< Job 21 >

1 Job replied,
Pamenepo Yobu anayankha kuti,
2 “Please listen carefully to what I say—that would be one comfort you could give me.
“Mvetserani bwino mawu anga; ichi chikhale chitonthozo changa chochokera kwa inu.
3 Bear with me; let me speak. After I've spoken you can resume mocking me.
Ndiloleni ndiyankhule ndipo ndikatha kuyankhula munditonzetonze.
4 Am I complaining against people? Of course not. Why shouldn't I be impatient?
“Kodi ine ndikudandaulira munthu? Tsono ndilekerenji kupsa mtima?
5 Just take a look at me. Aren't you appalled? Cover your mouth with your hand in shock!
Ndipenyeni ndipo mudabwe; mugwire dzanja pakamwa.
6 Every time I think of what's happened to me I am horrified and I shake all over with fear.
Ndikamaganiza zimenezi ndimachita mantha kwambiri; thupi langa limanjenjemera.
7 Why do the wicked continue to live, to grow old and increasingly powerful?
Chifukwa chiyani anthu oyipa amakhalabe ndi moyo, amakalamba ndi kusanduka amphamvu?
8 Their children are with them; they watch their grandchildren grow up.
Amaona ana awo akukhazikika pamodzi nawo, zidzukulu zawo zikukula bwino iwo akuona.
9 They live in their homes in safety—they are not afraid. God does not use his rod to beat them.
Mabanja awo amakhala pa mtendere ndipo sakhala ndi mantha; mkwapulo wa Mulungu suwakhudza nʼkomwe.
10 Their bulls always breed successfully; their cows give birth to calves and do not miscarry.
Ngʼombe zawo zazimuna sizilephera kubereketsa; ngʼombe zawo zazikazi sizipoloza.
11 They send out their little ones like lambs to play; their children dance around.
Amatulutsa ana awo ngati gulu la nkhosa; makanda awo amavinavina pabwalo.
12 They sing accompanied by the tambourine and lyre; they celebrate with the music of the flute.
Amayimba nyimbo pogwiritsa ntchito matambolini ndi azeze; amakondwa pakumva kulira kwa chitoliro.
13 They live out their lives contentedly, and go down to Sheol in peace. (Sheol h7585)
Zaka zawo zimatha ali mu ulemerero ndipo amatsikira ku manda mwamtendere. (Sheol h7585)
14 Yet they tell God, ‘Get lost! We don't want anything to do with you.
Koma anthuwo amawuza Mulungu kuti, ‘Tichokereni!’ Ife tilibe chikhumbokhumbo chofuna kudziwa njira zanu.
15 Who does the Almighty think he is for us to serve him as slaves? What benefit is there for us if we pray to him?’
Kodi Wamphamvuzonseyo ndani kuti timutumikire? Ife tipindula chiyani tikamapemphera kwa Iyeyo?
16 Such people believe they make their own fortune, but I don't accept their way of thinking.
Komatu ulemerero wawo suli mʼmanja mwawo, koma ine ndimakhala patali ndi uphungu wa anthu oyipa.
17 How often is the lamp of the wicked snuffed out? How often does disaster come upon them? How often does God punish the wicked in his anger?
“Koma nʼkangati kamene nyale ya anthu oyipa imazimitsidwa? Nʼkangati kamene tsoka limawagwera? Nʼkangati kamene Mulungu amawakwiyira ndi kuwalanga?
18 Are they blown along like straw in the wind? Does a tornado come in and carry them away?
Nʼkangati kamene iwo amakhala ngati phesi lowuluka ndi mphepo, ngati mungu wowuluzika ndi kamvuluvulu?
19 Some say, ‘God saves up people's punishment for their children.’ But I say, ‘God should punish those people themselves so that they can learn from it.’
Paja amati, ‘Mulungu amalanga ana chifukwa cha machimo abambo awo.’ Koma Mulungu amabwezera chilango munthuyo, kuti adziwe kuti Mulungu amalangadi.
20 Let them see their destruction themselves, and drink deeply from God's anger.
Mulole kuti adzionere yekha chilango chake, kuti alawe ukali wa Wamphamvuzonse.
21 For they don't care what happens to their families once they're dead.
Nanga kodi amalabadira chiyani zabanja lake limene walisiya mʼmbuyo, pamene chiwerengero cha masiku ake chatha?
22 Can anyone teach God anything he doesn't already know, since he is the one who judges even heavenly beings?
“Kodi alipo wina amene angaphunzitse Mulungu nzeru, poti Iye amaweruza ngakhale anthu apamwamba?
23 One person dies in good health, totally comfortable and secure.
Munthu wina amamwalira ali ndi mphamvu zonse, ali pa mtendere ndi pa mpumulo,
24 Their body is fat from eating well; their bones still strong.
thupi lake lili lonenepa, mafupa ake ali odzaza ndi mafuta.
25 Another dies after a miserable life without every experiencing happiness.
Munthu wina amamwalira ali wowawidwa mtima, wosalawapo chinthu chabwino chilichonse.
26 Yet they are both buried in the same dust; they are treated alike in death, eaten by maggots.
Olemera ndi osauka omwe amamwalira ndi kuyikidwa mʼmanda ndipo onse amatuluka mphutsi.
27 Look, I know what you're thinking, and your schemes to do me wrong.
“Ndikudziwa bwino zimene mukuganiza, ziwembu zanu zomwe mukuti mundichitire.
28 You may ask me, ‘Where is the home of the great man? Where is the place where the wicked live?’
Inu mukuti, ‘Kodi nyumba ya mkulu uja ili kuti, matenti amene munkakhala anthu oyipa aja ali kuti?’
29 Haven't you asked people who travel? Don't you pay attention to what they tell you?
Kodi munawafunsapo anthu amene ali pa ulendo? Kodi munaganizirapo zimene iwo amanena?
30 Wicked people are spared in times of disaster; they are rescued from the day of judgment.
Zakuti munthu woyipa amasungidwa chifukwa cha tsiku la tsoka, kuti amapulumutsidwa chifukwa cha tsiku la ukali wa Mulungu?
31 Who confronts them with their actions? Who pays them back for what they have done?
Kodi ndani amadzudzula munthu wochimwayo? Ndani amamubwezera zoyipa zimene anachita?
32 When they eventually die and are carried to the graveyard, their tomb is guarded. The earth of the grave softly covers them.
Iye amanyamulidwa kupita ku manda ndipo anthu amachezera pa manda ake.
33 Everyone attends their funeral service; a huge procession of people comes to pay their last respects.
Dothi la ku chigwa limamukomera; anthu onse amatsatira mtembo wake, ndipo anthu osawerengeka amakhala patsogolo pa chitanda chakecho.
34 Why do you try to comfort me with worthless nonsense? Your answers are just a pack of lies!”
“Nanga inu mudzanditonthoza bwanji ine ndi mawu anu opandapakewo palibe chimene chatsala kuti muyankhe koma mabodza basi!”

< Job 21 >