< Nehemiah 10 >

1 The document was sealed by: Nehemiah the governor, son of Hacaliah.
Amene anasindikiza chidindo anali awa: Nehemiya, bwanamkubwa uja, mwana wa Hakaliya. Zedekiya,
2 Zedekiah, Seraiah, Azariah, Jeremiah,
Seraya, Azariya, Yeremiya
3 Pashhur, Amariah, Malchijah,
Pasuri, Amariya, Malikiya,
4 Hattush, Shebaniah, Malluch,
Hatusi, Sebaniya, Maluki,
5 Harim, Meremoth, Obadiah,
Harimu, Meremoti, Obadiya,
6 Daniel, Ginnethon, Baruch,
Danieli, Ginetoni, Baruki,
7 Meshullam, Abijah, Mijamin,
Mesulamu, Abiya, Miyamini
8 Maaziah, Bilgai, and Shemaiah. These were the priests.
Maziya, Biligai ndi Semaya Awa anali ansembe.
9 The Levites: Jeshua, son of Azaniah, Binnui of the sons of Henadad, Kadmiel,
Alevi anali awa: Yesuwa mwana wa Azaniya, Binuyi wa fuko la Henadadi, Kadimieli,
10 and these other Levites: Shebaniah, Hodiah, Kelita, Pelaiah, Hanan,
ndi abale awo awa: Sebaniya, Hodiya, Kelita, Pelaya, Hanani,
11 Mica, Rehob, Hashabiah,
Mika, Rehobu, Hasabiya,
12 Zaccur, Sherebiah, Shebaniah,
Zakuri, Serebiya, Sebaniya,
13 Hodiah, Bani, and Beninu.
Hodiya, Bani ndi Beninu.
14 The leaders of the people: Parosh, Pahath-moab, Elam, Zattu, Bani,
Atsogoleri a anthu anali awa: Parosi, Pahati-Mowabu, Elamu, Zatu, Bani,
15 Bunni, Azgad, Bebai,
Buni, Azigadi, Bebai,
16 Adonijah, Bigvai, Adin,
Adoniya, Bigivai, Adini,
17 Ater, Hezekiah, Azzur,
Ateri, Hezekiya, Azuri,
18 Hodiah, Hashum, Bezai,
Hodiya, Hasumu, Bezayi
19 Hariph, Anathoth, Nebai,
Harifu, Anatoti, Nebayi,
20 Magpiash, Meshullam, Hezir,
Magipiyasi, Mesulamu, Heziri
21 Meshezabel, Zadok, Jaddua,
Mesezabeli, Zadoki, Yaduwa
22 Pelatiah, Hanan, Anaiah,
Pelatiya, Hanani, Ananiya,
23 Hoshea, Hananiah, Hasshub,
Hoseya, Hananiya, Hasubu
24 Hallohesh, Pilha, Shobek,
Halohesi, Piliha, Sobeki,
25 Rehum, Hashabnah, Maaseiah,
Rehumu, Hasabiya, Maaseya,
26 Ahiah, Hanan, Anan,
Ahiya, Hanani, Anani,
27 Malluch, Harim, and Baanah.
Maluki, Harimu ndi Baana.
28 The rest of the people, including the priests, Levites, gatekeepers, singers, and Temple servants, and everyone who had separated themselves from the people of the land to keep the Law of God, as well as their wives and all their sons and daughters who were old enough to understand,
Ife otsalafe, ndiye kuti ansembe, Alevi, alonda a ku Nyumba ya Mulungu, oyimba nyimbo, ogwira ntchito ku Nyumba ya Mulungu, onse amene anadzipatula pakati pa anthu a mitundu ina kuti atsate malamulo a Yehova, pamodzi ndi akazi athu, ana athu ndi onse amene ali ndi nzeru,
29 joined the leaders in swearing an oath to follow the Law of God given through Moses the servant of God, to pay attention to and carry out all the commands of the Lord our God, his rules and regulations.
tikuphatikana ndi abale athu wolemekezeka, ndipo tikulonjeza molumbira kuti tidzayenda motsata malamulo a Mulungu amene anapereka kudzera mwa Mose mtumiki wa Mulungu. Tilonjeza kumvera ndi kutsata bwino mawu onse, miyambo yonse ndi malangizo onse a Yehova. Yehova atilange ngati sitidzachita zimenezi.
30 “We promise not to allow our daughters to marry the people of the land, and not to allow our sons to marry their daughters.
“Ife tikulonjeza kuti sitidzapereka ana athu aakazi kuti akwatiwe ndi amuna a mayiko ena kapena kutenga ana awo aakazi kuti akwatiwe ndi ana athu aamuna.
31 When the people of the land bring goods and all kinds of food to sell on the holy Sabbath, we will not buy anything from them on the Sabbath or on other holy days. Every seventh year we will leave the land to rest, and we will cancel all debts.
“Ngati anthu a mitundu ina abwera ndi zinthu za malonda, monga tirigu, kudzagulitsa pa tsiku la Sabata, sitidzawagula pa tsiku la Sabata kapena pa tsiku lina lililonse loyera. Pa chaka chilichonse cha chisanu ndi chiwiri tidzagoneka munda wosawulima ndipo tidzafafaniza ngongole zonse.
32 We accept the obligation to pay one third of a shekel for the operation of the Temple of God,
“Tikulonjezanso molumbira kuti chaka ndi chaka tizipereka magalamu anayi a siliva kuti zithandize ntchito ya ku Nyumba ya Mulungu wathu.
33 for the showbread, for the regular grain offerings and burnt offerings, for the Sabbath offerings, for the new moon and yearly festivals, for the holy offerings, for the sin offerings to make atonement for Israel, in short all that takes place in the Temple of our God.
Ndalamayi izithandiza kulipirira buledi wa pa tebulo, chopereka cha chakudya cha nthawi zonse, zopereka zopsereza za nthawi zonse, zopereka za pa tsiku la Sabata, za pachikondwerero cha Mwezi Watsopano, za pa masiku a chikondwerero osankhika, zopereka za zinthu zopatulika, zopereka za nsembe yopepesera machimo a Aisraeli ndi ntchito ina iliyonse ya ku Nyumba ya Mulungu.
34 We have allocated by lot among the priests, Levites, and the people, to determine who will bring wood to the Temple of our God to burn on the altar of the Lord our God at specific times during the year, as required by the Law.
“Ife ansembe, Alevi ndi anthu onse, tachita maere kuti tidziwe pamene banja lathu lililonse lidzabweretsa ku nyumba ya Mulungu wathu pa nthawi yoyikika ya chaka zopereka za nkhuni zoyaka pa guwa lansembe la Yehova Mulungu wathu, monga momwe zinalembedwera mʼMalamulo.”
35 We also promise to bring the first part of the produce from our fields and from every fruit tree to the Lord's Temple every year.
“Tilonjezanso kuti tidzabwera ndi zipatso zoyamba kucha za mʼminda yathu ndi zipatso zoyamba kucha za mtengo uliwonse wa zipatso chaka ndi chaka kuti tidzapereke ku Nyumba ya Mulungu wathu.”
36 We will bring the firstborn of our sons and of our livestock and of our herds and flocks to the Temple of our God, to the priests who minister there, as required by the Law.
“Tidzabweranso nawo ku Nyumba ya Mulungu, kwa ansembe amene amatumikira ku Nyumba ya Mulungu ana athu aamuna oyamba kubadwa ndi ana angʼombe oyamba kubadwa monga zalembedwera mu Malamulo. Tidzaperekanso ana oyamba kubadwa a ziweto zathu ndi ana ankhosa oyamba kubadwa.”
37 We will bring to the storerooms of the Temple of our God, to the priests, the first part of our coarse-ground flour, of our grain offerings, of the fruit of all our trees, and of our new wine and olive oil. We will also bring a tithe of our produce to the Levites, for the Levites are the ones who collect the tithes in all the farming towns.
“Ndiponso ku zipinda za Nyumba ya Mulungu wathu, kwa ansembe tidzaperekanso mtanda wathu wa buledi wa ufa ndi mphatso zina monga zipatso za mtengo uliwonse, vinyo ndi mafuta. Tidzaperekanso kwa alevi chakhumi cha mbewu zathu pakuti alevi ndiwo amasonkhanitsa chakhumi mʼmidzi yathu yonse.
38 A priest descended from Aaron will accompany the Levites when they collect the tithe, and the Levites are to bring a tithe of these tithes to the rooms of the storehouse in the Temple of our God.
Wansembe, mdzukulu wa Aaroni azikhala pamodzi ndi Alevi pamene akulandira chakhumi. Ndipo Alevi azibwera ndi chakhumicho ku nyumba ya Mulungu wathu, kuzipinda zosungiramo chuma.”
39 The people of Israel and the Levites are to bring the offerings of grain, new wine, and olive oil to the storerooms where the sanctuary objects are kept, where the ministering priests, the gatekeepers, and the singers are. We will not forget the Temple of our God.”
Choncho Israeli, kuphatikiza zidzukulu za Alevi, azipititsa zopereka za tirigu, vinyo ndi mafuta ku zipinda zosungiramo katundu wopatulika, komanso kokhala ansembe amene akutumikira pamodzi ndi alonda a ku Nyumba ya Mulungu ndi anthu oyimba nyimbo. “Kwambiri ife sitidzaleka kusamala Nyumba ya Mulungu.”

< Nehemiah 10 >