< Jeremiah 9 >
1 How I wish my head was a spring of water, and my eyes a fountain of tears! Then I would weep day and night over all my people who have been killed.
Aa, ndikanakonda kuti mutu wanga ukanakhala chitsime cha madzi, ndi maso anga ngati kasupe wa misozi! Ndikanalira usana ndi usiku kulirira anthu anga amene aphedwa.
2 I wish I had a temporary shelter in the desert—I would give up on my people and leave them, because they're all adulterers, a bunch of traitors!
Ndani adzandipatsa malo ogona mʼchipululu kuti ndiwasiye anthu anga ndi kuwachokera kupita kutali; pakuti onse ndi achigololo, ndiponso gulu la anthu onyenga.
3 Their words are like arrows shot from a bow. Lies win out over the truth throughout the country. They go from one evil thing to the next, forgetting all about me, declares the Lord.
“Amapinda lilime lawo ngati uta. Mʼdzikomo mwadzaza ndi mabodza okhaokha osati zoonadi. Amapitirirabe kuchita zoyipa; ndipo sandidziwa Ine.” Akutero Yehova.
4 Everyone, watch out for your friends! Don't even trust your brother! Every brother is deceitful, and every friend slanders other people.
“Aliyense achenjere ndi abwenzi ake; asadalire ngakhale abale ake. Aliyense amafuna kumudyera mʼbale wake masuku pa mutu. Choncho aliyense amachitira bwenzi lake ugogodi.
5 Everyone betrays their friends; no one tells the truth. They've made themselves into expert liars; they tire themselves out doing wrong.
Aliyense amamunamiza mʼbale wake ndipo palibe amene amayankhula choonadi. Anapazoloweza pakamwa pawo kunena zabodza; amalimbika kuchita machimo.
6 Everyone exploits each other, and in all their lies they don't want to know me, declares the Lord.
Iwe wakhalira mʼchinyengo ndipo ukukana kundidziwa Ine,” akutero Yehova.
7 So this is what the Lord Almighty says: Look, I'm going to test them and purify them like metal in a furnace. What else can I do because of what my people have done?
Nʼchifukwa chake Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Taonani, Ine ndidzawasungunula ngati chitsulo ndi kuwayesa. Kodi ndingachite nawonso bwanji chifukwa cha machimo awo?
8 Their words are arrows that kill; they always tell lies. They're nice to their friends on the outside while plotting against them inside.
Lilime lawo lili ngati muvi wakuthwa; limayankhula zachinyengo. Aliyense ndi pakamwa pake amayankhula mawu achikondi kwa mnansi wake, koma mu mtima mwake amakonzekera zomuchita chiwembu.
9 Shouldn't I punish them for all this? declares the Lord. Shouldn't I retaliate for what this nation has done?
Kodi ndilekerenji kuwalanga chifukwa cha zimenezi? akutero Yehova. ‘Kodi ndisawulipsire mtundu wotere wa anthu?’”
10 I will weep and wail for the mountains, I will sing a funeral song over the pastures in the countryside, because they have been so badly burned that no one can pass through, and there are no cattle to make any noise. The birds have flown and the wild animals have run away.
Ndidzakhetsa misozi ndi kulira kwamphamvu chifukwa cha mapiri ndipo ndidzadandaula chifukwa cha msipu wa ku chipululu. Malo onsewo awonongeka ndipo palibe amene amapitako, ndipo sikumveka kulira kwa ngʼombe. Mbalame zamlengalenga zathawa ndipo nyama zakuthengo zachokako.
11 I'm going to make Jerusalem into a heap of rubble, a place where jackals live. I will destroy the towns of Judah, leaving them empty.
Ndipo Yehova anati, “Ndidzasandutsa Yerusalemu kukhala bwinja, malo okhalamo ankhandwe; ndipo ndidzawononga mizinda ya Yuda kotero kuti palibe munthu amene adzakhalemo.”
12 Who is wise enough to understand this? Has the Lord told anyone so they can explain what's happened? Why has the land been destroyed and burned so it's like a desert, so no one can pass through it?
Ine ndinati, “Kodi munthu wanzeru ndani woti nʼkumvetsa zimenezi? Kodi ndani amene Yehova anayankhula naye zimenezi kuti akafotokozere ena? Nʼchifukwa chiyani dziko lawonongeka ndi kusanduka chipululu, mʼmene anthu sadutsamo?”
13 The Lord replied, It's because they have given up keeping my laws that I placed before them. They haven't followed them; they haven't done what I told them.
Yehova anati, “Nʼchifukwa chakuti anthuwa analeka kutsata malamulo anga amene ndinawapatsa; sanandimvere kapena kuwasamala.
14 On the contrary, they have followed their own stubborn way of thinking, and went to worship the Baals, just as their forefathers taught them.
Mʼmalo mwake, anatsatira zolakwa za mʼmitima yawo; anapembedza Abaala ngati momwe makolo awo anawaphunzitsira.”
15 So this is what the Lord Almighty, the God of Israel, says: Watch out! I will give these people wormwood to eat and poisoned water to drink.
Tsono chimene Ine Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli ndidzachite ndi anthu amenewa ndi ichi: “Ndidzawadyetsa chakudya cha ziphe ndi kuwamwetsa madzi a ndulu.
16 I'm about to scatter them among nations unfamiliar to them and their forefathers, and I will send enemies with swords to chase after them until I have wiped them out.
Ndidzawabalalitsa pakati pa mitundu ya anthu imene iwowo kapena makolo awo sanayidziwe, ndipo ndidzawalondola ndi ankhondo mpaka nditawawononga.”
17 This is what the Lord Almighty says: Be aware of what's happening! Call for the professional women mourners, ask for the best of them.
Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Tsopano ganizirani! Muyitane akazi olira mwachisoni kuti abwere; itanani akazi odziwa kulira bwino.”
18 Have them come as quickly as possible, and sing a funeral song about us, so we can cry our eyes out, so our tears will flow like streams.
Anthu akuti, “Abwere mofulumira kuti adzatilire mpaka mʼmaso mwathu mutatuluka misozi ndi kuti msidze zathu zinyowe ndi madzi.
19 The sound of weeping comes from Zion, “We're completely devastated! We're totally ashamed, because we've had to abandon our country, because our houses have been demolished.”
Kulira mwachisoni kukumveka kuchokera mu Ziyoni akuti, ‘Aa! Ife tawonongeka! Tachita manyazi kwambiri! Tiyenera kuchoka mʼdziko lathu chifukwa atipirikitsa mʼnyumba zathu.’”
20 Women, listen to the Lord's message, hear what he has to say. Teach your daughters to mourn and sing songs of sadness.
Tsono inu amayi, imvani mawu a Yehova; tcherani makutu anu kuti mumve mawu a Yehova. Phunzitsani ana anu aakazi kulira mwachisoni; aliyense aphunzitse mnzake nyimbo ya maliro.
21 Death has slipped in through our windows; it has come into our fortresses. It has killed the children playing in the streets and the young people gathering in the town squares.
Imfa yatifikira kudzera mʼmazenera athu ndipo yalowa mʼnyumba zathu zotetezedwa; yapha ana athu mʼmisewu, ndi achinyamata athu mʼmabwalo.
22 Tell everyone this is what the Lord says: Dead bodies will be left where they fall like manure in the fields, lying there like stalks of freshly-cut grain behind the reaper, with no one to collect them.
Yehova anandiwuza kuti ndinene izi kuti, “‘Mitembo ya anthu idzakhala ili lambalamba ngati ndowe mʼminda, ngati mapesi mʼmbuyo mwa wokolola, popanda munthu woyitola.’”
23 This is what the Lord says: The wise shouldn't boast about their wisdom. The strong shouldn't boast about their strength. The rich shouldn't boast about their riches.
Yehova akuti, “Munthu wanzeru asanyadire nzeru zake, kapena munthu wamphamvu kunyadira nyonga zake, kapena munthu wolemera kunyadira chuma chake,
24 Anyone who wants to boast should boast that they really know and understand me, recognizing that I am the Lord who acts with trustworthy love, who shows fairness, and who does what is right everywhere on earth, because these mean the most to me, declares the Lord.
koma ngati munthu akufuna kunyadira, anyadire chinthu ichi: kuti iye amamvetsa za Ine ndipo amandidziwa, kuti ndine Yehova, amene ndimakonda chifundo, chilungamo ndiponso ungwiro pa dziko lapansi. Zimenezi ndizo ndimakondwera nazo,” akutero Yehova.
25 Watch out, for the time is coming, declares the Lord, when I will punish all who are only physically circumcised.
“Nthawi ikubwera,” akutero Yehova, “pamene ndidzalanga onse amene anachita mdulidwe koma mu mtima sasamala nʼkomwe.
26 Egypt, Judah, Edom, Ammon, Moab, and all the desert people who trim their hair on the sides of their heads—all these nations are uncircumcised, and all the Israelites are spiritually uncircumcised.
Ndidzalanga anthu a ku Igupto, Yuda, Edomu, Amoni, Mowabu, ndiponso onse amene amakhala kutali ku chipululu. Mitundu ina yonseyi ndi yosachita mdulidwe, ngakhalenso Aisraeli nawonso sanachite mdulidwe wa mu mtima.”