< Job 27 >
1 Job began to speak again.
Ndipo Yobu anapitiriza kuyankhula kwake:
2 “I promise you—as God lives, who has denied me justice, the Almighty, who has made my life bitter,
“Ndithu pali Mulungu wamoyo, amene wakana kundiweruza molungama, Wamphamvuzonse, amene wawawitsa mtima wanga,
3 for as long as I have life, while the breath of God remains in my nostrils—
nthawi zonse pamene ndili ndi moyo, mpweya wa Mulungu uli mʼmphuno mwanga,
4 my lips will never speak lies, my tongue will never be dishonest.
pakamwa panga sipadzatuluka mawu oyipa, lilime langa silidzayankhula zachinyengo.
5 I will never agree that you are right; I will insist on my innocence until the day I die.
Sindidzavomereza kuti inu mukunena zoona; mpaka imfa yanga, sindidzataya ungwiro wanga.
6 I'm convinced I'm right and will never give up believing this; my conscience will not condemn me as long as I live.
Ndidzasunga chilungamo changa ndipo sindidzalola kuti chindichokere; chikumbumtima changa sichidzanditsutsa nthawi yonse ya moyo wanga.
7 May my enemy become like the wicked; may those who oppose me become like those who do evil.
“Mdani wanga akhale ngati woyipa, wondiwukira akhale ngati munthu wosalungama!
8 For what hope do those who reject God have when he cuts them down, when God brings their lives to an end?
Nanga chiyembekezo cha munthu wosapembedza nʼchiyani pamene aphedwa, pamene Mulungu achotsa moyo wake?
9 When times of trouble come to them, will God hear their cry for help?
Kodi Mulungu amamva kulira kwake pamene zovuta zamugwera?
10 Do they have a good relationship with the Almighty? Can they call on God at any time?
Kodi adzapeza chikondwerero mwa Wamphamvuzonse? Kodi adzapemphera kwa Mulungu nthawi zonse?
11 Let me explain God's power to you. I will not keep anything back that the Almighty has planned.
“Ndidzakuphunzitsani za mphamvu ya Mulungu ndipo sindidzabisa njira za Wamphamvuzonse.
12 If all of you have recognized this, why do you talk such vain nonsense?
Inu mwadzionera nokha zonsezi. Nanga bwanji mukuyankhula zopanda pake?
13 This is what God provides as the destiny for the wicked, this is the inheritance that the ruthless will receive from the Almighty—
“Pano pali chilango chimene Mulungu amasungira woyipa, cholowa chimene munthu wankhanza amalandira kuchokera kwa Wamphamvuzonse.
14 even if they have many children, they will experience violent deaths or die of starvation.
Angakhale ana ake achuluke chotani adzaphedwa ndi lupanga ndipo zidzukulu zake zidzasowa zakudya.
15 Those who survive will die from disease, and even their widows will not mourn for them.
Amene adzatsalireko adzafa ndi mliri, ndipo akazi awo amasiye sadzawalira.
16 Even though they pile up silver like dust, and clothes like heaps of clay,
Ngakhale aunjike siliva ngati fumbi, ndi kukundika zovala ngati mchenga,
17 those who do good will wear the clothes and the innocent will divide the silver among them.
zimene wasungazo wolungama ndiye adzavale, ndipo anthu osalakwa ndiwo adzagawane siliva wakeyo.
18 They build their houses like a moth; like some flimsy shelter made by a watchman.
Nyumba imene akuyimanga ili ngati mokhala kadziwotche, ili ngati msasa umene mlonda amamanga.
19 They go to bed rich, but never again! For when they wake up, it's all gone.
Amapita kokagona ali wolemera koma kutha kwake nʼkomweko; akatsekula maso ake, chuma chake chonse chapita.
20 Waves of panic flood over them; in the night a whirlwind snatches them away.
Zoopsa zimamukokolola ngati madzi achigumula; mphepo yamkuntho imamunyamula usiku.
21 The east wind picks them up and they're gone, carried away from where they were.
Mphepo ya kummawa imamuwulutsa ndipo iye saonekanso ndipo imamuchotsa pamalo pake.
22 The wind blows at them with full force; they try desperately to escape.
Imakuntha pa iye osamuchitira chisoni, pamene akuyesa kuthawa mphamvu zake mwaliwiro.
23 People clap their hands at them and hiss at them wherever they are.
Mphepoyo imamuwomba ndithu ndipo kuchokera pamalo pake imamuopseza.”