< Leviticus 24 >
Yehova anawuza Mose kuti,
2 “Order the Israelites to bring you pure, pressed olive oil for the lamps, so they will always stay lit.
“Lamula Aisraeli kuti akupatse mafuta anyale, a olivi wabwino kwambiri kuti nyalezo ziziyaka nthawi zonse.
3 From evening until morning Aaron is to constantly look after the lamps continually before the Lord, outside the veil of the Testimony in the Tent of Meeting. This regulation is for all time and for all future generations.
Kunja kwa nsalu yotchinga Bokosi la Chipangano, mʼchihema cha msonkhano, Aaroni azionetsetsa kuti nyale ikukhala chiyakire pamaso pa Yehova kuyambira madzulo mpaka mmawa, nthawi zonse. Limeneli ndi lamulo lamuyaya pa mibado yonse.
4 He is to constantly look after the lamps placed on the pure gold lampstand before the Lord.
Aaroni ayatse nyale zimene zili pa choyikapo nyale chagolide wabwino kwambiri kuti zikhale zoyaka nthawi zonse pamaso pa Yehova.
5 Using the best flour bake twelve loaves, with two-tenths of an ephah of flour per loaf.
“Mutenge ufa wosalala ndipo muphike makeke khumi ndi awiri ndipo keke iliyonse ikhale ya ufa wa makilogalamu awiri.
6 Place them in two piles, six in each pile, on the table made of pure gold that stands before the Lord.
Muwayike pa tebulo la golide wabwino kwambiri pamaso pa Yehova mʼmizere iwiri. Mzere uliwonse ukhale wa makeke asanu ndi imodzi.
7 Place pure frankincense beside each pile to go with the bread to act as the ‘reminder part,’ a food offering to the Lord.
Pa mzere uliwonse muyikepo lubani wafungo lokoma kuti pamodzi ndi bulediyo akhale wachikumbutso cha nsembe yopsereza yopereka kwa Yehova.
8 Every Sabbath day the bread shall be placed before the Lord, given by the Israelites as an ongoing sign of the eternal agreement.
Sabata ndi sabata nthawi zonse Aaroni aziyika makeke amenewa pamaso pa Yehova mʼmalo mwa Aisraeli onse kuti akhale pangano lamuyaya.
9 It is for Aaron and his descendants. They are to eat it in a holy place; for they must treat it as a most holy part of the food offerings given to the Lord. It is their share of the food offerings for all time.”
Chakudyacho ndi cha Aaroni ndi ana ake ndipo azidyera ku malo wopatulika chifukwa kwa iye chakudyacho ndi chopatulika kwambiri chochokera pa chopereka chopsereza cha Yehova.”
10 One day a man who had an Israelite mother and an Egyptian father went into the Israelite camp and had a fight with an Israelite.
Tsiku lina munthu wina wamwamuna amene amayi ake anali Mwisraeli koma abambo ake anali Mwigupto anapita kwa Aisraeli ndipo anakangana ndi Mwisraeli wina ku msasa.
11 The Israelite woman's son cursed the name of the Lord. So they took him before Moses. (His mother's name was Shelomith, daughter of Dibri, from the tribe of Dan.)
Munthu uja ananyoza dzina la Yehova ndi kulitemberera. Choncho anabwera naye kwa Mose. Dzina la amayi ake linali Selomiti, mwana wa Dibiri, wa fuko la Dani.
12 They detained him until it was clear what the Lord wanted them to do about it.
Anamuyika mʼndende mpaka atadziwa bwino chofuna cha Yehova.
Ndipo Yehova anawuza Mose kuti,
14 “Take the man who cursed me outside the camp. Have all who heard him curse put their hands on his head; then have everyone stone him to death.
“Pita naye kunja kwa msasa munthu wotembererayo. Onse amene anamumva akutemberera asanjike manja awo pamutu pake ndipo gulu lonse la anthu limugende miyala.
15 Tell the Israelites that anyone who curses their God will be punished for their sin.
Choncho uza Aisraeli kuti, ‘Aliyense wotemberera Mulungu wake alangidwe.
16 Anyone who curses the name of the Lord must to be executed. All of you must stone them to death, whether they are a foreigner who lives with you or an Israelite. If they curse my name, they must be executed.
Aliyense wonyoza dzina la Yehova, mlendo ngakhale mbadwa, aphedwe. Gulu lonse la anthu limuponye miyala.
17 Anyone who kills someone else must be executed.
“‘Ngati munthu wina aliyense achotsa moyo wa munthu mnzake, munthuyo ayenera kuphedwa.
18 Anyone who kills an animal has to replace it—a life for a life.
Aliyense wopha chiweto cha mnzake ayenera kulipira china. Moyo kulipa moyo.
19 If anyone injures someone else, whatever they've done must be done to them:
Ngati munthu avulaza mnzake, nayenso amuchite zomwe wachitira mnzakeyo:
20 a broken bone for a broken bone, an eye for an eye, a tooth for a tooth. Whatever way they injured the victim, the same must be done to them.
kuthyola fupa kulipira kuthyola fupa, diso kulipira diso, dzino kulipira dzino. Monga momwe anavulazira mnzake, amuvulaze chimodzimodzinso.
21 Anyone who kills an animal has to replace it, but anyone who kills someone else must be executed.
Aliyense wopha chiweto cha mnzake, alipire chiweto china, koma aliyense wopha munthu ayenera kuphedwa.
22 The same laws apply to foreigners who live with you as to Israelites, for I am the Lord your God.”
Lamulo la mlendo ndi mbadwa ndi limodzi lomweli. Ine ndine Yehova Mulungu wanu.’”
23 Moses told this to the Israelites, and they took the man who cursed the Lord outside the camp and stoned him to death. The Israelites did what the Lord ordered Moses to do.
Pamenepo Mose anawuza Aisraeli zimenezi, ndipo iwo anatulutsira munthu wotembererayo kunja kwa msasa ndi kumugenda miyala. Aisraeli anachita zimene Yehova analamula Mose.