< Job 39 >
1 Do you know when the wild goats give birth? Have you watched the birth-pains of the deer?
“Kodi iwe umadziwa nthawi imene mbalale yayikazi imaswera? Kodi umaonerera pamene nswala ikubala?
2 Do you know how many months they carry their young? Do you know the time when they give birth?
Kodi umawerenga miyezi imene zimakhala ndi bere? Kodi nthawi imene zimaswana iwe umayidziwa?
3 They crouch down in labor to deliver their offspring.
Zimakhala tsonga ndi kuswa ana awo; pamenepo ululu wobereka nʼkutha.
4 Their young grow strong in the open countryside; they leave and never return.
Ana a nyamazi amakhala ndi mphamvu ndipo amakulira mʼthengo; kenaka amachoka ndipo sabwereranso.
5 Who gave the wild donkey its freedom? Who set it free from its bonds?
“Kodi bulu wakuthengo amamupatsa ndani ufulu wongodziyendera? Ndani amamasula zingwe zake?
6 I have given it the wilderness as its home, the salt plains as a place to live.
Ine ndinamupatsa chipululu kuti chikhale mudzi wake, nthaka ya mchere kuti ikhale malo ake okhalamo
7 It despises the noise of the city; it doesn't need to listen to the shouts of a driver.
Iye amakhala kutali ndi phokoso la mu mzinda; ndipo samva kufuwula kwa oyendetsa nyama zakatundu.
8 It hunts in the mountains for pastureland, searching for all kinds of green plants to eat.
Amayendayenda mʼmapiri kudya msipu ndipo amafunafuna msipu uliwonse wobiriwira.
9 Is the wild ox willing to serve you? Will it spend the night at your manger?
“Kodi njati ingavomere kukutumikira? Kodi ingagone mu gome lako usiku?
10 Can you tie a wild ox to a plow? Can you make it till your fields for you?
Kodi ungathe kuyimanga ndi zingwe kuti izilima? Kodi ingasalaze nthumbira mʼmunda mwako?
11 Because it's so powerful can you trust it? Can you depend on it to do your heavy work for you?
Kodi ungadalire njatiyo chifukwa champhamvu zake? Kodi ungayilekere kuti igwire ntchito zako zolemetsa?
12 Are you sure it will gather your grain and bring it to your threshing floor?
Kodi ungadalire kuti idzakubweretsera tirigu wako ndi kumuyika ku malo opunthira?
13 The ostrich proudly flaps her wings, but they are nothing like the flight feathers of the stork.
“Nthiwatiwa imakupiza mapiko ake monyadira, koma mapikowo sangafanane ndi mapiko ndi nthenga za kakowa.
14 The ostrich abandons her eggs on the ground, leaving them to be warmed in the dust.
Nthiwatiwa imakwirira mazira ake pansi ndipo amafundidwa ndi nthaka,
15 She doesn't think that they can be crushed underfoot, trampled by a wild animal.
nthiwatiwayo sidera nkhawa kuti mazira ake angathe kuswanyidwa, ndi kuti nyama zakuthengo zitha kuwaponda.
16 She is tough towards her young, acting as if they didn't belong to her. She doesn't care that all her work was for nothing.
Nthiwatiwa imachitira nkhanza ana ake ngati anawo si ake; Imayiwala zoti inavutika powabala.
17 For I, God, made her forget wisdom—she didn't get her share of intelligence.
Chifukwa Mulungu anayimana nzeru, simvetsa kanthu kalikonse.
18 But when she needs to, she can jump up and run, mocking a horse and its rider with her speed.
Komatu nthiwatiwa ikadzambatuka ndi kuyamba kuthamanga, imamusiya kutali kavalo ndi wokwerapo wake.
19 Did you give the horse its strength? Did you place a mane upon its neck?
“Kodi ndiwe amene umamupatsa mphamvu kavalo kapena kumuveka chenjerere mʼkhosi mwake?
20 Did you make it able to jump like a locust? Its loud snorting is terrifying!
Kodi ndiwe amene umalipatsa dzombe ulemerero wolumphira, ukali wake nʼkumachititsa mantha?
21 It paws at the ground, rearing up with power as it charges into battle.
Iye amalumphalumpha moopseza, kukondwerera mphamvu zake, ndipo amapita ku nkhondo ndi mphamvu zake zonse.
22 It laughs at fear; it is not frightened at all.
Iye sachita mantha, saopa chilichonse; sabwerera mʼmbuyo akaona lupanga.
23 The quiver full of arrows rattles against it; the spear and the javelin flash in the sunlight.
Zida zankhondo zimachita kwichikwichi mʼchimake pambali pake pamodzi ndi mkondo wonyezimira ndi nthungo.
24 Shaking with rage it gallops across the ground; it cannot remain still when the trumpet sounds.
Kavaloyo amanjenjemera ndi ukali ndi kulumphalumpha; satha kungoyima pamene wamva kulira kwa lipenga.
25 Whenever the trumpet calls, it is ready; he senses the sound of battle from far away, he hears the commanders shouting.
Lipenga likalira amati, ‘Twee!’ Amamva fungo la nkhondo ali patali, kufuwula kwa anthu olamulira nkhondo ndi mfuwu wankhondo.
26 Is it through your wisdom that the hawk soars, spreading its wings towards the south?
“Kodi kabawi amawuluka ndi nzeru zako, ndi kutambasula mapiko ake kupita kummwera?
27 Do you command the eagle to fly high and make its nest in the summits of the mountains?
Kodi umalamulira chiwombankhanga ndiwe kuti chiziwuluka ndi kumanga chisa chake pamwamba penipeni?
28 It lives among the cliffs, and roosts on a remote rocky crag.
Chimakhala pa phiri ndipo chimakhala pamenepo usiku; chimakhala pa msonga penipeni pa mwala.
29 From there it spies its prey from far away, fixing its gaze on its victim. Its chicks eagerly swallow blood.
Chili pamenepo chimayangʼanayangʼana choti chigwire kuti chidye; maso ake amachionera patali chinthucho.
30 Where the carcasses are, that's where birds of prey are found.”
Ana ake amayamwa magazi, ndipo kumene kuli mitembo ndiko chimapezeka.”