< Job 12 >

1 Job replied,
Pamenepo Yobu anayankha kuti,
2 “You really think you're special people, don't you? Obviously when you die, wisdom will die with you!
“Ndithudi inuyo ndinu anthu ndipo nzeru zanu zidzafera nanu pamodzi!
3 But I too have insights, and you're no better than me. Doesn't everyone know the things you've said?
Koma inenso ndili nazo nzeru ngati inu; ineyo sindine munthu wamba kwa inu. Ndani amene sadziwa zonse zimene mwanenazi?
4 But my friends laugh at me because I called on God and he answered me: the innocent man who does right has become an object of derision.
“Ndasanduka chinthu choseketsa kwa abwenzi anga, ngakhale ndinkapemphera kwa Mulungu ndipo Iye ankandiyankha. Ine ndasanduka chinthu chongoseketsa, ngakhale ndili wolungama ndi wosalakwa!
5 People who are comfortable have contempt for those who are in trouble, ready to push over those who are already slipping.
Anthu amene ali pabwino amanyoza anzawo amene ali pa tsoka. Tsokalo limagwa pa amene wayamba kale kugwa.
6 Robbers live in peace, and those who make God angry live in safety, trusting their own strength as their ‘god.’
Nyumba za anthu achifwamba zimakhala pa mtendere, ndipo anthu amene amaputa Mulungu amakhala pabwino, amene amanyamula milungu yawo mʼmanja.
7 But if you ask the animals they will teach you, the birds in the sky will tell you;
“Koma funsa nyama zakuthengo ndipo zidzakuphunzitsa, kapena mbalame zamumlengalenga ndipo zidzakuwuza;
8 ask the earth and it will teach you, and the fishes in the sea will tell you.
kapena uyankhule ndi dziko lapansi ndipo lidzakuphunzitsa, kapena ulole nsomba zamʼnyanja kuti zikufotokozere.
9 Which of all these doesn't know that the Lord has done this?
Kodi mwa zonsezi ndi chiti chimene sichidziwa kuti lachita zimenezi ndi dzanja la Yehova?
10 He gives life to every living thing, life to all humankind.
Mʼmanja mwake ndi mʼmene muli moyo wa cholengedwa chilichonse, ndiponso moyo wa anthu a mitundu yonse.
11 The ear distinguishes words just like the palate distinguishes foods.
Kodi khutu sindiye limene limamva mawu monga mmene lilime limalawira chakudya?
12 Wisdom to distinguish belongs to the old, and the ability to rightly discriminate belongs to those with long experience.
Kodi nzeru sipezeka pakati pa anthu okalamba? Kodi moyo wautali sumabweretsa nzeru zomvetsa zinthu?
13 God has wisdom and power, counsel and understanding belong to him.
“Kwa Mulungu ndiye kuli nzeru ndi mphamvu; uphungu ndi kumvetsa zinthu ndi zake.
14 If he tears something down, nobody can rebuild it. If he imprisons someone, nobody can free them.
Chimene Iye wapasula palibe angachimangenso. Akatsekera munthu mʼndende palibe angamutulutse.
15 If God holds back the waters, everything dries up; if he releases the waters, the earth floods.
Iyeyo akamanga mvula dziko limawuma; akamasula mvulayo, madzi amasefukira pa dziko.
16 He is mighty and victorious; both deceivers and those deceived are subject to him.
Kwa Iye kuli mphamvu ndi kupambana; munthu wopusitsidwa ndiponso wopusitsa onse ali mu ulamuliro wake.
17 He leads counselors away stripped of their wisdom, he makes judges into fools.
Iye amalanda aphungu nzeru zawo ndipo amapusitsa oweruza.
18 He removes the chains of office from kings and makes them wear loincloths.
Iye amachotsa zingwe zimene mafumu anawamanga nazo ndipo amawamanga lamba mʼchiwuno mwawo.
19 He leads priests away stripped of their religious garments, he overthrows the powerful.
Iye amasocheretsa ansembe atawalanda nzeru zawo ndipo amagonjetsa anthu amphamvu amene ndi okhazikika.
20 He takes away the advice of trusted advisors, he removes the discernment of the elders.
Iye amakhalitsa chete aphungu odalirika ndipo amalanda chidziwitso cha anthu akuluakulu.
21 He pours scorn upon princes and takes away power from the strong.
Iye amanyoza anthu otchuka ndipo anthu anyonga amawatha mphamvu.
22 He reveals what is hidden in darkness, and brings into the light the shadow of death.
Iye amatulutsira poyera zinthu zozama za mu mdima ndipo mdima wandiweyaniwo amawusandutsa kuwala.
23 He makes nations great and he destroys them; he expands nations and ruins them.
Iye amakuza mitundu ya anthu ndipo amayiwononganso; amachulukitsa mitundu ya anthu ndipo amayimwazanso.
24 He removes the understanding of rulers and makes them wander in the wilderness.
Iye amalanda nzeru za atsogoleri a dziko lapansi; amawayendetsa mʼthengo mopanda njira.
25 They grope around in the dark without a light. He makes them stagger like drunk people.
Iwo amafufuzafufuza njira mu mdima wopanda chowunikira; Iye amawayendetsa dzandidzandi ngati oledzera.

< Job 12 >