God's Temple;
Sabetayi ndi Yozabadi anali atsogoleri amene ankayangʼanira ntchito ya kunja kwa Nyumba ya Mulungu.
17 Mattaniah, son of Mica, son of Zabdi, son of Asaph, who led out in giving thanks and praise; and Bakbukiah, who was second; and Abda, son of Shammua, son of Galal, son of Jeduthun.
Mataniya mwana wa Mika, mwana wa Zabidi, mwana wa Asafu ndiye anali wotsogolera pa mapemphero achiyamiko. Panalinso Bakibukiya amene anali wachiwiri pakati pa abale ake. Kuwonjezera apo panalinso Abida mwana wa Samuwa, mwana wa Galali, mwana wa Yedutuni.
18 The total number of priests in the holy city was 284.
Alevi onse amene anali mu mzinda woyera analipo 284.
19 The gatekeepers: Akkub, Talmon, and their fellow workers, who guarded the gates: a total of 172.
Alonda a ku Nyumba ya Mulungu anali awa: Akubu, Talimoni ndi abale awo. Onse pamodzi anali 172.
20 The other Israelites, with rest of the priests and Levites, lived in their home towns in Judah, each on their own property.
Aisraeli ena onse pamodzi ndi ansembe ndi Alevi ankakhala mʼmizinda ya Yuda, ndipo aliyense ankakhala mʼdera la makolo ake.
21 The Temple servants lived on the hill of Ophel. Ziha and Gishpa were in charge of them.
Koma antchito a ku Nyumba ya Mulungu ankakhala pa phiri la Ofeli, ndipo Ziha ndi Gisipa ndiwo anali kuwayangʼanira.
22 The one in charge of the Levites in Jerusalem was Uzzi, son of Bani, son of Hashabiah, son of Mattaniah, son of Mica, one of Asaph's descendants, the singers who led the service in God's Temple.
Wamkulu wa Alevi mu Yerusalemu anali Uzi mwana wa Bani, mwana wa Hasabiya, mwana wa Mataniya, mwana wa Mika. Uzi anali mmodzi wa zidzukulu za Asafu, amene anali oyimba nyimbo pa nthawi zachipembedzo mʼNyumba ya Mulungu.
23 They had specific orders from the king who had instructed them to perform a daily service.
Pakuti mfumu inalamula kuti tsiku ndi tsiku pa nthawi zachipembedzo oyimba nyimbowo azikhalapo.
24 Pethahiah, son of Meshezabel, a descendant of Zerah, son of Judah, was the king's advisor on all things relating to the Israelites.
Petahiya mwana wa Mesezabeli, mmodzi mwa zidzukulu za Zera mwana wa Yuda ndiye ankayimirira Aisraeli pa bwalo la mfumu ya Perisiya.
25 Regarding the villages with their nearby fields: some of the people of Judah lived in Kiriath-arba, Dibon, and Jekabzeel, and their smaller settlements;
Anthu ena a fuko la Yuda ankakhala ku Kiriyati-Ariba ndi midzi yake, ku Diboni ndi midzi yake, ku Yekabizeeli ndi midzi yake,
26 in Jeshua, Moladah, and Beth-pelet;
ku Yesuwa, Molada, Beti-Peleti,
27 in Hazar-shual, in Beersheba with its settlements,
Hazari-Suwali, Beeriseba ndi midzi yawo.
28 in Ziklag, in Mekonah and its settlements,
Ku Zikilagi, Mekona ndi midzi yawo,
29 in En-rimmon, in Zorah, in Jarmuth,
ku Eni-Rimoni, Zora, Yarimuti,
30 Zanoah, Adullam, and their villages, Lachish and its fields, and Azekah and its settlements. They lived all the way from Beersheba to the Valley of Hinnom.
Zanowa, Adulamu ndi midzi yake, ku Lakisi ndi minda yake, ku Beeriseba mpaka ku chigwa cha Hinomu.
31 The people of Benjamin from Geba lived in Michmash, Aija, and Bethel and its settlements,
Nazonso zidzukulu za Benjamini zinkakhala mʼdera lawo kuyambira ku Geba mpaka ku Mikimasi, Ayiya, Beteli ndi midzi yake,
32 in Anathoth, Nob, Ananiah,
ku Anatoti, Nobu ndi Ananiya,
33 Hazor, Ramah, Gittaim,
ku Hazori, Rama ndi Gitaimu,
34 Hadid, Zeboim, Neballat,
ku Hadidi, Zeboimu ndi Nebalati,
35 Lod, Ono, and in the Valley of Craftsmen.
ku Lodi, Ono ndi ku chigwa cha Amisiri.
36 Some divisions of the Levites of Judah also settled in Benjamin.
Magulu ena a Alevi a ku Yuda ankakhala ku Benjamini.

< Nehemiah 11 >