< Job 40 >

1 God continued speaking to Job.
Yehova anati kwa Yobu:
2 “Are you still going to fight with the Almighty and try to set him straight? Anyone who argues with God must give some answers.”
“Kodi iwe ufuna kukangana ndi Wamphamvuzonse? Iwe amene unatsutsana ndi Mulungu umuyankhe Iyeyo!”
3 Job answered the Lord,
Pamenepo Yobu anayankha Yehova:
4 “Me—I am nothing at all. I have no answers. I put my hand in front of my mouth.
“Ine sindili kanthu konse, kodi ndingathe kukuyankhani chiyani? Ndagwira pakamwa panga.
5 I have already said far too much and I won't say anything more.”
Ndinayankhula kamodzi, koma pano ndilibe yankho, ndinayankha kawiri, koma sindiwonjezeranso mawu ena.”
6 Then the Lord answered Job out of the whirlwind,
Ndipo Yehova anayankha Yobu mʼkamvuluvulu kuti,
7 “Prepare yourself, be strong, for I am going to question you, and you must answer me.
“Tsopano vala dzilimbe ngati mwamuna; ndikufunsa mafunso ndipo iwe undiyankhe.
8 Are you really going to say my decisions are wrong? Are you going to condemn me so you can be right?
“Kodi iwe unganyoze chiweruzo changa cholungama? Kodi ungandidzudzule kuti iweyo ukhale wolungama?
9 Are you as powerful as I am? Does your voice thunder like mine?
Kodi uli ndi dzanja monga la Mulungu, ndipo mawu ako angagunde ngati mphenzi monga a Mulungu?
10 Why don't you dress yourself with majesty and dignity, and clothe yourself with glory and splendor!
Ngati zili choncho udzikometsere ndi ulemerero ndi kukongola, ndipo udziveke ulemu ndi ulemerero waufumu.
11 Let loose your fierce anger. Humble the proud with a glance.
Tsanula ukali wako wosefukirawo, uyangʼane aliyense wodzikuza ndipo umuchepetse,
12 Bring down the proud with your gaze; tread the wicked underfoot right where they are.
Uyangʼane aliyense wodzikweza ndipo umutsitse, uwapondereze oyipa onse pamalo pomwe alilipo.
13 Bury them in the dust; lock them away in the grave.
Onsewo uwakwirire pamodzi mfumbi; ukulunge nkhope zawo mʼmanda.
14 Then I will also agree that your own strength can save you.
Ukatero Ine ndidzakuvomereza kuti dzanja lako lamanja lakupulumutsadi.
15 Consider Behemoth, a creature I made just like I made you. It eats grass like cattle.
“Taganiza za mvuwu, imene ndinayipanga monga momwe ndinapangira iwe, ndipo imadya udzu ngati ngʼombe.
16 Look at its powerful loins, the muscles of its belly.
Mphamvu zake ndi zazikulu kwambiri, thupi lake ndi lanyonga kwambiri!
17 It bends its tail like a cedar; its thigh sinews are strong.
Mchira wake umayima tolotolo ngati mtengo wamkungudza; mitsempha ya ntchafu zake ndi yogwirana bwino.
18 Its bones are like bronze tubes; its limbs like iron rods.
Mafupa ake ali ngati mapayipi amkuwa, nthiti zake zili ngati mipiringidzo yachitsulo.
19 It is the most important example of what God can do; only the one who made it can approach it with a sword.
Mvuwuyo ndi yayikulu mwa zolengedwa za Mulungu, komatu mlengi wake amatha kuyiopseza ndi lupanga lake.
20 The hills produce food for it, and all the wild animals play there.
Imapeza chakudya chake ku mtunda ndipo nyama zakuthengo zonse zimasewera pambali pake.
21 It lies under the lotus; it hides in the reeds of the marsh.
Imagona pa tsinde pa zitsamba za mipeta, imabisala mʼbango ndiponso pa thawale.
22 The lotus covers it with shade; the willow trees of the valley surround it.
Imaphimbika ndi mthunzi wazitsamba za mipeta; imazunguliridwa ndi misondozi ya mu mtsinje.
23 Even if the river is in flood, it is not concerned; it remains calm when the Jordan river surges against it.
Madzi a mu mtsinje akakokoma, sichita mantha, iyo sitekeseka, ngakhale madzi a mu Yorodani afike mʼkhosi mwake.
24 No one can catch it while it is watching, or pierce its nose with a noose.
Kodi alipo amene angathe kukola mvuwu ndi mbedza kapena kuyikola mu msampha?

< Job 40 >