< Jeremiah 38 >

1 Shephatiah son of Mattan, Gedaliah son of Pashhur, Jucal son of Shelemiah, and Pashhur son of Malchijah heard what Jeremiah was telling everyone:
Sefatiya mwana wa Matani, Gedaliya mwana wa Pasi-Huri, Yukali mwana wa Selemiya, ndi Pasi-Huri mwana wa Malikiya anamva zimene Yeremiya ankawuza anthu onse kuti,
2 This is what the Lord says: Anyone who remains in this city will die from war and famine and disease, but anyone who goes over to the Babylonians will live. Their reward will be to save their lives.
“Yehova akuti, ‘Aliyense amene akhale mu mzinda muno adzafa ndi nkhondo njala kapena mliri. Koma aliyense amene atatuluke kukadzipereka kwa Ababuloni adzapulumutsa moyo wake; iyeyo adzakhala ndi moyo.
3 This is what the Lord says: Be sure of this—Jerusalem will be handed over to the army of the king of Babylon. He is going to capture it.
Mzinda uno udzaperekedwa ndithu kwa gulu lankhondo la mfumu ya ku Babuloni, amene adzawulande.’”
4 The officers told the king, “This man deserves to die because he's demoralizing the defenders left in the city, and all the people too, by telling them this. This man isn't trying to help these people, he's only going to destroy them.”
Tsono akuluakuluwo anawuza mfumu kuti, “Munthu uyu ayenera kuphedwa. Iye akutayitsa mtima asilikali pamodzi ndi anthu onse amene atsala mu mzinda muno, chifukwa cha zimene akuwawuza. Munthu ameneyu sakufunira zabwino anthuwa koma chiwonongeko chawo.”
5 “Well, you can do whatever you want to him,” King Zedekiah replied. “I can't stop you.”
Mfumu Zedekiya anayankha kuti, “Munthuyu ali mʼmanja mwanu. Ine sindingakuletseni chimene mukufuna kumuchitira.”
6 So they took Jeremiah and put him in the cistern belonging to Malchiah, the king's son, which was in the guard's courtyard. They lowered Jeremiah down with ropes into the cistern. It didn't have any water, only mud, and Jeremiah sank into the mud.
Choncho iwo anatenga Yeremiya nakamuponya mʼchitsime cha Malikiya, mwana wa mfumu, chimene chinali mʼbwalo la alonda. Iwo anamutsitsira mʼdzenjemo ndi chingwe. Munalibe madzi koma matope okhaokha, ndipo Yeremiya anamira mʼmatopewo.
7 Ebed-melech the Cushite, a royal official in the king's palace, found out that they had put Jeremiah in the cistern. The king was sitting at the Benjamin Gate,
Koma Ebedi-Meleki, Mkusi, mmodzi mwa anthu ofulidwa ogwira ntchito mʼnyumba ya mfumu, anamva kuti Yeremiya anamuponya mʼchitsime. Nthawi imeneyo nʼkuti mfumu ili ku chipata cha Benjamini.
8 so Ebed-melech left the palace and went to talk to the king
Ebedi-Meleki anatuluka ku nyumba ya mfumu kukayiwuza kuti,
9 “My lord the king, all these terrible things these men have done to Jeremiah the prophet are evil. They've put him in the cistern, and he'll starve to death there because there's no more bread left in the city.”
“Mbuye wanga mfumu, zimene anthu awa amuchitira mneneri Yeremiya ndi zoyipa kwambiri. Iwo amuponya mʼchitsime, ndipo adzafa ndi njala chifukwa buledi watha mu mzinda muno.”
10 So the king gave the order to Ebed-melech the Cushite, “Take thirty men with you and go and pull Jeremiah the prophet out of the cistern before he dies.”
Tsono mfumu inalamula Ebedi-Meleki, Mkusi, kuti, “Tenga anthu makumi atatu, ndipo mukamutulutse mʼchitsimemo mneneri Yeremiya asanafe.”
11 Ebed-melech took the men and went to the storehouse under the palace. He took some rags and old clothes from there and then went to the cistern where he lowered them with ropes to Jeremiah.
Pamenepo Ebedi-Meleki anatenga anthuwo, napita nawo ku nyumba ya mfumu ya pansi pa chipinda chosungiramo chuma. Kumeneko anakatengako sanza ndipo anatsitsira sanzazo ndi chingwe mʼchitsime mʼmene munali Yeremiya.
12 Ebed-melech the Cushite called down to Jeremiah, “Put these rags and old clothes under your arms to protect you from the ropes.” Jeremiah did so,
Ebedi-Meleki, Mkusi, anawuza Yeremiya kuti, “Ika sanzazo mkwapa mwako kuti zingwe zingakupweteke.” Yeremiya anachitadi zimenezi,
13 and using the ropes they pulled him up and took him out of the cistern. Jeremiah stayed there in the guard's courtyard.
ndipo anamukoka ndi zingwe ndi kumutulutsa mʼchitsimecho. Ndipo Yeremiya anakhalabe ku bwalo la alonda.
14 Then King Zedekiah sent for Jeremiah the prophet and met him at the third Temple entrance. “I need to ask you something,” the king told Jeremiah. “You mustn't hide anything from me.”
Tsiku lina Mfumu Zedekiya anayitana mneneri Yeremiya ndipo anabwera naye ku chipata chachitatu cha Nyumba ya Yehova. Mfumu inawuza Yeremiya kuti, “Ndikufuna kukufunsa kanthu kena, ndipo usandibisire chilichonse.”
15 “If I tell you then you'll definitely have me killed,” Jeremiah replied. “Even if I were to give you advice, you wouldn't listen to me anyway.”
Yeremiya anati kwa Zedekiya, “Ndikakuyankhani, kodi simundipha? Ngakhaletu ine nditakulangizani, inu simudzandimvera.”
16 King Zedekiah solemnly promised Jeremiah in private, “As the Lord lives, who gave us this life, I won't have you killed, and I won't hand you over to those who want to kill you.”
Koma Mfumu Zedekiya mwachinsinsi inalumbira kwa Yeremiya kuti, “Pali Yehova wamoyo, amene amatipatsa moyo, sindidzakupha ngakhalenso kukupereka kwa amene akufuna kukuphawa.”
17 Then Jeremiah told Zedekiah, “This is what the Lord God Almighty, the God of Israel, says: ‘If you hand yourself over to the officers of the king of Babylon, then you'll live. Jerusalem won't be burned down, and you and your family will survive.
Pamenepo Yeremiya anati kwa Zedekiya, “Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli akuti, ‘Ngati mutuluka kukadzipereka kwa ankhondo a mfumu ya ku Babuloni, mudzakhala ndi moyo ndipo mzinda uno sadzawutentha, inu pamodzi ndi banja lanu mudzakhala ndi moyo.
18 But if you don't hand yourself over to the officers of the king of Babylon, then this city will be given to the Babylonians. They will burn it down, and you yourself won't escape being captured.”
Koma ngati simutuluka kukadzipereka kwa ankhondo a mfumu ya ku Babuloni, mzinda uno udzaperekedwa kwa Ababuloni ndipo adzawutentha; inuyo simudzapulumuka mʼdzanja mwawo.’”
19 But King Zedekiah said to Jeremiah, “I am afraid of the those people of Judah who have gone over to the Babylonians, because the Babylonians might hand me over the them so they could abuse me.”
Mfumu Zedekiya inati kwa Yeremiya, “Ine ndikuopa Ayuda amene anathawira kale kwa Ababuloni, pakuti mwina Ababuloniwo adzandipereka kwa Ayudawo ndipo iwowo adzandizunza.”
20 “They won't hand you over,” Jeremiah replied. “If you obey what the Lord says by doing what I tell you, then things will go well for you and you'll live.
Yeremiya anayankha kuti, “Ngati mumvera Yehova ndi kuchita zimene ndakuwuzani, ndiye kuti zinthu zidzakuyenderani bwino. Inu simudzaphedwa.
21 But if you refuse to hand yourself over, this is what the Lord has told me:
Koma mukakana kudzipereka, chimene Yehova wandiwululira ndi ichi:
22 All the women who are left in the palace of the king of Judah will be led out and handed over to the officials of the king of Babylon Those women will say: ‘Those good friends of yours! You were taken in by them and conquered by them. Your feet got stuck in the mid, so they abandoned you.’
Akazi onse amene atsala mʼnyumba ya mfumu ya Yuda adzaperekedwa kwa akuluakulu a mfumu ya ku Babuloni. Akazi amenewo adzakuwuzani kuti, “‘Abwenzi ako okhulupirika aja anakusokeretsa, ndipo anakugonjetsa. Poti tsopano miyendo yako yazama mʼmatope; abwenzi ako aja akusiya.’
23 All your wives and children will be handed over to the Chaldeans. And you yourself will not escape, for you will be captured by the king of Babylon, and Jerusalem will be burned down.”
“Akazi pamodzi ndi ana anu adzaperekedwa kwa Ababuloni. Inuyo simudzapulumuka mʼmanja mwawo koma mfumu ya ku Babuloni idzakugwirani; mzinda uno adzawutentha.”
24 Zedekiah warned Jeremiah, “Nobody can find out about this conversation, otherwise you'll die.
Pamenepo Zedekiya anati kwa Yeremiya, “Usawuze munthu wina aliyense zimene takambiranazi, ukatero udzaphedwa.
25 If the officers find out that I've talked with you, and they come and ask you, ‘Tell us what you and the king were talking about! Don't hide anything from us, or we'll kill you;’
Akuluakulu akamva kuti ndinayankhula nawe ndipo akabwera kwa iwe nʼkudzakufunsa kuti, ‘Tiwuze zimene unanena kwa mfumu ndi zimene mfumu inanena kwa iwe; usatibisire, ukatero tidzakupha,’
26 then you are to tell them, ‘I was asking the king to grant my request not to return me to the house of Jonathan to die there.’”
udzawawuze kuti, ‘Ine ndimapempha mfumu kuti isandibwezerenso ku nyumba ya Yonatani kuti ndikafere kumeneko.’”
27 When all the officers came to Jeremiah wanting to know, he repeated to them exactly what the king had told him to say. So they didn't ask him anything more because no one had heard what had been said.
Akuluakulu onse anabweradi kwa Yeremiya kudzamufunsa. Iye anawayankha monga momwe mfumu inamulamula. Choncho palibe amene ananenanso kanthu, pakuti palibe amene anamva zomwe anakambirana ndi mfumu.
28 Jeremiah remained there in the guard's courtyard until the day Jerusalem was captured.
Ndipo Yeremiya anakhalabe mʼbwalo la alonda mpaka tsiku limene mzinda wa Yerusalemu unalandidwa.

< Jeremiah 38 >