< Jeremiah 7 >

1 This is the Lord's message that came to Jeremiah from the Lord:
Mawu amene Yehova anayankhula kwa Yeremiya ndi awa,
2 Go and stand in the entrance to the Lord's Temple, and deliver this message: Listen to what Lord has to say, all of you from Judah who are coming in through these gates to worship the Lord.
“Ima pa chipata cha Nyumba ya Yehova ndipo kumeneko ukalalikire uthenga uwu: “‘Imvani mawu a Yehova, inu nonse anthu a ku Yuda amene mumalowa pa chipata ichi kudzapembedza Yehova.
3 This is what the Lord Almighty, the God of Israel says: Change your ways and do what's right, and I'll let you go on living here.
Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli akuti: Konzani makhalidwe anu ndi zochita zanu, ndipo ndidzakulolani kukhala pa malo ano.
4 Don't believe in those who try and deceive you by repeating, “The Temple of the Lord is here, the Temple of the Lord is here, the Temple of the Lord is here.”
Musamakhulupirire mawu anu achinyengo onena kuti, ‘Ino ndi Nyumba ya Yehova, Nyumba ya Yehova, Nyumba ya Yehova!’
5 If you sincerely change your ways and do what's right, if you treat each other fairly,
Ngati mutasinthadi makhalidwe anu ndi zochita zanu, ndi kumachitirana zolungama,
6 if you stop mistreating foreigners and orphans and widows, and if you stop murdering innocent people and stop hurting yourselves by worshiping,
ngati mutaleka kuzunza mlendo, ana amasiye kapena akazi amasiye ndi kuleka kupha anthu osalakwa pa malo ano, ndipo ngati muleka kutsatira milungu ina, kuti ingakuwonongeni,
7 then I'll let you go on living here in the country that I gave to your forefathers forever and ever.
Ine ndidzakulolani kukhala pa malo ano, mʼdziko limene ndinapatsa makolo anu mpaka muyaya.
8 But look at you! You go on believing in these deceptions, these worthless words.
Koma onani, inu mukudalira mawu abodza amene alibe phindu.
9 Are you really going to continue stealing, murdering, committing adultery, and lying, burning incense to Baal, and worshiping other gods that you know nothing about,
“Kodi inu muziba ndi kupha, kuchita chigololo ndi kulumbira monama, kufukiza lubani kwa Baala ndi kutsatira milungu ina imene simunayidziwe,
10 and then come and stand before me in my own Temple and say, “We're safe, so we can continue doing all these offensive things”?
ndipo kenaka nʼkubwera kudzayima pamaso panga mʼNyumba ino, Nyumba imene imadziwika ndi Dzina langa, inu nʼkumati, ‘Tapulumuka.’ Mwapulumuka kuti muzichitabe zonyansazi?
11 Do you see this house, my own Temple, as a den of thieves? Well, that's what it looks like to me too, declares the Lord.
Kodi Nyumba ino imene imadziwika ndi Dzina langa, yasanduka phanga la anthu olanda zinthu anzawo mwachifwamba inu mukuona? Komatu ndakhala ndi kuziona zonsezi! akutero Yehova.”
12 So why don't you go to Shiloh where I first made myself a place for me to live with you, and see what I did to it because of the evil my people Israel did?
“‘Pitani tsopano ku malo anga ku Silo, malo amene poyamba ankadziwika ndi Dzina langa, ndipo mukaone zimene ndinachita kumeneko chifukwa cha kuyipa kwa anthu anga Aisraeli.
13 I've warned you time and again about all these things you've done but you've refused to listen, declares the Lord. I've called out to you but you didn't want to answer me.
Tsono popeza munkachita zonsezi, ngakhale Ine kukuyankhulani koma inu osamvera, kukuyitanani koma inu osayankha,
14 So now I'm going to do to my Temple, what I did to Shiloh. This is the Temple your put your faith in, the place I gave to you and your forefathers.
choncho ndidzachita pa Nyumba imene imadziwika ndi Dzina langayi, Nyumba ya Yehova imene mumayidalira, malo amene ndinapereka kwa inu ndi makolo anu, zomwe ndinachita ku Silo.
15 I will throw you out of my presence, just as I expelled all your Israelite relatives, all the descendants of Ephraim.
Ndidzakuthamangitsani pamaso panga, ngati momwe ndinachitira abale anu onse, anthu a Efereimu.’”
16 You, Jeremiah, are not to pray for these people. Don't cry out to me in prayer for them, don't plead with me on their behalf, because I won't listen to you.
“Choncho iwe Yeremiya usawapempherere anthu awa ngakhale kuwapepesera kapenanso kuwapembedzera; usandidandaulire, chifukwa Ine sindidzakumvera.
17 Can't you see how they're behaving in the towns of Judah and in the streets of Jerusalem?
Kodi sukuona zimene akuchita mʼmizinda ya ku Yuda ndi mʼmisewu ya ku Yerusalemu?
18 The children collect the firewood, the fathers light the fire, and the women knead the dough to make cakes for the Queen of Heaven, and they pour out drink offerings to other gods to make me angry and hurt.
Ana akutorera nkhuni, abambo akusonkha moto, ndipo amayi akukanda ufa kuti aphike makeke oti akapereke nsembe kwa mfumukazi yazakumwamba. Iwo amathira nsembe ya zakumwa kwa milungu ina kuti andipsetse mtima.
19 But is it really me they're hurting? declares the Lord. Aren't they really hurting themselves and bringing shame on themselves?
Koma kodi akuvutitsa Ine? Kodi sakungodzivuta okha, ndi kudzichititsa manyazi? akutero Yehova.”
20 So this is what the Lord God says: Watch! My furious anger and will be poured out on this country, on people and animals, on the orchards and the crops in the field. It will burn and nobody will be able to put it out.
“Nʼchifukwa chake Ambuye Yehova akuti: Ndidzatsanulira mkwiyo wanga pa Nyumba yangayi, anthu, nyama, mitengo ndi zipatso zomwe. Mkwiyowo udzakhala ngati moto wosazimitsika.
21 This is what the Lord Almighty, the God of Israel, says: You can add your burnt offerings to your other sacrifices and eat all the meat yourselves!
“Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli akuti: Wonjezerani nsembe zanu zopsereza pa nsembe zanu zinazo ndipo mudye nyama yakeyo!
22 When I led your forefathers out of Egypt I didn't just give them instructions about burnt offerings and sacrifices,
Pakuti pamene ndinatulutsa makolo anu ku Igupto ndi kuyankhula nawo, sindinawalamulire kuti azipereka nsembe zopsereza kapena nsembe zinazo,
23 This is the commandment I gave them: Obey me, and I will be your God, and you will be my people. Follow everything I have commanded you to do, so that all will go well for you.
koma ndinawalamula kuti: Mverani Ine, ndipo ndidzakhala Mulungu wanu ndipo inu mudzakhala anthu anga. Muzitsata zonse zimene ndakulamulirani, ndipo zinthu zidzakuyenderani bwino.
24 But they refused to listen or pay attention. Instead they followed the desires of their own stubborn and evil thinking, so they ended up going backward and not forward.
Koma anthuwo sanamvere kapena kulabadira; mʼmalo mwake anapitirira kusamvera ndi mitima yawo yoyipa. Iwo anabwerera mʼmbuyo mʼmalo mopita patsogolo.
25 From the time your forefathers left Egypt until now, I have sent you time after time my servants the prophets.
Kuyambira tsiku limene makolo awo anachoka ku Igupto mpaka lero lino, ndakhala ndikuwatumizira atumiki anga, aneneri.
26 But you refused to listen or pay them attention. Instead, you became more stubborn and rebellious than your forefathers!
Koma anthuwo sanandimvere kapena kusamalira. Anawumitsa mitima yawo ndi kuchita zoyipa kuposa makolo awo.
27 When you tell them all this, they won't listen to you. When you call out to them, they won't answer.
“Ngakhale iwe uwawuze zonsezi koma sadzakumvera. Ngakhale uwayitane koma sadzakuyankha.
28 So you have to tell them, “This is the nation that refused to listen to what the Lord their God said, and would not accept the Lord's discipline. Truth has died out; people don't even talk about it.
Nʼchifukwa chake udzawawuze kuti, ‘Uwu ndi mtundu wa anthu umene sunamvere Yehova Mulungu wake, wosalola kulangizidwa. Choonadi chatha; chazimirira pa milomo yawo.’
29 Cut off your hair and throw it away. Sing a song of mourning on the bare hills, for the Lord has rejected and abandoned the generation who made him angry.”
“Tsono meta tsitsi lako ndi kulitaya. Ulire kwambiri pa zitunda zopanda zomera, pakuti Yehova waukana ndi kuwusiya mʼbado umene wamukwiyitsawu.”
30 For the people of Judah have done what is evil in my sight, declares the Lord. They have placed their offensive idols in my own Temple, making it unclean.
“Anthu a ku Yuda achita zoyipa pamaso panga, akutero Yehova. Ayimika mafano awo onyansa mʼnyumba imene imadziwika ndi Dzina langa ndipo ayipitsa.
31 They have built pagan shrines at Topheth in the Valley of Hinnom so they could sacrifice their sons and daughters by burning them in the fire. This is something I never commanded. I never even thought of such a thing!
Amanga nsanja yopembedzera Tofeti mʼChigwa cha Hinomu kuti apserezereko ana awo aamuna ndi aakazi. Zimenezi Ine sindinawalamulire ngakhale kuziganizira nʼkomwe.
32 So watch out! The time is coming, declares the Lord, when instead of Topheth and the Valley of Hinnom this place will be called the Valley of Killing. People will bury their dead in Topheth until it's full.
Nʼchifukwa chake masiku akubwera, akutero Yehova, pamene anthu sadzawatchulanso malowo Tofeti kapena Chigwa cha Hinomu, koma adzawatchula Chigwa cha Imfa, chifukwa adzakwirira anthu akufa ku Tofeti mpaka osapezekanso malo owayika.
33 The dead bodies of these people will be food for birds of prey and wild animals, and there won't be anyone to scare them away.
Ndipo mitembo ya anthu amenewa idzakhala chakudya cha mbalame zamlengalenga ndi zirombo zakuthengo, ndipo palibe wina amene adzazipirikitse.
34 I will put a stop to the cheerful sounds of celebration and the happy voices of the bride and bridegroom from the cities of Judah and the streets of Jerusalem, for the country will be turned into a wasteland.
Ndidzathetsa nyimbo zonse zachisangalalo ndi zachikondwerero mʼmizinda ya ku Yuda ndi mʼmisewu ya ku Yerusalemu. Sikudzamvekanso mawu a chikondwerero a mkwatibwi ndi mkwati pakuti dzikolo lidzasanduka chipululu.”

< Jeremiah 7 >