< Jeremiah 46 >
1 In the fourth year of the reign of Jehoiakim the son of Josiah king of Judah, the Lord's message that came to Jeremiah the prophet about foreign nations.
Yehova anamupatsa Yeremiya uthenga wonena za anthu a mitundu ina.
2 This concerns Pharaoh Neco king of Egypt and the Egyptian army which was defeated at Carchemish on the Euphrates River by Nebuchadnezzar king of Babylon.
Kunena za Igupto: Yehova ananena za gulu lankhondo la Farao Neko mfumu ya ku Igupto limene Nebukadinezara mfumu ya ku Babuloni analigonjetsa ku Karikemesi ku mtsinje wa Yufurate mʼchaka cha chinayi cha Yehoyakimu mwana wa Yosiya mfumu ya Yuda,
3 Pick up both your small and large shields, and advance ready for battle!
anati, “Konzani zishango zanu ndi malihawo, ndipo yambanipo kupita ku nkhondo!
4 Put the harnesses on the horses and get into your chariots; take your positions with your helmets on! Sharpen your spears; put on your armor!
Mangani akavalo, ndipo kwerani inu okwerapo! Khalani pa mzere mutavala zipewa! Nolani mikondo yanu, valani malaya anu ankhondo!
5 Why do I see their lines broken and retreating? Their soldiers are defeated. They run away so quickly they don't even look back because they're so terrified by what's happening around them, declares the Lord.
Yeremiya anati: Kodi ndikuona chiyani? Achita mantha akubwerera, ankhondo awo agonjetsedwa. Akuthawa mofulumirapo osayangʼananso mʼmbuyo, ndipo agwidwa ndi mantha ponseponse,” akutero Yehova.
6 Even the fastest of them can't get away; the soldiers can't escape. There in the north beside the Euphrates they fall and die.
Waliwiro sangathe kuthawa ngakhale wankhondo wamphamvu sangathe kupulumuka. Akunka napunthwa ndi kugwa kumpoto kwa mtsinje wa Yufurate.
7 Who is this that's coming, rising like the Nile, like swirling rivers whose waters flood?
“Kodi ndani amene akukwera ngati Nailo, ngati mtsinje wa madzi amkokomo?
8 Egypt is rising like the Nile; its waters swirl like flooding rivers, boasting, “I will rise and sweep over the earth; I will destroy towns and the people in them.”
Igupto akusefukira ngati Nailo, ngati mitsinje ya madzi amkokomo. Iye akunena kuti, ‘Ndidzadzuka ndi kuphimba dziko lapansi; ndidzawononga mizinda ndi anthu ake.’
9 Horses, charge in! Chariots, drive like crazy! Have the infantry advance: soldiers from Ethiopia and Put carrying their shields, archers from Lydia with their bows.
Tiyeni, inu akavalo! Thamangani inu magaleta! Tulukani, inu ankhondo, ankhondo a ku Kusi ndi Puti amene mumanyamula zishango, ankhondo a ku Ludi amene mumaponya uta.
10 But this is the day of the Lord God Almighty, a day of retribution when he takes vengeance on his enemies. The sword will destroy until it is satisfied, until it's had enough of their blood. The Lord God Almighty is having a sacrifice in the north country beside the Euphrates.
Koma tsikulo ndi la Ambuye Yehova Wamphamvuzonse; tsiku lolipsira, lolipsira adani ake. Lupanga lake lidzawononga ndi kukhuta magazi, lidzaledzera ndi magazi. Pakuti Yehova, Yehova Wamphamvuzonse, adzapereka adani ake ngati nsembe mʼdziko la kumpoto mʼmbali mwa mtsinje wa Yufurate.
11 Go and find some healing ointment in Gilead, Virgin Daughter of Egypt! But whatever you use to help you will fail, because there's nothing that will heal you.
“Pita ku Giliyadi ukatenge mankhwala iwe namwali Igupto. Wayesayesa mankhwala ambiri koma osachira; palibe mankhwala okuchiritsa.
12 The other nations have heard how you were humiliated in defeat. Everyone can hear your cries of pain. Soldiers fall over each other, and die together.
Anthu a mitundu ina amva za manyazi ako; kulira kwako kwadzaza dziko lapansi. Ankhondo akunka nagwetsanagwetsana, onse awiri agwa pansi limodzi.”
13 This is the message that the Lord gave to Jeremiah the prophet about the attack by Nebuchadnezzar king of Babylon on Egypt:
Uthenga umene Yehova anapatsa mneneri Yeremiya wonena za kubwera kwa Nebukadinezara mfumu ya ku Babuloni kudzathira nkhondo Igupto ndi uwu:
14 Shout a warning in Egypt! Tell everyone in Migdol, and in Memphis and Tahpanhes: Get ready to defend yourselves, because war is destroying everything around you.
“Mulengeze ku Igupto. Mulengeze ku Migidoli. Mulengezenso ku Mefisi ndi ku Tapanesi. Muwawuze anthu akumeneko kuti, ‘Imani pamalo panu ndi kukhala okonzeka kudziteteza, chifukwa lupanga lidzawononga zonse zimene muli nazo.’
15 Why did Apis your bull god run away? He couldn't stand his ground because the Lord has knocked him down.
Chifukwa chiyani mulungu wanu wamphamvu uja Apisi wathawa? Iye sakanatha kulimba chifukwa Yehova anamugwetsa.
16 Many soldiers trip and fall over one another and say, “Come on! Let's get back home to our people where we were born, otherwise we're going to be killed.”
Ankhondo anu apunthwa ndi kugwa. Aliyense akuwuza mnzake kuti, ‘Tiyeni tibwerere kwathu, ku dziko kumene tinabadwira, tithawe lupanga la adani athu.’
17 When they get there they'll say about Pharaoh king of Egypt, “He just makes a lot of noise. He wasted his opportunity.”
Kumeneku iwo adzafuwula kuti, ‘Farao, mfumu ya ku Igupto mupatseni dzina lakuti, Waphokoso, Wotaya mwayi wake.’
18 As I live, declares the King who has the name “the Lord Almighty,” the king of Babylon will come. He is like Mount Tabor that stands out from the other mountains, like Mount Carmel high above the sea.
“Pali Ine wamoyo,” ikutero Mfumu, imene dzina lake ndi Yehova Wamphamvuzonse, “wina adzabwera amene ali ngati Tabori phiri lopambana mapiri ena, ngati phiri la Karimeli loti njoo mʼmbali mwa nyanja.
19 Pack your bags ready for exile, daughter living in Egypt! Memphis is going to be destroyed, an empty place where no one lives.
Konzani katundu wanu wopita naye ku ukapolo inu anthu a ku Igupto, pakuti Mefisi adzasanduka chipululu ndipo adzakhala bwinja mopanda wokhalamo.
20 Egypt is a beautiful young cow, but a stinging insect from the north is coming to attack her.
“Igupto ali ngati mwana wangʼombe wokongola, koma chimphanga chikubwera kuchokera kumpoto kudzalimbana naye.
21 The soldiers that Egypt hired are like calves made fat for slaughter. They will also retreat. They won't stand and fight—they will all run away. Their day of destruction is coming; the time when they'll be punished.
Ngakhale ankhondo aganyu amene ali naye ali ngati ana angʼombe onenepa. Nawonso abwerera mʼmbuyo, nathawa pamodzi. Palibe amene wachirimika. Ndithu, tsiku la tsoka lawafikira; ndiyo nthawi yowalanga.
22 The Egyptians will retreat with a rustle like a snake sliding away, because the enemy will attack them with axes, coming at them like wood-cutters chopping down trees.
Aigupto akuthawa ndi liwu lawo lili ngati la njoka yothawa pamene adani abwera ndi zida zawo, abwera ndi nkhwangwa ngati anthu odula mitengo.
23 They will cut them down like a thick forest, declares the Lord, because the invaders are like a swarm of locusts—there's so many of them that they can't be counted.
Iwo adzadula nkhalango ya Igupto,” akutero Yehova, “ngakhale kuti ndi yowirira. Anthuwo ndi ochuluka kupambana dzombe, moti sangatheke kuwerengeka.
24 The people of Egypt will be humiliated. They will be handed over to the people of the north.
Anthu a ku Igupto achita manyazi atengedwa ukapolo ndi anthu a kumpoto.”
25 The Lord Almighty, the God of Israel, says: Watch, because I will punish Amon, the god of Thebes, and Pharaoh. I will punish the people of Egypt with their gods and kings, and everyone who trusts in Pharaoh.
Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli, akunena kuti, “Ndili pafupi kulanga Amoni mulungu wa Tebesi. Ndidzalanganso Farao ndi Igupto pamodzi ndi milungu yake yonse, mafumu ake ndi onse amene amamukhulupirira.
26 I'm going to hand them over to those who want to kill them, to Nebuchadnezzar king of Babylon and his officers. But after all this happens, people will live in Egypt as they used to, declares the Lord.
Ndidzawapereka kwa amene akufuna kuwapha, ndiye kuti kwa Nebukadinezara mfumu ya ku Babuloni ndi atsogoleri ake ankhondo. Komabe, mʼtsogolomo Igupto adzakhalanso ndi anthu monga kale,” akutero Yehova.
27 But you, descendants of Jacob my servant, you don't have to be fearful. Israelites, you don't need to be discouraged. I promise to rescue you from your distant places of exile, your descendants from the countries where they're being held captive. You will go home to a quiet and comfortable life, free from any threats.
“Iwe mtumiki wanga Yakobo, usachite mantha; usataye mtima, iwe Israeli. Ndithu Ine ndidzakupulumutsa kuchokera ku mayiko akutali, ndidzapulumutsanso zidzukulu zako kuchokera ku mayiko kumene anapita nazo ku ukapolo. Yakobo adzabwerera ndipo adzakhala motakasuka ndi pa mtendere, ndipo palibenso wina amene adzamuopsa.
28 You descendants of Jacob, don't be afraid! declares the Lord, for I will be with you. I will completely destroy all the nations where I've scattered you, I won't completely destroy you. However, I will discipline you as you deserve, and you can be sure I won't leave you unpunished.
Iwe mtumiki wanga Yakobo, usachite mantha, pakuti Ine ndili nawe,” akutero Yehova. “Ndidzawonongeratu mitundu yonse ya anthu a ku mayiko kumene ndakupirikitsira, Koma iwe sindidzakuwononga kotheratu. Ndidzakulanga iwe ndithu koma moyenerera; sindidzakulekerera osakulanga.”