< Jeremiah 20 >

1 Pashhur, son of Immer, was a priest and the official in charge of the Lord's Temple. When he heard Jeremiah prophesying these things,
Wansembe Pasuri mwana wa Imeri, woyangʼanira wamkulu wa Nyumba ya Yehova, anamva Yeremiya akulosera zinthu zimenezi.
2 he beat Jeremiah the prophet and had him put in the stocks at the Upper Benjamin Gate, near to the Lord's Temple.
Tsono iye analamula kuti mneneri Yeremiyayo amenyedwe ndi kuyikidwa mʼndende pa Chipata chakumtunda kwa Benjamini ku Nyumba ya Yehova.
3 The following day, when Pashhur had Jeremiah released from the stocks, Jeremiah told him, “The Lord doesn't call you Pashhur (tear in pieces), but Magor-missabib (terror is everywhere).
Mmawa mwake, Pasuri anatulutsa Yeremiya mʼndende, ndipo Yeremiyayo anamuwuza kuti, “Pasuri, Yehova sadzakutchulanso dzina lako kuti Pasuri koma Zoopsa pa Mbali Zonse.
4 For this is what the Lord says: I'm going to make you terrified—you and all those you love. Enemies will kill them as you watch. I will hand Judah over to the king of Babylon. He will kill some, and the rest he will take away into exile in Babylon.
Pakuti Yehova akuti, ‘Ndidzakusandutsa choopsa kwa mwiniwakewe ndi kwa abwenzi ako onse; iweyo ukuona. Anthu a ku Yuda ndidzawapereka onse mʼmanja mwa mfumu ya ku Babuloni. Ena adzatengedwa ukapolo ku Babuloni ndipo ena adzaphedwa pa nkhondo.
5 I'm going to give it all away. All the wealth of this city, all the results of hard work, all the valuables, all the crown jewels of Judah's kings—I'm going to hand it over to their enemies, who will take it as plunder and carry it off to Babylon.
Ndidzapereka kwa adani awo chuma chonse cha mu mzinda uno, phindu lonse la ntchito yake, zinthu zake zonse za mtengowapatali ndiponso katundu yense wa mafumu a ku Yuda. Iwo adzazitenga monga zinthu zolanda ku nkhondo ndi kupita nazo ku Babuloni.
6 You, Pashhur, and everyone who lives with you, will go into captivity. You will go to Babylon. You will die there and be buried—you and all those you love, those to whom you prophesied lies.”
Ndipo iwe, Pasuri, pamodzi ndi onse a pa banja pako mudzapita ku ukapolo ku Babuloni. Mudzafera kumeneko ndi kuyikidwa mʼmanda, iweyo pamodzi ndi abwenzi ako amene unawalosera zabodza.’”
7 You fooled me, Lord, and I let myself be fooled! You're stronger than me—you've won! I've become a joke people laugh at all day long. Everyone is mocking me.
Inu Yehova, mwandinamiza, ndipo ndinapusadi; Inu ndi wamphamvu kuposa ine ndipo munandipambana. Anthu akundinyoza tsiku lonse. Aliyense akundiseka kosalekeza.
8 This is because every time I open my mouth I have to shout out warnings of violence and destruction. The Lord's message has become the reason people criticize and ridicule me the whole time.
Nthawi iliyonse ndikamayankhula, ndimafuwula kunena kuti, ziwawa kuno! Tikuwonongeka! Mawu anu Yehova andisandutsa chinthu chonyozeka ndipo ndimachitidwa chipongwe tsiku lonse.
9 If I tell myself, “I won't talk about him anymore, I won't even mention his name,” then his message is like a fire trapped within me, burning me from the inside out. I'm getting tired of holding it in. I just can't win.
Koma ndikanena kuti, “Sindidzalalikiranso za Iye kapena kuyankhulanso mʼdzina lake,” mawu anu amayaka ngati moto mu mtima mwanga, amakhaladi ngati moto wotsekeredwa mʼmafupa anga. Ndapirira kusunga mawu anu mu mtima mwanga osawatulutsa, koma sindingathe kupirirabe.
10 I've heard many people gossiping: “He's the one who says, ‘terror is everywhere!’ He has to be reported! Report what he's doing!” All my good friends are waiting for me to slip up. “Maybe he'll make a mistake so we can defeat him and get our revenge on him,” they say.
Ndimamva anthu ambiri akunongʼona kuti, “Zoopsa ku mbali zonse! Kamunenezeni! Tiyeni tikamuneneze!” Onse amene anali abwenzi anga akuyembekezera kuti ndigwa pansi, akumanena kuti, “Mwina mwake adzanyengedwa; tidzamugwira ndi kulipsira pa iye.”
11 But the Lord stands beside me like a powerful warrior. So those who are attacking me will fall. They won't win! Because they're not successful they will be totally disgraced. Their shame won't ever be forgotten.
Koma Yehova ali nane, ndiye wankhondo wamphamvu. Nʼchifukwa chake ondizunza adzalephera ndipo sadzandipambana. Adzachita manyazi kwambiri chifukwa sadzapambana. Manyazi awo sadzayiwalika konse.
12 Lord Almighty, you know without question who is living right. You examine people's thoughts and feelings. So let me see your punishment fall on them, because I've trusted you to judge my case.
Inu Yehova Wamphamvuzonse, Inu amene mumayesa anthu molungama ndipo mupenya za mu mtima mwa munthu. Ndiloleni kuti ndione kuti mwalipsira adani anga popeza ndapereka mlandu wanga kwa Inu.
13 Sing to the Lord! Praise the Lord! For he saves the poor from the power of the wicked.
Imbirani Yehova! Mutamandeni Yehova! Iye amapulumutsa wosauka mʼmanja mwa anthu oyipa.
14 May the day I was born be cursed! May the day my mother gave birth to me never be blessed!
Litembereredwe tsiku limene ndinabadwa! Tsiku limene amayi anga anandibereka lisatamandidwe!
15 May the man be cursed who brought my father the news that made him really happy, saying, “You have a son.”
Wotembereredwa munthu amene anapita kukasangalatsa abambo anga ndi uthenga woti: “Kwabadwa mwana wamwamuna!”
16 May that man be like the towns that the Lord destroyed without mercy. May he hear shouts of alarm in the morning and war-cries at noon,
Munthu ameneyo akhale ngati mizinda imene Yehova anayiwononga mopanda chisoni. Amve mfuwu mmawa, phokoso la nkhondo masana.
17 because he should have killed me in the womb so that my mother would have been my grave, remaining pregnant forever.
Chifukwa sanandiphere mʼmimba, kuti amayi anga asanduke manda anga, mimba yawo ikhale yayikulu mpaka kalekale.
18 Why was I born only to see trouble and sadness, and to end my life in shame?
Kodi ndinabadwira mavuto ndi chisoni kuti moyo wanga ukhale wamanyazi wokhawokha?

< Jeremiah 20 >