< Job 24 >

1 Why doesn't the Almighty set a definite time to punish the wicked? Why don't those who follow him never see him act in judgment?
“Chifukwa chiyani Wamphamvuzonse sayikiratu nthawi yoti aweruze? Chifukwa chiyani iwo amene amadziwa Iyeyo amayembekezera pachabe masiku oterewa?
2 The wicked move boundary stones; they seize other people's flocks and move them to their own pastures.
Anthu amasuntha miyala ya mʼmalire, kuti akuze dziko lawo; amadyetsa ziweto zimene aba.
3 They steal the orphan's donkey; they take the widow's ox as security for a debt.
Amalanda abulu a ana amasiye ndipo amatenganso ngʼombe ya mkazi wamasiye ngati chikole.
4 They push the poor out of their way; the destitute are forced to hide from them.
Amachotsa mʼmisewu anthu osauka, ndipo amathamangitsa amphawi onse mʼdziko.
5 Like wild donkeys in the desert, the poor have to scavenge for their food, looking for anything to feed their children in the wasteland.
Amphawiwo amakhala ngati mbidzi mʼchipululu, amayendayenda kufuna chakudya; dziko lowuma limapereka chakudya cha ana awo.
6 They are forced to find what they can in other people's fields, to glean among the vineyards of the wicked.
Iwo amakolola za mʼminda ya eni ake, ndipo amakunkha mphesa mʼminda ya anthu oyipa.
7 They spend the night naked because they have no clothes; they have nothing to cover themselves against the cold.
Amagona maliseche usiku wonse kusowa zovala; pa nthawi yozizira amasowa chofunda.
8 They are soaked by the cold mountain storms, and huddle beside the rocks for shelter.
Amavumbwa ndi mvula ya mʼmapiri ndipo amakangamira ku matanthwe kusowa pobisalapo.
9 Fatherless children are snatched from their mother's breasts, taking the babies of the poor as security for a debt.
Amatsomphola mwana wamasiye wa ku bere; ndipo amagwira mwana wakhanda wa mʼmphawi kuti akhale chikole.
10 Because they have no clothes to wear they have to go naked, harvesting sheaves of grain while they themselves are hungry.
Amphawi amangoyenda maliseche kusowa zovala; amasenza mitolo ya tirigu, koma nʼkumagonabe ndi njala.
11 In the olive groves they work to produce oil, but do not taste it; they tread the winepress, but are thirsty.
Iwo amayenga mafuta a olivi mʼminda ya anthu oyipa; amapsinya mphesa, koma nʼkumamvabe ludzu.
12 In the city the dying groan, and the wounded cry for help, but God ignores their prayers.
Kubuwula kwa anthu amene akufa kumamveka kuchokera mu mzinda, anthu ovulala akulirira chithandizo. Koma Mulungu sakuyimba mlandu wina aliyense.
13 These are people who rebel against the light. They do not want to know its ways, or to stay on its paths.
“Pali ena amene amakana kuwala, amene safuna kuyenda mʼkuwalako kapena kukhala mʼnjira zake.
14 The murderer gets up at dawn to kill the poor and needy, and when night falls he becomes a thief.
Dzuwa likalowa, wopha anzake amadzuka ndipo amakapha osauka ndi amphawi; nthawi ya usiku iye amasanduka mbala.
15 The adulterer waits for dusk, saying to himself, ‘No one will see me now,’ and he covers his face.
Munthu wachigololo amadikira chisisira; iyeyo amaganiza kuti, ‘Palibe amene akundiona,’ ndipo amaphimba nkhope yake.
16 Thieves break into houses during the night and they sleep during the day. They don't even know what the light is like!
Mbala zimathyola nyumba usiku, koma masana zimadzitsekera; izo zimathawa kuwala.
17 Total darkness is like light to them, for they are familiar with the night.
Pakuti kwa onsewa mdima wandiweyani ndiye kuti kwawachera. Iwo amachita ubale ndi zoopsa za mdima.
18 Like bubbles on the surface of a river they are quickly carried away. The land they own is cursed by God. They don't enter their own vineyards.
“Komatu iwowo ndi thovu loyandama pa madzi; minda yawo ndi yotembereredwa pa dzikolo kotero kuti palibe amene amapita ku minda ya mpesa.
19 Just as heat and drought dry up snowmelt, so Sheol takes away those who have sinned. (Sheol h7585)
Monga momwe kutentha ndi chilala zimasungunulira madzi owundana ndi momwemonso mmene manda amachotsera omwe achimwa. (Sheol h7585)
20 Even their mothers forget them, maggots feast on them, they are no longer remembered, and their wickedness becomes like a tree that is broken into pieces.
Mayi wowabereka amawayiwala, mphutsi zimasangalala powadya; anthu oyipa sakumbukiridwanso koma amathyoka ngati mtengo.
21 They mistreat childless women and are mean to widows.
Amachitira nkhanza mayi wosabala ndi mayi amene alibe mwana, ndipo sakomera mtima mkazi wamasiye.
22 God prolongs the life of the wicked by his power; but when they arise, they have no assurance of life.
Koma Mulungu amawononga munthu wamphamvu mwa mphamvu zake; ngakhale munthuyo atakhazikika, alibe chiyembekezo cha moyo wake.
23 He supports them and gives them security, but he is always watching what they're doing.
Mulungu atha kuwalola kuti akhale mosatekeseka, koma amakhala akupenyetsetsa njira zawo.
24 Though they may be illustrious for a while, soon they are gone. They are brought down like all others, cut off like the heads of grain.
Kwa kanthawi kochepa oyipa amakwezedwa ndipo kenaka saonekanso; amatsitsidwa ndipo amachotsedwa monga ena onse; amadulidwa ngati ngala za tirigu.
25 If this isn't so, who can prove I'm a liar and there's nothing to what I say?”
“Ngati zimenezi sizoona, ndani angaonetse kuti ndine wabodza ndi kusandutsa mawu anga kukhala wopanda pake?”

< Job 24 >