< Joshua 21 >
1 The leaders of the tribe of Levi approached Eleazar the priest, Joshua the son of Nun, and the leaders of the Israelite tribes.
Tsono atsogoleri a mabanja a fuko la Levi anabwera kwa wansembe Eliezara, Yoswa mwana wa Nuni, ndi kwa atsogoleri a mabanja a mafuko onse a Aisraeli,
2 They spoke to them at Shiloh in Canaan, saying, “The Lord gave instructions through Moses to give us towns to live in, and pastures for our flocks.”
ku Silo mʼdziko la Kanaani ndipo anati, “Yehova analamula kudzera mwa Mose kuti atipatse mizinda kuti tikhalemo, pamodzi ndi malo odyetseramo ziweto zathu.”
3 So, following the Lord's instructions, the Israelites gave towns and pastures to the Levites from their own allocations.
Choncho, Aisraeli anapereka kwa fuko la Levi mizinda iyi pamodzi ndi malo owetera ziweto zawo kuchokera ku madera awo, monga Yehova analamulira:
4 The lot was cast for the families of the Kothaites. These Levites, descendants of Aaron, were allotted thirteen towns from the tribes of Judah, Simeon, and Benjamin.
Maere oyamba anagwera mabanja a Kohati, Alevi amene anali zidzukulu za wansembe Aaroni anapatsidwa mizinda 13 kuchokera ku mafuko a Yuda, Simeoni ndi Benjamini.
5 The remaining families of the descendants of Kothah were allotted ten towns from the tribes of Ephraim, Dan, and the half-tribe of Manasseh.
Ndipo mabanja otsala a Kohati anapatsidwa mizinda khumi kuchokera ku mafuko a Efereimu, Dani ndi theka la fuko la Manase.
6 The families of the descendants of Gershon were allotted thirteen towns from the tribes of Issachar, Asher, Naphtali, and the half-tribe of Manasseh living in Bashan.
Zidzukulu za Geresoni zinapatsidwa mizinda 13 kuchokera ku mabanja a mafuko a Isakara, Aseri, Nafutali ndi theka la fuko la Manase ku Basani.
7 The families of the descendants of Merari were allotted twelve towns from the tribes of Reuben, Gad, and Zebulun.
Mabanja a Merari anapatsidwa mizinda khumi ndi iwiri kuchokera ku mafuko a Rubeni, Gadi ndi Zebuloni.
8 So the Israelites gave the Levites by lot these towns and pastures, as the Lord had instructed through Moses.
Choncho Aisraeli anapereka kwa fuko la Levi mizindayi pamodzi ndi malo odyetserako ziweto pogwiritsa ntchito maere, monga Yehova analamula kudzera mwa Mose.
9 They gave from the tribe of Judah and the tribe of Simeon the following towns, specifically named,
Awa ndi mayina a mizinda ya mafuko a Yuda ndi Simeoni imene inaperekedwa kwa zidzukulu za Aaroni,
10 to the families of the Kothaites, descendants of Aaron, of the tribe of Levi, since the first lot fell to them:
ku banja la Kohati amene anali Alevi. Paja maere oyamba anagwera mabanja a Kohati kuti alandira mizinda.
11 Kiriath-arba (or Hebron), in the hill country of Judah, together with the pastures around it. (Arba was the forefather of Anak.)
Anapatsidwa mzinda wa Kiriati Ariba. (Paja Ariba ndiye kholo la Anaaki). Dzina lina la mzindawu ndi Hebroni, ndipo unali mʼdziko la mapiri la Yuda. Pamodzi ndi mzindawu anapatsidwanso mabusa ake onse ozungulira.
12 But the more distant fields from the town and the villages had been given to Caleb son of Jephunneh to own.
Komabe minda ndi midzi yozungulira mizindayi inali itaperekedwa kale kwa Kalebe, mwana wa Yefune kuti ikhale cholowa chake.
13 They gave to the descendants of Aaron the priest the following towns and their pastures: Hebron (a sanctuary town for those who accidentally committed murder), Libnah,
Choncho zidzukulu za Aaroni wansembe, zinapatsidwa Hebroni (mzinda wopulumukirako amene wapha munthu), Libina,
16 Ain, Juttah, and Beth-shemesh—nine towns from these two tribes.
Aini, Yuta, ndi Beti-Semesi pamodzi ndi mabusa odyetseramo ziweto ozungulira mizindayi. Yonse pamodzi inali mizinda isanu ndi inayi yochokera ku mafuko awiriwa.
17 From the tribe of Benjamin the following four towns and their pastures: Gibeon, Geba,
Fuko la Benjamini linapereka Gibiyoni, Geba,
Anatoti ndi Alimoni, pamodzi ndi mabusa odyetsera ziweto ozungulira mizindayi. Yonse pamodzi inali mizinda inayi.
19 So in total thirteen towns and their pastures were given to the priests, the descendants of Aaron.
Choncho mizinda 13 pamodzi ndi malo odyetsera ziweto anapatsidwa kwa ansembe, zidzukulu za Aaroni.
20 As for the remaining families of the children of Kothah from the tribe of Levi, they were given by lot four towns and their pastures from the tribe of Ephraim:
Mabanja ena otsalira a Kohati a fuko la Levi anapatsidwa mizinda iyi kuchokera ku fuko la Efereimu:
21 Shechem in the hill country of Ephraim (a sanctuary town for those who accidentally committed murder), Gezer,
Mizinda ya Sekemu ndi Gezeri ndiye inali mizinda wopulumukirako munthu aliyense wopha mnzake mwangozi. Mizindayi inali ku mapiri a Efereimu.
22 Kibzaim, and Beth-horon.
Analandiranso mizinda ya Gezeri, Kibuzaimu, Beti-Horoni pamodzi ndi malo odyetsera ziweto ozungulira mizindayi. Yonse pamodzi inali mizinda inayi.
23 From the tribe of Dan, the following four towns and their pastures: Eltekeh, Gibbethon,
Fuko la Dani linapereka mizinda ya Eliteke, Gibetoni,
24 Aijalon, and Gath-rimmon.
Ayaloni, Gati-Rimoni pamodzi ndi mabusa odyetsera ziweto ozungulira mizindayi. Yonse pamodzi inali mizinda inayi.
25 From the half-tribe of Manasseh the following two towns and their pastures: Taanach and Gath-rimmon.
Kuchokera ku theka la fuko la Manase analandira Taanaki ndi Gati-Rimoni pamodzi ndi malo awo owetera ziweto, mizinda iwiri.
26 So in total ten towns and their pastures were given to remaining families of the descendants of Kothah.
Mizinda khumi yonseyi pamodzi ndi malo odyetsera ziweto, zinapatsidwa ku mabanja ena onse a Akohati.
27 The families of the descendants of Gershon from the tribe of Levi received the following two towns and their pastures from the half-tribe of Manasseh: Golan in Bashan (a sanctuary town for those who accidentally committed murder), and Be-eshterah.
Mabanja a Ageresoni a fuko la Levi anapatsidwa mizinda iwiri kuchokera ku theka la Manase wa kummawa, Golani ku Basani (mzinda wopulumukirako amene wapha munthu mwangozi) ndi Beesitera, pamodzi ndi malo awo odyetserako ziweto.
28 From the tribe of Issachar the following four towns and their pastures: Kishion, Daberath,
Fuko la Isakara linapereka mizinda ya Kisoni, Daberati,
29 Jarmuth, and En-gannim.
Yarimuti ndi Eni Ganimu, pamodzi ndi malo awo odyetsera ziweto. Yonse pamodzi inali mizinda inayi.
30 From the tribe of Asher the following four towns and their pastures: Mishal, Abdon,
Fuko la Aseri linapereka mizinda ya Misali, Abidoni,
Helikati ndi Rehobu pamodzi ndi malo awo odyetsera ziweto. Yonse pamodzi inali mizinda inayi.
32 From the tribe of Naphtali the following three towns and their pastures: Kedesh in Galilee (a sanctuary town for those who accidentally committed murder), Hammoth-dor, and Kartan.
Fuko la Nafutali linapereka mizinda ya Kedesi wa ku Galileya, mzinda umene unali wopulumukiramo munthu wopha mnzake mwangozi. Analandiranso mizinda ya Hamoti-Dori ndi Karitani. Kuphatikizira apa, analandira malo odyetsera ziweto a mizindayi. Yonse pamodzi inali mizinda inayi.
33 So in total thirteen towns and their pastures were allotted to the families of Gershon.
Mabanja onse a Ageresoni analandira mizinda 13 pamodzi ndi malo awo odyetsera a ziweto.
34 The families of the descendants of Merari, those remaining from the tribe of Levi, received the following four towns and their pastures from the tribe of Zebulun: Jokneam, Kartah,
Mabanja a Merari amene anali otsala a fuko la Levi, anapatsidwa mizinda iyi kuchokera ku fuko la Zebuloni: Yokineamu, Karita,
Dimuna ndi Nahalali, pamodzi ndi malo awo odyetsera ziweto. Yonse pamodzi inali mizinda inayi.
36 From the tribe of Reuben the following four towns and their pastures: Bezer, Jahaz,
Kuchokera ku fuko la Rubeni analandira Bezeri, Yahaza,
37 Kedemoth, and Mephaath.
Kedemoti ndi Mefaati, pamodzi ndi malo awo odyetsera ziweto. Yonse pamodzi inali mizinda inayi.
38 From the tribe of Gad the following four towns and their pastures: Ramoth in Gilead (a sanctuary town for those who accidentally committed murder), Mahanaim,
Kuchokera ku fuko la Gadi analandira mzinda wa Ramoti ku Giliyadi. Mzinda umene unali wopulumukiramo munthu wopha mnzake mwangozi.
Analandiranso mizinda ya Mahanaimu, Hesiboni, Yazeri pamodzi ndi malo odyetserako ziweto ozungulira mizinda yonseyi. Yonse pamodzi inali mizindayi anayi.
40 So in total twelve towns were allotted to the families of Merari, those remaining from the tribe of Levi.
Choncho mabanja onse a Merari, amene anali otsala a fuko la Levi analandira mizinda khumi ndi iwiri pogwiritsa ntchito maere.
41 The Levites received a total of forty-eight towns and pastures within the land of the Israelites.
Motero mizinda 48 ya mʼdziko limene Aisraeli analanda inapatsidwa kwa Alevi, kuphatikizapo malo ake odyetsera ziweto.
42 Each of these towns had pastures around them.
Iliyonse mwa mizindayi inali ndi malo owetera ziweto oyizungulira.
43 And so the Lord gave to the Israelites all the land he had promised their ancestors. They took possession of it and settled there.
Motero Yehova anapereka kwa Israeli dziko limene analumbira kulipereka kwa makolo awo. Atalilandira anadzakhalamo.
44 The Lord gave them peace on every side as he had promised their ancestors. Not a single one of their enemies could stand against them, for the Lord had handed their enemies over to them to defeat.
Yehova anawapatsa mtendere mʼdziko lonse monga momwe analonjezera makolo awo. Palibe ndi mmodzi yemwe mwa adani awo amene anatha kuwagonjetsa chifukwa Yehova anapereka adani awo onse mʼmanja mwawo.
45 Not a single one of the good things the Lord promised Israel had failed; everything had come true.
Yehova anakwaniritsa zonse zimene analonjeza kwa Aisraeli.