< Leviticus 23 >
Yehova anawuza Mose kuti,
2 “Tell the Israelites that these are my religious festivals, the festivals of the Lord that you are to call as the holy times when we meet together.
“Yankhula ndi Aisraeli ndipo uwawuze kuti, ‘Awa ndi masiku anga osankhika a chikondwerero, masiku osankhika olemekeza Yehova amene uyenera kulengeza kuti akhale masiku opatulika a misonkhano.
3 You have six days to work, but the seventh day is a Sabbath of complete rest, a holy day of meeting together. Don't do any work. It is the Lord's Sabbath everywhere you live.
“‘Pa masiku asanu ndi limodzi muzigwira ntchito, koma tsiku lachisanu ndi chiwiri ndi Sabata lopuma, tsiku la msonkhano wopatulika. Kulikonse kumene inu mukukhala musamagwire ntchito iliyonse tsiku limeneli popeza ndi tsiku la Sabata la Yehova.
4 These are the Lord's religious festivals, the holy meetings that you ate to announce at their specific times.
“‘Awa ndiwo masiku osankhidwa a zikondwerero za Yehova, masiku woyera a misonkhano amene muti mudzalengeze pa nthawi yake:
5 The Lord's Passover starts on the evening of the fourteenth day of the first month.
Chikondwerero cha Paska chiziyamba madzulo a tsiku la 14 la mwezi woyamba.
6 The Lord's Festival of Unleavened Bread begins on the fifteenth day of the first month. For seven days the bread you eat must be made without yeast.
Tsiku la 15 la mwezi womwewo ndi tsiku lolemekeza Yehova ndipo muziyamba Chikondwerero cha Buledi Wopanda Yisiti. Muzidya buledi wopanda yisiti kwa masiku asanu ndi awiri.
7 On the first day you are hold a holy meeting. You must not do any of your usual work.
Pa tsiku loyamba muzichita msonkhano wopatulika. Musamagwire ntchito iliyonse.
8 For seven days you shall present food offerings to the Lord. There is to be a holy meeting on the seventh day. You must not do any of your usual work.”
Pa masiku asanu ndi awiri muzipereka nsembe yopsereza kwa Yehova. Ndipo tsiku lachisanu ndi chiwiri muzikhala ndi msonkhano wopatulika ndipo musamagwire ntchito yolemetsa.’”
Yehova anawuza Mose kuti,
10 “Tell the Israelites that when you enter the land that I'm giving you and you harvest your crops, take a stack of grain from the firstfruits of your harvest to the priest.
“Yankhula ndi Aisraeli ndipo uwawuze kuti, ‘Mukakalowa mʼdziko limene ndikukupatsanilo ndi kukolola za mʼminda mwanu, mudzabwere kwa wansembe ndi mtolo wa tirigu woyambirira kucha wa mʼminda mwanu.
11 He will wave the stack of grain before the Lord so that it may be accepted on your behalf. The priest is to do this the day following the Sabbath.
Wansembeyo auweyule mtolowo pamaso pa Yehova kotero mtolowo udzalandiridwa mʼmalo mwanu. Wansembe auweyule tsiku lotsatana ndi la Sabata.
12 When you wave the stack of grain, you are to present a one-year-old lamb without defects as a burnt offering to the Lord,
Pa tsiku limene muweyula mtolowo, muperekenso mwana wankhosa wa mwamuna wa chaka chimodzi, wopanda chilema kuti akhale nsembe yopsereza ya kwa Yehova.
13 together with its grain offering of two-tenths of an ephah of best flour mixed with olive oil (a food offering to the Lord to be accepted by him) and its drink offering of a quarter of a hin of wine.
Chopereka chachakudya chake chikhale cha makilogalamu awiri a ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta kuti chikhale nsembe yopsereza yopereka kwa Yehova, ya fungo lokoma. Ndipo chopereka cha chakumwa chake chikhale vinyo wa malita anayi ndi theka.
14 Don't eat any bread, roasted grain, or new grain until the time you bring this offering to your God. This regulation is for all time and for future generations everywhere you live.
Musadye buledi aliyense kapena tirigu wokazinga, kapena wamuwisi mpaka tsiku limene mwabwera ndi chopereka ichi kwa Mulungu wanu. Limeneli ndi lamulo lamuyaya pa mibado yanu yonse, kulikonse kumene mukakhale.
15 Count seven full weeks from the day after the Sabbath—the day you brought the stack of grain as a wave offering.
“‘Kuyambira tsiku lotsatana ndi la Sabata lija, tsiku limene munabwera ndi mtolo wa nsembe yoweyula, muziwerenga masabata asanu ndi awiri athunthu.
16 Count fifty days until the day after the seventh Sabbath, and on that day present an offering of new grain to the Lord.
Ndiye kuti muwerenge masiku makumi asanu kuchokera pa tsiku lotsatana ndi Sabata la chisanu ndi chiwiri, ndipo kenaka mupereke nsembe ya tirigu watsopano kwa Yehova.
17 Bring two loaves of bread from your homes as a wave offering. Make them from two-tenths of an ephah of best flour, baked with yeast, as the firstfruits to the Lord.
Kuchokera kulikonse kumene mukukhala, mubwere pamaso pa Yehova ndi buledi muwiri wa ufa wosalala wa makilogalamu awiri, ophikidwa ndi yisiti kuti akhale nsembe yoweyula ya zakudya zoyamba kucha.
18 As well as the bread, present seven one-year-old male lambs a year old without defects, one young bull, and two rams. They will be a burnt offering to the Lord, as well as their grain offerings and drink offerings, a food offering to the Lord to be accepted by him.
Pamodzi ndi bulediyu muperekenso ana ankhosa aamuna asanu ndi awiri, aliyense akhale wa chaka chimodzi ndi wopanda chilema. Pakhalenso ngʼombe yayingʼono yayimuna ndi nkhosa zazimuna ziwiri. Zimenezi zidzakhala nsembe zopsereza zopereka kwa Yehova pamodzi ndi nsembe za zakudya ndi nsembe za zakumwa. Zonsezi zikhale nsembe zopsereza za fungo lokomera Yehova.
19 Present one male goat as a sin offering and two one-year-old male lambs a year old as a peace offering.
Kenaka mupereke mbuzi imodzi yayimuna kuti ikhale nsembe yopepesera machimo ndiponso ana ankhosa awiri, aliyense wa chaka chimodzi kuti akhale nsembe yachiyanjano.
20 The priest will wave the lambs as a wave offering before the Lord, along with the bread of the firstfruits. The bread and the two lambs are holy to the Lord and belong to the priest.
Wansembe aweyule ana ankhosa awiriwo pamaso pa Yehova monga nsembe yoweyula, pamodzi ndi buledi wa tirigu woyambirira kucha. Zimenezi ndi zopereka zopatulika za Yehova zopatsidwa kwa ansembe.
21 That same day you are to announce a holy meeting, and you must not to do any of your usual work. This regulation is for all time and for future generations everywhere you live.
Pa tsiku lomwelo mulengeze za msonkhano wopatulika ndipo musagwire ntchito zolemetsa. Limeneli ndi lamulo lamuyaya pa mibado yanu yonse, kulikonse kumene mukakhale.
22 When you harvest the crops grown on your land, don't harvest right up to the edges of your field, or collect what has been missed. Leave them for the poor people and foreigners. I am the Lord your God.”
“‘Pamene mukukolola zinthu mʼmunda mwanu, musakolole munda wanu mpaka mʼmalire mwenimweni, ndipo musatole khunkha lake. Zimenezo musiyire anthu osauka ndi alendo. Ine ndine Yehova Mulungu wanu.’”
Yehova anawuza Mose kuti,
24 “Tell the Israelites that on the first day of the seventh month you are to have a special Sabbath of complete rest, a holy meeting that is announced by the sound of trumpets.
“Uza Aisraeli kuti, ‘Tsiku loyamba la mwezi wachisanu ndi chiwiri, likhale tsiku lopumula, la msonkhano wopatulika, mulilengeze poyimba lipenga.
25 Don't do any of your usual work; instead you are to present a food offering to the Lord.”
Musagwire ntchito zolemetsa koma mupereke nsembe yopsereza kwa Yehova.’”
Yehova anawuza Mose kuti,
27 “The Day of Atonement is on the tenth day of this seventh month. You are to have a holy meeting, deny yourselves, and present a food offering to the Lord
“Tsiku lakhumi la mwezi wachisanu ndi chiwiri ndi tsiku lochita Mwambo Wopepesera Machimo. Muzichita msonkhano wopatulika. Muzidzichepetsa pamaso pa Yehova ndi kupereka nsembe zopsereza kwa Yehova.
28 On this day you must not do any of your usual work because it is the Day of Atonement, when things are made right for you before the Lord your God.
Tsiku limeneli musamagwire ntchito chifukwa ndi tsiku la Mwambo Wopepesera Machimo, kupepesera machimo anu pamaso pa Yehova Mulungu wanu.
29 Anyone who does not practice self-denial on this day must be expelled from their people.
Munthu aliyense amene sasala zakudya pa tsiku limeneli ayenera kuchotsedwa pakati pa anthu a mtundu wake.
30 I will destroy anyone of you who does any work on this day.
Aliyense wogwira ntchito tsiku limeneli ndidzamuwononga pakati pa anthu a mtundu wake.
31 Don't do any kind of work at all. This regulation is for all time and for future generations everywhere you live.
Inu musadzagwire ntchito iliyonse. Limeneli ndi lamulo lamuyaya pa mibado yanu yonse, kulikonse kumene mukakhale.
32 It is to be a Sabbath of complete rest for you, and you shall practice self-denial. You are to observe your Sabbath from the evening of the ninth day of the month until evening the next day.”
Limeneli kwa inu ndi tsiku la Sabata lopumula, ndipo muyenera kusala zakudya. Kuyambira madzulo a tsiku lachisanu ndi chinayi la mwezi mpaka madzulo ena otsatirawo muzisunga tsikulo ngati Sabata lanu.”
Yehova anawuza Mose kuti,
34 “Tell the Israelites that the Feast of Tabernacles to honor the Lord begins on the fifteenth day of the seventh month and lasts for seven days.
“Uwawuze Aisraeli kuti pa masiku asanu ndi awiri kuyambira pa tsiku la 15 la mwezi wachisanu ndi chiwiri pazikhala Chikondwerero cha Misasa cholemekeza Yehova.
35 On the first day have a holy meeting. You must not do any of your usual work.
Tsiku loyamba ndi la msonkhano wopatulika, musagwire ntchito zolemetsa.
36 For seven days you shall present food offerings to the Lord. On the eighth day you are to have another holy meeting and present a food offering to the Lord. It is a meeting for worship. You must not do any of your usual work.
Pa masiku asanu ndi awiri muzipereka nsembe zopsereza kwa Yehova. Ndipo pa tsiku lachisanu ndi chitatu muzikhala ndi msonkhano wopatulika ndipo muzipereka nsembe yopsereza kwa Yehova. Kumeneku ndi kutsekera kwa msonkhano waukulu. Musagwire ntchito zolemetsa.
37 (These are the Lord's holy festivals, which you are to announce as holy meetings for presenting food offerings to the Lord. These include burnt offerings, grain offerings, sacrifices and drink offerings, each according to the specific day.
(“‘Amenewa ndi masiku osankhika a chikondwerero cha Yehova, amene muziwalengeza kuti ndi nthawi ya msonkhano wopatulika. Masiku amenewa muzipereka nsembe zopsereza, nsembe za chakudya, nsembe zanyama ndi zopereka zachakumwa za tsiku ndi tsiku.
38 All of these offerings are in addition to those for the Lord's Sabbaths. They are also in addition to your gifts, to all your offerings to fulfill promises, and to all the freewill offerings you present to the Lord.)
Zopereka zimenezi ndi zowonjezera pa zopereka za Yehova za pa Sabata, zopereka zanu zolumbira ndiponso mphatso zanu zaufulu zopereka kwa Yehova.)
39 You shall celebrate a feast to honor the Lord for seven days on the fifteenth day of the seventh month, once you have harvested your crops. The first day and the eighth day are Sabbaths of complete rest.
“‘Choncho kuyambira pa tsiku la 15 la mwezi wachisanu ndi chiwiri, mutakolola zinthu mʼmunda mwanu, muchite chikondwerero cha Yehova kwa masiku asanu ndi awiri. Tsiku loyamba ndi tsiku lopumula, ndipo tsiku lachisanu ndi chitatu ndi lopumulanso.
40 On the first day you are to gather branches from large trees, from palm trees, from leafy trees and of river willows, and celebrate before the Lord your God for seven days.
Pa tsiku loyamba muzitenga zipatso zabwino kwambiri zothyola mʼmitengo, nthambi za kanjedza, nthambi zazikulu za mitengo ya masamba ambiri, ndi za misondozi yakumtsinje, ndipo muzikondwera pamaso pa Yehova Mulungu wanu kwa masiku asanu ndi awiri.
41 You are to hold this festival to honor the Lord for seven days every year. This regulation is for all time and for all future generations.
Chaka chilichonse muzichita chikondwerero cha Yehova kwa masiku asanu ndi awiri. Limeneli ndi lamulo lamuyaya pa mibado yanu yonse. Muzichita chikondwerero chimenechi mwezi wachisanu ndi chiwiri.
42 You are to live in temporary shelters for seven days. Every Israelite born in the country must live in shelters,
Muzikhala mʼmisasa masiku asanu ndi awiri. Onse amene ali mbadwa mʼdziko la Israeli azikhala mʼmisasa
43 so that your descendants will remember that I made the Israelites live in shelters when I led them out of Egypt. I am the Lord your God.”
kuti zidzukulu zanu zidzadziwe kuti ndine amene ndinakhazika Aisraeli mʼmisasa nditawatulutsa ku Igupto. Ine ndine Yehova Mulungu wanu.’”
44 So Moses told the Israelites all about the Lord's festivals.
Choncho Mose analengeza kwa Aisraeli masiku osankhika a zikondwerero za Yehova.