< Job 17 >

1 My spirit is crushed; my life is extinguished; the grave is ready for me.
“Mtima wanga wasweka, masiku anga atha, manda akundidikira.
2 Mockers surround me. I see how bitterly they ridicule me.
Ndithudi, anthu ondiseka andizungulira; maso anga akupenyetsetsa mdani wanga.
3 God, you need to put down a pledge for me with yourself, for who else will be my guarantor?
“Inu Mulungu, patseni chikole chimene mukufuna. Ndani wina amene adzandiperekera ine chikole?
4 You have closed their minds to understanding, so do not let them win!
Inu mwatseka maganizo awo kuti asamvetse zinthu; choncho simudzawalola kuti apambane.
5 They betray friends to gain benefit for themselves and their children suffer for it.
Ngati munthu apereka mnzake chifukwa cha chuma, ana ake sadzaona mwayi.
6 He has made me a proverb of ridicule among the people; they spit in my face.
“Mulungu wandisandutsa chisudzo chochiseka aliyense, munthu amene anthu amalavulira malovu nkhope yake.
7 My eyes are worn out from crying and my body is a shadow of its former self.
Mʼmaso mwanga mwada ndi chisoni; ndawonda ndi mutu womwe.
8 People who think they are good are shocked to see me. Those who are innocent are troubled by the godless.
Anthu olungama akudabwa nazo zimenezi; anthu osachimwa akupsera mtima anthu osapembedza Mulungu.
9 Those who are right keep going, and those whose hands are clean grow stronger and stronger.
Komabe anthu olungama adzasunga njira zawo, ndipo anthu a makhalidwe abwino mphamvu zawo zidzanka zikuchuluka.
10 Why don't you come back and repeat again what you've been saying?—yet I still won't find a wise man among you!
“Tsono bwerani nonsenu, bwerezaninso mawu anuwo, sindidzapezapo munthu wanzeru pakati panupo.
11 My life is over. My plans are gone. My heart is broken.
Masiku anga atha, zimene ndinakonza zalephereka, pamodzinso ndi zokhumba za mtima wanga.
12 They turn night into day, and say that daylight is close to darkness.
Anthu awa amasandutsa usiku kukhala usana, nthawi ya usiku iwo amati ‘kwatsala pangʼono kucha.’
13 What am I looking for? To make my home in Sheol, to make my bed in darkness? (Sheol h7585)
Ngati nyumba imene ndikuyiyembekezera ndi manda, ngati ndiyala bedi langa mu mdima, (Sheol h7585)
14 Should I call the grave my father, and the maggot my mother or my sister?
ngati ndinena kwa dzenje la manda ‘ndinu abambo anga,’ ndiponso kwa mphutsi kuti, ‘ndinu amayi anga’ kapena ‘mlongo wanga,’
15 So then where is my hope? Can anyone see any hope for me?
tsono chiyembekezo changa chili kuti? Ndani angaone populumukira panga?
16 Will hope go down with me to the gates of Sheol? Will we go down together into the dust?” (Sheol h7585)
Ndithu sindidzakhalanso ndi chiyembekezo chilichonse, polowa mʼmanda, pamene ndidzatsikira ku fumbi.” (Sheol h7585)

< Job 17 >