< Joshua 19 >
1 The second lot cast went to the tribe of Simeon, by families. The land was within the land allotted to the tribe of Judah.
Maere achiwiri anagwera mabanja a fuko la Simeoni. Dziko lawo linali mʼkati mwenimweni mwa dziko la Yuda.
2 Their allocation included Beersheba, Sheba, Moladah,
Dzikolo linaphatikiza zigawo izi: Beeriseba (ndi Seba), Molada,
3 Hazar-shual, Balah, Ezem,
Hazari-Suwali, Bala, Ezemu,
4 Eltolad, Bethul, Hormah,
Elitoladi, Betuli, Horima,
5 Ziklag, Beth-marcaboth, Hazar-susah,
Zikilagi, Beti-Marikaboti, Hazari-Susa,
6 Beth-lebaoth, and Sharuhen—thirteen towns with their associated villages.
Beti-Lebaoti ndi Saruheni. Yonse pamodzi inali mizinda 13 ndi midzi yawo.
7 Also: Ain, Rimmon, Ether, and Ashan—four towns with their associated villages,
Panalinso mizinda inayi iyi: Aini, Rimoni, Eteri ndi Asani pamodzi ndi midzi yawo.
8 as well as all the villages around these towns as far as Baalath-beer (or Ramah of the Negev). This was the land allotted to the tribe of Simeon, by families.
Dzikolo linaphatikizanso midzi yonse yozungulira mizinda imeneyi mpaka ku Baalati-Beeri, ndiye kuti Rama wa kummwera. Ili ndi dziko limene mabanja a fuko la Simeoni analandira kukhala lawo.
9 The allocation of the tribe of Simeon was part of that given to the tribe of Judah, since what the tribe of Judah had received was too large for them.
Cholowa cha fuko la Simeoni chinatengedwa kuchokera ku gawo la Yuda chifukwa fuko la Yuda linali lalikulu kwambiri. Izi zinachititsa fuko la Simeoni kukhala mʼkati mwenimweni mwa dziko la Yuda.
10 The third lot cast went to the tribe of Zebulun, by families. The boundary of their allocation began at Sarid,
Maere achitatu anagwera mabanja a fuko la Zebuloni: Malire a dziko lawo anafika mpaka ku Saridi.
11 and then went west past Maralah, touched Dabbeshah, and then the brook near Jokneam.
Malirewo anakwera kupita cha kumadzulo ku Marala nakafika ku Dabeseti ndi ku mtsinje wa kummawa kwa Yokineamu.
12 Going the other way from Sarid, the boundary headed east to the border of Kislot-tabor, on to Daberath, and then up to Japhia.
Kuchokera ku mbali ina ya Saridi malire anakhota kupita kummawa ku malire a Kisiloti-Tabori mpaka ku Daberati nakwera mpaka ku Yafiya.
13 From there it ran east to Gath-hepher, Eth-kazin, and on to Rimmon, and turned towards Neah.
Kuchokera kumeneko anabzola kulowa cha kummawa mpaka ku Gati-Heferi ndi ku Eti Kazini ndi kumaloza ku Neya njira ya ku Rimoni.
14 There the boundary turned north to Hannathon, ending at the valley of Iphtah-el.
Mbali ya kumpoto malirewo analoza ku Hanatoni ndipo anakathera ku chigwa cha Ifita Eli.
15 The towns included: Kattath, Nahalal, Shimron, Idalah, and Bethlehem—twelve towns with their associated villages.
Anaphatikizapo Katati, Nahalala, Simironi, Idala ndi Betelehemu. Mizinda yonse inakwana khumi ndi iwiri pamodzi ndi midzi yake.
16 This was the allocation—the land, towns, and villages—given to the tribe of Zebulun, by families.
Mizinda imeneyi pamodzi ndi midzi yake ndi imene mabanja a fuko la Zebuloni analandira.
17 The fourth lot cast went to the tribe of Issachar, by families.
Maere achinayi anagwera mabanja a fuko la Isakara.
18 Their land included these towns: Jezreel, Kesulloth, Shunem,
Dziko lawo linaphatikiza zigawo izi: Yezireeli, Kesuloti, Sunemu,
19 Hapharaim, Shion, Anaharath,
Hafaraimu, Sioni, Anaharati,
20 Rabbith, Kishion, Ebez,
Rabiti, Kisoni, Ebezi,
21 Remeth, En-gannim, En-haddah, and Beth-pazzez.
Remeti, Eni Ganimu, Eni Hada ndi Beti-Pazezi.
22 The boundary also reached the towns of Tabor, Shahazumah, and Beth-shemesh, and ended at the Jordan River—sixteen towns with their associated villages.
Malirewa anakafikanso ku Tabori, Sahazuma ndi Beti-Semesi ndipo anakathera ku Yorodani. Mizinda yonse inalipo 16 ndi midzi yake.
23 This was the allocation—the land, towns, and villages—given to the tribe of Zebulun, by families.
Mizinda imeneyi pamodzi ndi midzi yake ndiyo inali cholowa cha mabanja a fuko la Isakara.
24 The fifth lot cast went to the tribe of Asher, by families.
Maere achisanu anagwera mabanja a fuko la Aseri.
25 Their allocation included the towns of Helkath, Hali, Beten, Acshaph,
Gawo lawo linaphatikiza Helikati, Hali, Beteni, Akisafu,
26 Allammelech, Amad, and Mishal. Their boundary reached Carmel and Shihor-libnat in the west.
Alameleki, Amadi ndi Misali. Kumadzulo malire anafika ku Karimeli ndi Sihori Libinati.
27 Then it turned east towards Beth-dagon, reaching the land of Zebulun and the valley of Iphtah-el. From there it headed north to Beth-emek and Neiel, and continued north to Cabul, and on through to
Kenaka anakhotera kummawa kulowera ku Beti-Dagoni nafika ku dziko la Zebuloni ndi ku chigwa cha Ifita Eli, ndipo anapita kumpoto ku Beti-Emeki ndi Neieli. Anapitirirabe kumpoto mpaka kukafika ku Kabuli,
28 Ebron, Rehob, Hammon, Kanah, and on up to Great Sidon.
Ebroni, Rehobu, Hamoni, ndi Kana, mpaka ku Sidoni Wamkulu.
29 The boundary then turned towards Ramah and then the fortified town of Tyre, turning to Hosah and ending at the sea. Towns included Mehebel, Aczib,
Kenaka malirewo anakhotera ku Rama ndi kupita ku mzinda wotetezedwa wa ku Turo. Kuchokera pamenepo malirewo anakhota kupita ku Hosa nakatulukira ku Nyanja, mʼchigawo cha Akizibu,
30 Ummah, Aphek, and Rehob—twenty-two towns with their associated villages.
Uma, Afeki ndi Rehobu. Mizinda yonse inalipo 22 pamodzi ndi midzi yake.
31 This was the allocation—the land, towns, and villages—given to the tribe of Asher, by families.
Mizinda yonseyi pamodzi ndi midzi yake ndiyo inali cholowa cha mabanja a fuko la Aseri.
32 The sixth lot cast went to the tribe of Naphtali, by families.
Maere achisanu ndi chimodzi anagwera mabanja a fuko la Nafutali.
33 Their boundary began at Heleph, by the oak at Zaananim, and went across to Adami-nekeb, Jabneel, and up to Lakkum, and ending at the Jordan.
Malire awo anayambira ku Helefu mpaka ku mtengo wa thundu wa ku Zaananimu, ndipo anapitirira nʼkukafika ku Adami Nekebu, Yabineeli mpaka ku Lakumi ndi kukathera ku Yorodani.
34 Then the boundary headed west to Aznoth-tabor, and on to Hukkok. It reached the land of Zebulun on the south, the land of Asher on the west, and the Jordan on the east.
Tsono malirewo anakhotera kumadzulo kupita ku Azinoti-Tabori. Kuchoka kumeneko anapita ku Hukoki, modutsa Zebuloni cha kummwera, Aseri cha kumadzulo ndi mtsinje wa Yorodani cha kummawa.
35 The fortified towns included: Ziddim, Zer, Hammath, Rakkath, Kinnereth,
Mizinda yotetezedwa inali Zidimi, Zeri, Hamati, Rakati, Kinereti,
37 Kedesh, Edrei, En-hazor,
Kedesi, Ederi, Eni Hazori,
38 Yiron, Migdal-el, Horem, Beth-anath, and Beth-shemesh—nineteen towns with their associated villages.
Yironi, Migidali Eli, Horemu, Beti-Anati ndi Beti-Semesi. Yonse pamodzi inalipo mizinda 19 ndi midzi yake.
39 This was the allocation—the land, towns, and villages—given to the tribe of Naphtali, by families.
Mizinda yonseyi pamodzi ndi midzi yawo ndiyo inali cholowa cha mabanja a fuko la Nafutali.
40 The seventh lot cast went to the tribe of Dan, by families.
Maere achisanu ndi chiwiri anagwera mabanja a fuko la Dani.
41 Their allocation included the towns of Zorah, Eshtaol, Ir-shemesh,
Gawo lawo linaphatikiza mizinda iyi: Zora, Esitaoli, Iri Semesi,
42 Shaalabbin, Aijalon, Ithlah,
Saalabini, Ayaloni, Itira,
44 Eltekeh, Gibbethon, Baalath,
Eliteke, Gibetoni, Baalati,
45 Jehud, Bene-berak, Gath-rimmon,
Yehudi, Beni Beraki, Gati-Rimoni,
46 Me-jarkon, Rakkon, along with the territory opposite Joppa.
Me-Yarikoni ndi Rakoni, pamodzi ndi dera loyangʼanana ndi Yopa.
47 However, the tribe of Dan was not able to hold on to their allotted land, so they went and attacked Leshem and captured it. They slaughtered its inhabitants and took possession of the town, settling there. They renamed Leshem as Dan, after their ancestor.
Anthu a fuko la Dani atalandidwa dziko lawo, anapita kukathira nkhondo Lesemu. Iwo anapha anthu ake onse, nawulandiratu mzindawo, kuwusandutsa wawo ndi kumakhalamo. Tsono anatcha mzindawo dzina loti Dani popeza ndilo linali dzina la kholo lawo.
48 This was the allocation—the land, towns, and villages—given to the tribe of Dan, by families.
Mizinda yonseyi pamodzi ndi midzi yake ndiyo inali cholowa cha mabanja a fuko la Dani.
49 After they finished allotting the land and establishing its borders, the Israelites gave Joshua, son of Nun, an allocation among them.
Atatha kugawana zigawo zosiyanasiyana za dzikolo, Aisraeli anamupatsa Yoswa mwana wa Nuni chigawo chake.
50 Following the Lord's command, they gave him the town he requested—Timnath-serah in the hill country of Ephraim. He rebuilt the town and settled there.
Potsata zimene Yehova anawalamula, anamupatsa mzinda wa Timnati-Sera umene anawupempha. Mzindawu unali mʼdziko lamapiri la Efereimu. Iye anawumanga mzindawu ndi kukhazikikako.
51 These were the allocations distributed by Eleazar the priest, Joshua, son of Nun, and the leaders of the Israelite tribes. They were made by casting lots at Shiloh in the presence of the Lord at the entrance of the Tent of Meeting. So they finished dividing up the land.
Wansembe Eliezara, Yoswa ndi atsogoleri a mabanja onse a Israeli anagawa dziko lija zigawozigawo pogwiritsa ntchito maere pamaso pa Yehova. Izi zinachitika ku Silo pa khomo la tenti ya msonkhano. Choncho anamaliza kugawa dzikolo.