< Leviticus 8 >
Yehova anawuza Mose kuti,
2 “Go with Aaron and his sons, and take their priestly clothes, anointing oil, the bull of the sin offering, two rams, and the basket of bread made without yeast,
“Tenga Aaroni ndi ana ake, zovala zawo, mafuta wodzozera, ngʼombe yayimuna kuti ikhale nsembe yopepesera machimo, nkhosa ziwiri zazimuna ndi dengu la buledi wopanda yisiti,
3 and have everyone assemble at the entrance to the Tent of Meeting.”
ndipo usonkhanitse gulu la anthu pa khomo la tenti ya msonkhano.”
4 Moses did as the Lord instructed him, and everyone gathered at the entrance to the Tent of Meeting.
Mose anachita zomwe Yehova anamulamula ndipo gulu la anthu linasonkhana pa khomo la tenti ya msonkhano.
5 Moses told them, “The following is what the Lord has ordered to be done.”
Mose anawuza gulu la anthuwo kuti, “Izi ndi zimene Yehova walamulira kuti zichitike.”
6 Moses had Aaron and his sons come forward, and he washed them with water.
Pamenepo Mose anabwera ndi Aaroni ndi ana ake nawasambitsa ndi madzi.
7 He dressed Aaron with the tunic, tied the sash around him, put the robe on him and then the ephod. He tied the waistband of the ephod around him, fastening it to him.
Anamuveka Aaroni mwinjiro, ndi kumumanga lamba mʼchiwuno. Anamuvekanso mkanjo wa efodi ndi efodiyo. Anamangira lamba efodiyo amene analukidwa mwaluso uja, motero efodiyo analimba mʼchiwunomo.
8 Then Moses attached the breastpiece to Aaron and put the Urim and Thummim in the breastpiece.
Anamuvekanso chovala chapachifuwa ndipo mʼchovalacho anayikamo Urimu ndi Tumimu.
9 He put the turban on Aaron's head and placed the gold plate, the holy crown, on the front of the turban, as the Lord had instructed him to do.
Kenaka anamuveka Aaroniyo nduwira kumutu ndipo patsogolo pa nduwirayo anayikapo duwa lagolide, chizindikiro chopatulika monga momwe Yehova analamulira Mose.
10 Then Moses took the anointing oil and anointed the Tabernacle and everything in it to dedicate it all.
Pamenepo Mose anatenga mafuta wodzozera nadzoza tenti ya msonkhano pamodzi ndi zonse zimene zinali mʼmenemo, ndipo potero anazipatula.
11 He sprinkled some of the oil on the altar seven times to anoint it and all its utensils, as well as the basin with its stand to dedicate them.
Anawaza mafuta ena pa guwa kasanu ndi kawiri, nalidzoza guwalo pamodzi ndi ziwiya zake zonse. Anadzozanso beseni ndi tsinde lake, nazipatula.
12 Moses poured some of the anointing oil on Aaron's head to anoint him and to dedicate him.
Anathira mafuta wodzozera ena pamutu pa Aaroni ndipo anamudzoza ndi kumupatula.
13 Then Moses had Aaron's sons come forward, dressed them tunics in them, tied sashes around them, and wrapped headbands on them, as the Lord had ordered him to do.
Kenaka anabwera ndi ana a Aaroni. Anawaveka minjiro, ndi kuwamanga malamba mʼchiwuno ndi kuwaveka nduwira kumutu monga momwe Yehova analamulira Mose.
14 Moses brought the bull over for the sin offering, and Aaron and his sons put their hands on its head.
Kenaka Mose anabwera ndi ngʼombe yayimuna ya nsembe yopepesera machimo, ndipo Aaroni ndi ana ake anasanjika manja awo pamutu pa ngʼombeyo.
15 Moses killed the bull and took some of the blood. He used his finger to put the blood on all four horns of the altar to dedicate it and purify it. He poured out the rest of the blood at the bottom of the altar, and consecrated the altar so that it could be used to make people right.
Mose anapha ngʼombeyo, ndi kutenga magazi ena angʼombeyo ndi kupaka ndi chala chake pa nyanga zaguwa lansembe, naliyeretsa. Magazi otsalawo anawakhuthulira pa tsinde laguwalo. Motero anachita mwambo wopepesera machimo.
16 Moses took all the fat that covers the insides, the best part of the liver, both kidneys with the fat on them, burned all of it on the altar.
Mose anatenganso mafuta onse okuta matumbo, mafuta ophimba chiwindi, ndiponso impsyo zonse ziwiri pamodzi ndi mafuta ake, nazitentha pa guwapo.
17 But the rest of the bull—the skin, the meat, and the waste he burned outside the camp, as the Lord had ordered him to do.
Koma nyama yangʼombeyo, chikopa chake ndi matumbo ake anaziwotcha kunja kwa msasa monga momwe Yehova analamulira Mose.
18 Moses brought the ram for the burnt offering, and Aaron and his sons put their hands on its head.
Kenaka anabwera ndi nkhosa yayimuna ya nsembe yopsereza, ndipo Aaroni ndi ana ake aamuna anasanjika manja awo pamutu pake.
19 Moses killed the ram and sprinkled the blood on all sides of the altar.
Ndipo Mose anapha nkhosayo ndi kuwaza magazi ake mbali zonse zaguwalo.
20 He divided the ram into pieces and burned the head, the pieces, and the fat.
Anayidula nkhosayo nthulinthuli ndipo anatentha mutu wake, nthulizo ndi mafuta.
21 He washed the insides and legs with water and burned the whole ram on the altar as a burnt offering, a food offering to be accepted by the Lord, as the Lord had ordered Moses to do.
Anatsuka matumbo ake ndi miyendo yake, ndi kutentha nkhosa yonseyo pa guwa lansembe kuti ikhale nsembe yopsereza, fungo lokoma, nsembe yachakudya yoperekedwa kwa Yehova monga Yehovayo analamulira Mose.
22 Moses brought the second ram, the ram of ordination, and Aaron and his sons put their hands on its head.
Kenaka Mose anapereka nkhosa yayimuna ina pamwambo wodzoza ansembe, ndipo Aaroni ndi ana ake aamuna anasanjika manja awo pamutu pake.
23 Moses killed the ram and took some of its blood. He put it on Aaron's right earlobe, on the thumb of his right hand, and on the big toe of his right foot.
Mose anayipha nkhosayo ndipo anatenga magazi ake ena ndi kupaka ndewere za khutu la kudzanja lamanja la Aaroni, pa chala chake chachikulu cha kudzanja lamanja, ndi pa chala chake chachikulu cha phazi lakumanja.
24 Then Moses had Aaron and his sons come forward and put some of the blood on their right earlobes, on the thumbs of their right hands, and on the big toes of their right feet. Then he sprinkled blood on all sides of the altar.
Pambuyo pake Mose anabwera ndi ana aamuna a Aaroni ndi kupaka magazi pa ndewere za makutu awo akumanja, pa zala zawo zazikulu za dzanja lamanja, ndiponso pa zala zawo zazikulu za kuphazi lakumanja. Kenaka iye anawaza magazi otsalawo mbali zonse za guwalo.
25 Moses took the fat, including the fat tail, all the fat on the insides, the best part of the liver, both kidneys with the fat on them Moses took the fat—together with the right thigh.
Anatenganso mafuta ake, mafuta a ku mchira wake, mafuta okuta matumbo, mafuta okuta chiwindi, impsyo zonse ziwiri ndi mafuta ake ndiponso ntchafu yakumanja.
26 He took one loaf of bread without yeast, one loaf made with olive oil, and one wafer from the basket of bread without yeast that was in the presence of the Lord. He placed them on top of the portions of fat and on the right thigh.
Ndipo mʼdengu la buledi wopanda yisiti limene linali pamaso pa Yehova, anatengamo buledi mmodzi, buledi mmodzi wokhala ndi mafuta a olivi, ndi buledi wopyapyala mmodzi. Zonsezi anaziyika pa mafuta aja ndi pa ntchafu ya ku dzanja lamanja ija.
27 Then he gave them to Aaron and his sons, and waved them before the Lord as a wave offering.
Mose anapereka zonsezi mʼmanja mwa Aaroni ndi ana ake amene anazipereka kwa Yehova kuti zikhale nsembe yoweyula.
28 After this Moses took them back and burned them on the altar with the burnt offering. This was an ordination offering, a food offering to be accepted by the Lord.
Kenaka Mose anazitenga mʼmanja mwawo ndipo anazipsereza pa guwa lansembe pamwamba penipeni pamodzi ndi nsembe yopsereza ija kuti ikhale nsembe yopereka pamwambo wodzoza ansembe, kuti ipereke fungo lokoma, chopereka chachakudya kwa Yehova.
29 Moses then took the breast, his share of the ordination ram, and waved it before the Lord as a wave offering, as the Lord had ordered him to do.
Mose anatenga chidale cha nkhosa yayimuna, chomwe ndi gawo lake pamwambo wodzoza ansembe, ndipo anachiweyula pamaso pa Yehova kuti chikhale nsembe yoweyula monga momwe Yehova analamulira Mose.
30 Moses then took some of the anointing oil and some of the blood from the altar. He sprinkled both of them on the clothes of Aaron and his sons. This is how he dedicated he dedicated the clothes of Aaron and his sons.
Kenaka Mose anatenga mafuta wodzozera ansembe ndi magazi amene anali pa guwa nawaza pa Aaroni ndi zovala zake ndiponso ana ake aja ndi zovala zawo. Motero Mose anapatula Aaroni ndi zovala zake, ndiponso ana ake ndi zovala zawo.
31 Moses told Aaron and his sons, “You are to boil the meat at the entrance to the Tent of Meeting, and then eat it there with the bread that is in the basket of offerings for the ordination, as I ordered: ‘It is for Aaron and his sons to eat.’
Mose anawuza Aaroni ndi ana ake kuti, “Phikani nyamayo pa khomo la tenti ya msonkhano, ndipo mudyere pomwepo pamodzi ndi buledi amene ali mʼdengu la zopereka za pamwambo wodzoza ansembe monga Yehova analamulira kuti, ‘Aaroni ndi ana ake azidya zimenezi.’
32 Afterwards you must burn what's left over of the meat and bread.
Ndipo nyama ndi buledi zotsalazo, muziwotche.
33 You are not to leave the entrance to the Tent of Meeting for seven days until the ordination ceremony is completed, because your ordination will take seven days.
Musatuluke kunja kwa tenti ya msonkhano kwa masiku asanu ndi awiri mpaka masiku amwambo wokudzozani unsembe atatha, pakuti mwambowu ndi wa masiku asanu ndi awiri.
34 What was done today was ordered by the Lord as a means of making you right.
Zimene zachitika lerozi analamula ndi Yehova kuti zichitike ngati nsembe yopepesera machimo anu.
35 You must stay at the entrance to the Tent of Meeting for seven days, day and night, and follow the Lord's commands so that you will not die, for this is what I have been ordered to do.”
Muzikhala pa khomo la tenti ya msonkhano usana ndi usiku kwa masiku asanu ndi awiri. Ndipo muzichita zimene Yehova wakulamulani kuti musafe, pakuti zimenezi ndi zomwe Yehova wandilamulira.”
36 Aaron and his sons did everything that the Lord had ordered through Moses.
Choncho Aaroni ndi ana ake anachita zonse zimene Yehova analamula kudzera mwa Mose.